Yesaya 49 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 49:1-26

Mtumiki wa Yehova

1Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba

tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali:

Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe,

ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.

2Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa,

anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake;

Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa

ndipo anandibisa mʼchimake.

3Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli.

Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”

4Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito

ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe,

koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova,

ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”

5Yehova anandiwumba ine

mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake

kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye

ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye,

choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova,

ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.

6Yehovayo tsono akuti,

“Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga,

kuti udzutse mafuko a Yakobo

ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka.

Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira,

udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”

7Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula,

Woyerayo wa Israeli akunena,

amene mitundu ya anthu inamuda,

amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti,

“Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira.

Akalonga nawonso adzagwada pansi.

Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika

ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”

Kubwezeretsedwa kwa Israeli

8Yehova akuti,

“Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha,

ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza;

ndinakusunga ndi kukusandutsa

kuti ukhale pangano kwa anthu,

kuti dziko libwerere mwakale

ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.

9Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke

ndi a mu mdima kuti aonekere poyera.

“Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira

ndi msipu pa mʼmalo owuma.

10Iwo sadzamva njala kapena ludzu,

kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza;

chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera

ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.

11Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo,

ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.

12Taonani, anthu anga adzachokera kutali,

ena kumpoto, ena kumadzulo,

enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”

13Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga;

kondwera, iwe dziko lapansi;

imbani nyimbo inu mapiri!

Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,

ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.

14Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya,

Ambuye wandiyiwala.”

15“Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere

ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni?

Ngakhale iye angathe kuyiwala,

Ine sindidzakuyiwala iwe!

16Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga;

makoma ako ndimawaona nthawi zonse.

17Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira,

ndipo amene anakupasula akuchokapo.

18Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane

ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe.

Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo,

anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa

chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’

19“Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa

ndipo dziko lako ndi kusakazidwa,

chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera

ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.

20Ana obadwa nthawi yako yachisoni

adzanena kuti,

‘Malo ano atichepera,

tipatse malo ena woti tikhalemo.’

21Tsono iwe udzadzifunsa kuti,

‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa?

Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena;

ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa.

Ndani anawalera ana amenewa?

Ndinatsala ndekha,

nanga awa, achokera kuti?’ ”

22Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi,

“Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere.

Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere.

Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo

ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.

23Mafumu adzakhala abambo wongokulera

ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera.

Iwo adzagwetsa nkhope

zawo pansi.

Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova;

iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”

24Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo,

kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?

25Koma zimene Yehova akunena ndi izi,

“Ankhondo adzawalanda amʼndende awo,

ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo;

ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu,

ndipo ndidzapulumutsa ana anu.

26Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe;

adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo.

Zikadzatero anthu onse adzadziwa

kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu,

Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”

La Bible du Semeur

Esaïe 49:1-26

Le deuxième chant du Serviteur

1Vous tous qui habitez les îles ╵et les régions côtières, ╵écoutez-moi !

Et vous peuples lointains, ╵prêtez-moi attention !

J’ai été appelé par l’Eternel ╵dès le sein maternel,

et il a mentionné mon nom ╵dès avant ma naissance.

2Il a fait de ma bouche ╵une épée acérée49.2 Voir Hé 4.12 ; Ap 1.16.,

il m’a couvert ╵de l’ombre de sa main49.2 Voir 51.16.,

et il a fait de moi ╵une flèche aiguisée ;

il m’a tenu caché, ╵dans son carquois.

3Il m’a dit : « Tu es mon serviteur, Israël ;

je manifesterai ╵ma splendeur au travers de toi. »

4Cependant, moi, j’ai dit :

« Je me suis fatigué pour rien,

c’est inutilement, ╵oui, c’est en pure perte, ╵que j’ai usé mes forces…

Mais l’Eternel me fera droit

et il tient en réserve ╵ma récompense. »

5Et maintenant, voici ╵ce que dit l’Eternel,

celui qui m’a formé ╵dès le sein de ma mère

pour que je sois son serviteur,

pour ramener Jacob à lui

et pour rassembler Israël ╵auprès de lui.

Je serai honoré ╵aux yeux de l’Eternel

et mon Dieu est la source de ma force.

6Et il a dit aussi : ╵« Tu ne seras pas seulement ╵mon serviteur

pour rétablir ╵les tribus de Jacob

et ramener ceux que j’ai préservés ╵du peuple d’Israël.

Car je t’établirai ╵pour être la lumière ╵des autres peuples

afin que mon salut parvienne ╵aux extrémités de la terre49.6 Voir 42.6. Cité en Ac 13.47. Allusion en Lc 2.32 (voir Jn 8.12 ; Ac 26.23).. »

7Voici ce que dit l’Eternel

qui délivre Israël, ╵qui en est le Dieu saint,

à l’homme méprisé

et détesté du peuple,

celui dont les despotes ╵ont fait leur serviteur :

Les rois t’apercevront, ╵et ils se lèveront,

les princes te verront, ╵ils se prosterneront,

afin d’honorer l’Eternel ╵qui est fidèle,

oui, le Saint d’Israël, ╵qui t’a choisi.

8Voici ce que dit l’Eternel :

Au moment favorable ╵je répondrai à ton appel,

et au jour du salut ╵je viendrai à ton aide.

Je te protégerai, ╵et je t’établirai

pour conclure une alliance avec le peuple

et pour relever le pays,

pour faire le partage ╵des patrimoines dévastés49.8 Cité en 2 Co 6.2. Voir 42.6.,

9pour dire aux prisonniers : « Sortez »,

et à ceux qui demeurent ╵dans les ténèbres :

« Montrez-vous ! »

Et ils se nourriront ╵partout le long des routes ;

ils trouveront des pâturages ╵sur toutes les collines.

10Ils n’endureront plus ╵ni la faim ni la soif,

la chaleur du désert et le soleil ╵ne les abattront plus

car celui qui les aime ╵les conduira

et il les mènera ╵auprès des sources d’eau49.10 Cité en Ap 7.16-17..

11Et toutes mes montagnes, ╵je les transformerai ╵en chemins praticables,

je remblaierai mes routes.

12Les voici, ils arrivent ╵des pays éloignés,

les uns viennent du nord, ╵les autres du couchant,

d’autres encore ╵de la région d’Assouan49.12 Assouan: dans le sud de l’Egypte. Selon le texte hébreu de Qumrân. Le texte hébreu traditionnel a Sinim, région non identifiée..

13O cieux, poussez des cris de joie !

O terre, éclate d’allégresse !

Faites retentir votre joie, montagnes,

parce que l’Eternel ╵a consolé son peuple

et qu’il a compassion ╵des affligés.

Le retour en grâce de Sion

14Cependant, Sion dit : ╵« L’Eternel m’a abandonnée,

oui, le Seigneur m’a oubliée. »

15Une femme oublie-t-elle ╵l’enfant qu’elle nourrit ?

Cesse-t-elle d’aimer ╵l’enfant qu’elle a conçu ?

Et même si les mères ╵oubliaient leurs enfants,

je ne t’oublierai pas !

16Voici, je t’ai gravée ╵dans le creux de mes mains,

je pense constamment ╵à tes remparts.

17Déjà tes fils49.17 Selon le texte hébreu traditionnel. Le texte hébreu de Qumrân et plusieurs autres versions anciennes ont : ceux qui te rebâtiront. accourent,

ceux qui te détruisaient ╵et qui te ravageaient

s’en iront loin de toi.

18Porte les yeux autour de toi, ╵regarde :

ils se rassemblent tous,

et ils viennent vers toi.

Aussi vrai que je suis vivant,

déclare l’Eternel,

tu t’en revêtiras ╵comme d’une parure,

et tu te les attacheras ╵comme la mariée sa ceinture.

19Car ton pays en ruine,

dévasté, désolé,

deviendra trop étroit ╵pour tous tes habitants ;

ceux qui te dévoraient ╵auront fui loin de toi.

20Tu entendras tes fils ╵dont tu étais privée

te répéter :

« Ce lieu est trop étroit pour nous.

Fais-nous donc de la place,

pour que nous puissions habiter ici ! »

21Alors tu te demanderas :

« Qui donc a mis, pour moi, ╵tous ces enfants au monde ?

J’étais privée d’enfants, ╵stérile,

et bannie en exil.

Qui donc a élevé ceux-ci ?

J’étais demeurée seule :

ceux-là, d’où viennent-ils ? »

22Voici ce que déclare ╵le Seigneur, l’Eternel :

Je ferai signe de la main ╵aux nations étrangères,

je dresserai mon étendard ╵en direction des peuples,

ils amèneront tes fils dans leurs bras,

ils chargeront tes filles ╵sur leurs épaules.

23Des rois s’occuperont de toi ╵comme s’ils étaient tes parents,

et leurs princesses ╵seront tes mères nourricières.

Ils se prosterneront ╵devant toi jusqu’à terre

et ils lécheront la poussière ╵attachée à tes pieds.

Et tu sauras alors ╵que je suis l’Eternel

et qu’on n’est pas déçu ╵quand on compte sur moi.

24Pourrait-on enlever ╵ce qu’a pris le guerrier ?

Les captifs du tyran49.24 D’après le texte hébreu de Qumrân et plusieurs versions anciennes. Le texte hébreu traditionnel a : du juste. ╵seront-ils délivrés ?

25Voici ce que dit l’Eternel :

Les captifs du guerrier ╵lui seront enlevés,

et la proie du tyran ╵va être délivrée.

Je ferai un procès moi-même ╵à ceux qui t’ont fait un procès

et je délivrerai ╵moi-même tes enfants.

26J’amènerai tes oppresseurs ╵à s’entredéchirer.

Et ils s’enivreront ╵du sang les uns des autres ╵comme de vin nouveau ;

alors tout le monde saura

que je suis l’Eternel ╵que c’est moi qui te sauve,

que je suis ton libérateur ╵le Puissant de Jacob.