Yesaya 49 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 49:1-26

Mtumiki wa Yehova

1Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba

tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali:

Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe,

ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.

2Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa,

anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake;

Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa

ndipo anandibisa mʼchimake.

3Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli.

Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”

4Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito

ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe,

koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova,

ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”

5Yehova anandiwumba ine

mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake

kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye

ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,

choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,

ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.

6Yehovayo tsono akuti,

“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,

kuti udzutse mafuko a Yakobo

ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.

Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,

udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”

7Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,

Woyerayo wa Israeli akunena,

amene mitundu ya anthu inamuda,

amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,

“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.

Akalonga nawonso adzagwada pansi.

Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika

ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

8Yehova akuti,

“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha,

ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza;

ndinakusunga ndi kukusandutsa

kuti ukhale pangano kwa anthu,

kuti dziko libwerere mwakale

ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.

9Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke

ndi a mu mdima kuti aonekere poyera.

“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira

ndi msipu pa mʼmalo owuma.

10Iwo sadzamva njala kapena ludzu,

kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza;

chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera

ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.

11Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo,

ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.

12Taonani, anthu anga adzachokera kutali,

ena kumpoto, ena kumadzulo,

enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”

13Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;

kondwera, iwe dziko lapansi;

imbani nyimbo inu mapiri!

Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,

ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.

14Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,

Ambuye wandiyiwala.”

15“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere

ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?

Ngakhale iye angathe kuyiwala,

Ine sindidzakuyiwala iwe!

16Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga;

makoma ako ndimawaona nthawi zonse.

17Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira,

ndipo amene anakupasula akuchokapo.

18Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane

ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe.

Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo,

anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa

chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’

19“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa

ndipo dziko lako ndi kusakazidwa,

chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera

ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.

20Ana obadwa nthawi yako yachisoni

adzanena kuti,

‘Malo ano atichepera,

tipatse malo ena woti tikhalemo.’

21Tsono iwe udzadzifunsa kuti,

‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa?

Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena;

ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa.

Ndani anawalera ana amenewa?

Ndinatsala ndekha,

nanga awa, achokera kuti?’ ”

22Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi,

“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere.

Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere.

Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo

ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.

23Mafumu adzakhala abambo wongokulera

ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera.

Iwo adzagwetsa nkhope

zawo pansi.

Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova;

iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”

24Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo,

kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?

25Koma zimene Yehova akunena ndi izi,

“Ankhondo adzawalanda amʼndende awo,

ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo;

ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu,

ndipo ndidzapulumutsa ana anu.

26Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe;

adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo.

Zikadzatero anthu onse adzadziwa

kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu,

Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”