Yesaya 5 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 5:1-30

Nyimbo ya Munda Wamphesa

1Ndidzamuyimbira bwenzi langa

nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa:

Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa

pa phiri la nthaka yachonde.

2Anatipula nachotsa miyala yonse

ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri.

Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo

ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo.

Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino,

koma ayi, unabala mphesa zosadya.

3“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda,

weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.

4Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa

kupambana chomwe ndawuchitira kale?

Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino,

bwanji unabala mphesa zosadya?

5Tsopano ndikuwuzani

chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa:

ndidzachotsa mpanda wake,

ndipo mundawo udzawonongeka;

ndidzagwetsa khoma lake,

ndipo nyama zidzapondapondamo.

6Ndidzawusandutsa tsala,

udzakhala wosatengulira ndi wosalimira

ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina.

Ndidzalamula mitambo

kuti isagwetse mvula pa mundapo.”

7Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse

ndi Aisraeli,

ndipo anthu a ku Yuda ndiwo

minda yake yomukondweretsa.

Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana;

mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.

Tsoka ndi Chiweruzo

8Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba,

ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda,

mpaka mutalanda malo onse

kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.

9Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti,

“Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja,

nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.

10Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi,

kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”

11Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa

nathamangira chakumwa choledzeretsa,

amene amamwa mpaka usiku

kufikira ataledzera kotheratu.

12Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe,

matambolini, zitoliro ndi vinyo,

ndipo sasamala ntchito za Yehova,

salemekeza ntchito za manja ake.

13Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo

chifukwa cha kusamvetsa zinthu;

atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala,

ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.

14Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta

ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake;

mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka;

adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko.

15Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa,

anthu onse adzachepetsedwa,

anthu odzikuza adzachita manyazi.

16Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama.

Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.

17Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo;

ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.

18Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo,

ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,

19amene amanena kuti, “Yehova afulumire,

agwire ntchito yake mwamsanga

kuti ntchitoyo tiyione.

Ntchito zionekere,

zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita,

zichitike kuti tizione.”

20Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino

ndipo zabwino amaziyesa zoyipa,

amene mdima amawuyesa kuwala

ndipo kuwala amakuyesa mdima,

amene zowawasa amaziyesa zotsekemera

ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.

21Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru

ndipo amadziyesa ochenjera.

22Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo

ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,

23amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu

koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.

24Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu

ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto,

momwemonso mizu yawo idzawola

ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi;

chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse,

ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.

25Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake;

watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha

Mapiri akugwedezeka,

ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala.

Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke,

dzanja lake likanali chitambasulire;

26Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali,

akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi.

Awo akubwera,

akubweradi mofulumira kwambiri!

27Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa,

palibe amene akusinza kapena kugona;

palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka,

palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.

28Mivi yawo ndi yakuthwa,

mauta awo onse ndi okoka,

ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi,

magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.

29Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango,

amabangula ngati misona ya mkango;

imadzuma pamene ikugwira nyama

ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.

30Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula

ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja.

Ndipo wina akakayangʼana dzikolo

adzangoona mdima ndi zovuta;

ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

La Bible du Semeur

Esaïe 5:1-30

Le chant de la vigne

1Je veux chanter ╵pour mon ami

la chanson de mon bien-aimé ╵au sujet de sa vigne.

Mon ami avait une vigne

sur un coteau fertile.

2Il en sarcla le sol, ╵en enleva les pierres

et il y mit des plants de choix.

Il bâtit une tour de guet ╵au milieu de la vigne

et il y creusa un pressoir.

Il attendait donc de sa vigne ╵de beaux raisins,

mais elle n’a produit ╵que des raisins infects5.2 Voir Mt 21.33 ; Mc 12.1 ; Lc 20.9..

3Maintenant donc, ╵habitants de Jérusalem, ╵gens de Juda,

soyez les juges ╵entre moi et ma vigne !

4Qu’y avait-il encore ╵à faire pour ma vigne

que je n’aurais pas fait ?

Pourquoi, alors que j’attendais de bons raisins,

n’a-t-elle produit que des fruits infects ?

5Maintenant donc, ╵je vous ferai savoir

ce que je vais faire à ma vigne :

j’arracherai sa haie

pour qu’elle soit broutée,

je ferai une brèche ╵dans sa clôture

pour que les passants la piétinent.

6J’en ferai une friche :

nul ne la taillera, ╵nul ne la sarclera.

Les ronces, les épines ╵y croîtront librement,

et j’interdirai aux nuages

de répandre leur pluie sur elle.

7Or, c’est le peuple d’Israël

qui est la vigne ╵de l’Eternel, ╵du Seigneur des armées célestes.

Le plant qui faisait ses délices

ce sont les habitants ╵du pays de Juda.

Il attendait d’eux la droiture,

et ce n’est qu’injustice ; ╵il attendait d’eux la justice,

et ce sont des cris de détresse.

Malheurs et jugements

8Malheur à vous ╵qui joignez maison à maison

et ajoutez un champ à l’autre

au point qu’il n’y a plus d’espace libre

parce que vous occupez à vous seuls ╵tout le pays.

9Le Seigneur des armées célestes ╵m’a parlé et m’a dit :

Ces nombreuses maisons ╵deviendront une ruine,

ces maisons grandes et superbes ╵seront inhabitées.

10Car dix arpents de vigne ╵ne produiront qu’un tonnelet de vin,

et dix mesures de semence ╵n’en donneront qu’une de blé5.10 Trois hectares de vignes ne produiront pas 50 litres de vin et celui qui sèmera 100 kilogrammes de blé n’en récoltera que dix..

11Malheur à vous ╵qui courez de bonne heure

après les boissons enivrantes

et qui vous attardez, le soir, ╵excités par le vin !

12Des lyres et des luths, ╵des tambourins, des flûtes

animent vos festins ╵où le vin coule à flots.

Mais vous n’avez pas un regard ╵pour ce que l’Eternel a fait,

et vous ne voyez pas ╵l’œuvre qu’il accomplit.

13Voilà pourquoi mon peuple ╵s’en ira en exil,

car il n’a rien voulu savoir.

Ses notables mourront de faim

et la population de soif.

14C’est pourquoi le séjour des morts ╵fera gonfler sa gorge

et, démesurément, ╵élargira sa bouche.

Les dignitaires de la ville ╵et sa foule bruyante ╵y descendront ensemble

et leur joyeux tumulte ╵s’en ira avec eux.

15C’est pourquoi tous les hommes ╵devront courber le dos,

ils seront humiliés

et tous les orgueilleux ╵devront baisser les yeux.

16Le Seigneur des armées célestes ╵montrera sa grandeur ╵en instaurant le droit,

le Dieu saint manifestera ╵sa sainteté par la justice.

17Dans la ville ruinée, ╵des agneaux brouteront ╵comme en leur pâturage,

et des chevreaux ╵brouteront5.17 D’après l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel a : des étrangers dévoreront les ruines. sur les ruines ╵des demeures des riches.

18Malheur à vous ╵qui traînez le péché ╵derrière vous ╵avec les cordes du mensonge,

et qui tirez la faute ╵comme les traits d’un attelage !

19Oui, vous qui dites : ╵« Que Dieu se presse donc

d’accomplir son ouvrage

pour que nous le voyions !

Et qu’elle arrive, ╵la réalisation

des projets du Saint d’Israël,

afin que nous les connaissions. »

20Malheur à vous ╵qui nommez le mal bien

et le bien mal,

vous qui changez ╵les ténèbres en lumière,

la lumière en ténèbres,

vous qui changez ╵l’amertume en douceur

et la douceur en amertume.

21Malheur à vous ╵qui vous prenez pour sages

et vous croyez intelligents !

22Malheur à vous ╵qui êtes des héros

quand il s’agit de consommer du vin,

et des champions ╵pour vous gorger d’alcool ;

23qui, pour un pot-de-vin, ╵acquittez le coupable

et qui privez le juste ╵du droit qui lui est dû.

La colère de Dieu

24Voilà pourquoi ╵vous serez consumés ╵comme un fétu de paille ╵dévoré par la flamme

et comme une herbe sèche ╵engloutie par le feu.

Oui, vos racines pourriront,

votre fleur sera emportée ╵comme de la poussière,

puisque vous avez rejeté ╵la Loi de l’Eternel, ╵du Seigneur des armées célestes,

et avez méprisé ╵ce qu’a dit le Saint d’Israël.

25Voilà pourquoi ╵l’Eternel s’est mis en colère ╵contre son peuple,

et a porté la main sur lui ╵pour le frapper :

les montagnes sont ébranlées,

et les cadavres sont ╵pareils à des ordures ╵qui traînent dans les rues ;

mais malgré tout cela, ╵son courroux ne s’apaise pas,

sa main reste levée.

26L’Eternel dresse un étendard ╵pour des peuples lointains,

il siffle pour les appeler ╵du bout du monde.

Les voici qui arrivent ╵d’un pas prompt et léger5.26 Il s’agit très certainement des Assyriens..

27Personne parmi eux ╵ne connaît la fatigue, ╵personne ne chancelle,

personne ne somnole ╵et nul n’est endormi.

Nul n’a son ceinturon ╵dénoué de ses hanches,

les lanières de leurs sandales ╵ne sont pas déchirées.

28Leurs flèches sont aiguës,

et tous leurs arcs tendus,

les sabots des chevaux ╵sont comme du silex

et les roues de leurs chars ╵sont comme un ouragan.

29Quand ils rugissent, ╵on croirait des lions,

et leurs rugissements ╵rappellent ceux des lionceaux.

Ils grondent et saisissent ╵leur proie pour l’emporter,

personne ne peut la leur arracher.

30En ce jour-là, ╵retentira contre eux ╵un grondement pareil

à celui de la mer.

On regardera le pays :

on n’y verra que des ténèbres ╵et une grande angoisse ;

la lumière sera voilée ╵par d’épaisses nuées.