Yesaya 50 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 50:1-11

Tchimo la Israeli, Kumvera kwa Mtumiki

1Yehova akuti,

“Kalata imene ndinasudzulira amayi

anu ili kuti?

Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole,

ndinakugulitsani kwa ati?

Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu;

amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.

2Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu?

Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha?

Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani?

Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani?

Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu,

mitsinje ndinayisandutsa chipululu;

nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi;

ndipo zinafa ndi ludzu.

3Ndinaphimba thambo ndi mdima

ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”

4Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula

kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka.

Mmawa mulimonse amandidzutsa,

amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.

5Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga,

ndipo sindinakhale munthu wowukira

ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.

6Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya

masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu;

sindinawabisire nkhope yanga

anthu ondinyoza ndi ondilavulira.

7Popeza Ambuye Yehova amandithandiza,

sindidzachita manyazi.

Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi,

chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.

8Wondikhalira kumbuyo ali pafupi,

ndaninso amene adzandiyimba mlandu?

Abwere kuti tionane maso ndi maso!

Mdani wanga ndi ndani?

Abweretu kuti tilimbane!

9Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza.

Ndaninso amene adzanditsutsa?

Onse adzatha ngati chovala

chodyedwa ndi njenjete.

10Ndani mwa inu amaopa Yehova

ndi kumvera mawu a mtumiki wake?

Aliyense woyenda mu mdima,

popanda chomuwunikira,

iye akhulupirire dzina la Yehova

ndi kudalira Mulungu wake.

11Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto

ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu,

lowani mʼmoto wanu womwewo.

Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa.

Ndipo ine Yehova

ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.

King James Version

Isaiah 50:1-11

1Thus saith the LORD, Where is the bill of your mother’s divorcement, whom I have put away? or which of my creditors is it to whom I have sold you? Behold, for your iniquities have ye sold yourselves, and for your transgressions is your mother put away. 2Wherefore, when I came, was there no man? when I called, was there none to answer? Is my hand shortened at all, that it cannot redeem? or have I no power to deliver? behold, at my rebuke I dry up the sea, I make the rivers a wilderness: their fish stinketh, because there is no water, and dieth for thirst. 3I clothe the heavens with blackness, and I make sackcloth their covering.

4The Lord GOD hath given me the tongue of the learned, that I should know how to speak a word in season to him that is weary: he wakeneth morning by morning, he wakeneth mine ear to hear as the learned.

5¶ The Lord GOD hath opened mine ear, and I was not rebellious, neither turned away back. 6I gave my back to the smiters, and my cheeks to them that plucked off the hair: I hid not my face from shame and spitting.

7¶ For the Lord GOD will help me; therefore shall I not be confounded: therefore have I set my face like a flint, and I know that I shall not be ashamed. 8He is near that justifieth me; who will contend with me? let us stand together: who is mine adversary? let him come near to me.50.8 mine…: Heb. the master of my cause? 9Behold, the Lord GOD will help me; who is he that shall condemn me? lo, they all shall wax old as a garment; the moth shall eat them up.

10¶ Who is among you that feareth the LORD, that obeyeth the voice of his servant, that walketh in darkness, and hath no light? let him trust in the name of the LORD, and stay upon his God. 11Behold, all ye that kindle a fire, that compass yourselves about with sparks: walk in the light of your fire, and in the sparks that ye have kindled. This shall ye have of mine hand; ye shall lie down in sorrow.