Yesaya 5 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 5:1-30

Nyimbo ya Munda Wamphesa

1Ndidzamuyimbira bwenzi langa

nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa:

Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa

pa phiri la nthaka yachonde.

2Anatipula nachotsa miyala yonse

ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri.

Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo

ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo.

Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino,

koma ayi, unabala mphesa zosadya.

3“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda,

weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.

4Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa

kupambana chomwe ndawuchitira kale?

Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino,

bwanji unabala mphesa zosadya?

5Tsopano ndikuwuzani

chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa:

ndidzachotsa mpanda wake,

ndipo mundawo udzawonongeka;

ndidzagwetsa khoma lake,

ndipo nyama zidzapondapondamo.

6Ndidzawusandutsa tsala,

udzakhala wosatengulira ndi wosalimira

ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina.

Ndidzalamula mitambo

kuti isagwetse mvula pa mundapo.”

7Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse

ndi Aisraeli,

ndipo anthu a ku Yuda ndiwo

minda yake yomukondweretsa.

Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana;

mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.

Tsoka ndi Chiweruzo

8Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba,

ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda,

mpaka mutalanda malo onse

kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.

9Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti,

“Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja,

nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.

10Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi,

kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”

11Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa

nathamangira chakumwa choledzeretsa,

amene amamwa mpaka usiku

kufikira ataledzera kotheratu.

12Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe,

matambolini, zitoliro ndi vinyo,

ndipo sasamala ntchito za Yehova,

salemekeza ntchito za manja ake.

13Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo

chifukwa cha kusamvetsa zinthu;

atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala,

ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.

14Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta

ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake;

mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka;

adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko.

15Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa,

anthu onse adzachepetsedwa,

anthu odzikuza adzachita manyazi.

16Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama.

Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.

17Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo;

ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.

18Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo,

ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,

19amene amanena kuti, “Yehova afulumire,

agwire ntchito yake mwamsanga

kuti ntchitoyo tiyione.

Ntchito zionekere,

zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita,

zichitike kuti tizione.”

20Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino

ndipo zabwino amaziyesa zoyipa,

amene mdima amawuyesa kuwala

ndipo kuwala amakuyesa mdima,

amene zowawasa amaziyesa zotsekemera

ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.

21Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru

ndipo amadziyesa ochenjera.

22Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo

ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,

23amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu

koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.

24Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu

ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto,

momwemonso mizu yawo idzawola

ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi;

chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse,

ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.

25Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake;

watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha

Mapiri akugwedezeka,

ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala.

Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke,

dzanja lake likanali chitambasulire;

26Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali,

akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi.

Awo akubwera,

akubweradi mofulumira kwambiri!

27Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa,

palibe amene akusinza kapena kugona;

palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka,

palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.

28Mivi yawo ndi yakuthwa,

mauta awo onse ndi okoka,

ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi,

magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.

29Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango,

amabangula ngati misona ya mkango;

imadzuma pamene ikugwira nyama

ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.

30Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula

ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja.

Ndipo wina akakayangʼana dzikolo

adzangoona mdima ndi zovuta;

ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.