Yesaya 51 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 51:1-23

Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni

1“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso

ndiponso amene mumafunafuna Yehova:

Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa

ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;

2taganizani za Abrahamu, kholo lanu,

ndi Sara, amene anakubalani.

Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,

koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.

3Yehova adzatonthozadi Ziyoni,

ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;

Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,

malo ake owuma ngati munda wa Yehova.

Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda

ndi kundiyamika.

4“Mverani Ine, anthu anga:

tcherani khutu, inu mtundu wanga:

malangizo adzachokera kwa Ine;

cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.

5Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.

Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;

ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.

Mayiko akutali akundiyembekezera.

Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.

6Kwezani maso anu mlengalenga,

yangʼanani pansi pa dziko;

mlengalenga udzazimirira ngati utsi,

dziko lapansi lidzatha ngati chovala

ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.

Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,

chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.

7“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,

anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;

musaope kudzudzulidwa ndi anthu

kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.

8Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;

mbozi idzawadya ngati thonje.

Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,

chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”

9Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,

Inu Yehova;

dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,

monga nthawi ya mibado yakale.

Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,

amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?

10Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,

madzi ozama kwambiri aja?

Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,

kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?

11Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera

nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;

chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.

Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,

chisoni ndi kubuwula zidzathawa.

12Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.

Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?

Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.

13Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,

amene anayala za mlengalenga

ndi kuyika maziko a dziko lapansi.

Inu nthawi zonse mumaopsezedwa

chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani

amene angofuna kukuwonongani.

Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?

14Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;

sadzalowa mʼmanda awo,

kapena kusowa chakudya.

15Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.

Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu

ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.

Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,

ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,

ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”

Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu

17Dzambatuka, dzambatuka!

Imirira iwe Yerusalemu.

Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo

chimene Yehova anakupatsa.

Iwe amene unagugudiza

chikho chochititsa chizwezwe.

18Mwa ana onse amene anabereka,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;

mwa ana onse amene analera,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.

19Mavuto awiriwa akugwera iwe.

Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.

Ndani angakumvere chisoni?

Ndani angakutonthoze?

20Ana ako akomoka;

ali lambalamba pa msewu,

ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.

Ukali wa Yehova

ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.

21Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,

iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.

22Ambuye Yehova wanu,

Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,

“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako

chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;

sudzamwanso chikho

cha ukali wanga.

23Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,

amene ankakuwuza kuti,

‘gona pansi tikuyende pa msana.’

Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,

ngati msewu woti ayendepo.”