Yesaya 48 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 48:1-22

Israeli ndi Nkhutukumve

1“Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,

inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,

ndinu a fuko la Yuda,

inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,

ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,

ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.

2Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika

ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,

amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:

3Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,

zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;

tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.

4Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve

wa nkhongo gwaa,

wa mutu wowuma.

5Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;

zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe

kuti unganene kuti,

‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,

kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’

6Inu munamva zinthu zimenezi.

Kodi inu simungazivomereze?

“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano

zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.

7Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;

munali musanazimve mpaka lero lino.

Choncho inu simunganene kuti,

‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’

8Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;

makutu anu sanali otsekuka.

Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti

chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.

9Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.

Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.

Sindidzakuwonongani kotheratu.

10Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;

ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.

11Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.

Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?

Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.

Kumasulidwa kwa Israeli

12“Tamvera Ine, iwe Yakobo,

Israeli, amene ndinakuyitana:

Mulungu uja Woyamba

ndi Wotsiriza ndine.

13Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,

dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.

Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba

ndi dziko lapansi.

14“Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:

Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?

Wokondedwa wa Yehova uja adzachita

zomwe Iye anakonzera Babuloni;

dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.

15Ine, Inetu, ndayankhula;

ndi kumuyitana

ndidzamubweretsa ndine

ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.

16“Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:

“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;

pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”

Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake

ndi kundituma.

17Yehova, Mpulumutsi wanu,

Woyerayo wa Israeli akuti,

“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,

ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.

18Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,

bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,

ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.

19Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,

ana ako akanachuluka ngati fumbi;

dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga

ndipo silikanafafanizidwa konse.”

20Tulukani mʼdziko la Babuloni!

Thawani dziko la Kaldeya!

Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo

ndipo muzilalikire

mpaka kumathero a dziko lapansi;

muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”

21Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;

anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;

anangʼamba thanthwelo ndipo

munatuluka madzi.

22“Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 48:1-22

Katonda bye Yayogera Bituukirira

148:1 a Is 58:2 b Yer 4:2“Muwulire kino, mmwe ennyumba ya Yakobo,

abayitibwa erinnya lya Isirayiri,

era abaava mu nda ya Yuda.

Mmwe abalayirira mu linnya lya Mukama,

era abaatula Katonda wa Isirayiri,

naye si mu mazima wadde mu butuukirivu.

248:2 a Is 52:1 b Is 10:20; Mi 3:11; Bar 2:17Kubanga beeyita ab’ekibuga ekitukuvu,

abeesiga Katonda wa Isirayiri,

Mukama Katonda ow’Eggye lye linnya lye.

348:3 a Is 41:22 b Is 45:21Okuva ku ntandikwa, nayasanguza ebyali bigenda okubaawo;

byava mu kamwa kange ne mbyogera.

Amangwago ne tubikola ne bituukirira.”

448:4 a Ma 31:27 b Kuv 32:9; Bik 7:51 c Ez 3:9Kubanga namanya obukakanyavu bwammwe;

ebinywa by’ensingo nga bikakanyavu ng’ekyuma;

ekyenyi ng’ekikomo.

548:5 Yer 44:15-18Nabamanyisizaawo edda ebyali bigenda okujja nga tebinnabaawo,

muleme kugamba nti,

“Bakatonda bange be baabikola:

Ekifaananyi kyange ekyole

n’ekifaananyi ekisaanuuse bye byakikola.”

6Mulabe ebintu bino nabibagamba dda,

era temubikkirize?

“Okuva leero nzija kubabuulira ku bintu ebiggya ebigenda okujja,

eby’ekyama bye mutawulirangako.

7Mbikola kaakano,

so si ekiseera ekyayita:

mwali temubiwulirangako mu biseera eby’emabega

si kulwa nga mugamba nti, ‘Laba nnali mbimanyi.’

848:8 Ma 9:7, 24; Zab 58:3Towulirangako wadde okutegeera.

Okuva edda n’edda okutu kwo tekuggukanga.

Kubanga namanya nti wali kyewaggula,

okuva ku kuzaalibwa kwo wayitibwa mujeemu.

948:9 a Zab 78:38; Is 30:18 b Nek 9:31Olw’erinnya lyange

ndwawo okusunguwala. Olw’ettendo lyange

ndwawo okukusunguwalira nneme okukuzikiriza.

1048:10 1Bk 8:51Laba nkugezesezza naye si nga ffeeza.

Nkugezesezza mu kirombe ky’okubonaabona.

1148:11 a 1Sa 12:22; Is 37:35 b Ma 32:27; Yer 14:7, 21; Ez 20:9, 14, 22, 44 c Is 42:8Ku lwange nze,

ku lwange nze ndikikola. Erinnya lyange nga livumiddwa.

Ekitiibwa kyange sirikiwa mulala.

Isirayiri Enunulibwa

1248:12 a Is 46:3 b Is 41:4; Kub 1:17; 22:13“Mpuliriza ggwe Yakobo.

Isirayiri gwe nalonda.

Nze Nzuuyo.

Nze ow’olubereberye era nze ow’enkomerero.

1348:13 a Beb 1:10-12 b Kuv 20:11 c Is 40:26Omukono gwange gwe gwateekawo omusingi gw’ensi,

era omukono gwange ogwa ddyo ne gwanjuluza eggulu.

Bwe mbiyita

byombi bijja.

1448:14 a Is 43:9 b Is 46:10-11“Mwekuŋŋaanye mwenna

mujje muwulire!

Ani ku bo eyali alangiridde ebintu bino?

Mukama amwagala; ajja kutuukiriza ekigendererwa kye e Babulooni,

era omukono gwe gwolekere Abakaludaaya.48:14 Abakaludaaya be Bababulooni

1548:15 Is 45:1Nze; Nze nzennyini nze njogedde.

Nze namuyita.

Ndimuleeta

era alituukiriza omulimu gwe.

1648:16 a Is 41:1 b Is 45:19 c Zek 2:9, 11“Munsemberere muwulirize bino.

“Okuva ku lubereberye saayogera mu kyama.

Nze mbaddewo okuviira ddala ku ntandikwa.”

Era kaakano Mukama Ayinzabyonna

n’Omwoyo we antumye.

1748:17 a Is 49:7 b Is 43:14 c Is 49:10 d Zab 32:8Bw’atyo bw’ayogera Mukama, Omununuzi wammwe,

Omutukuvu wa Isirayiri nti,

“Nze Mukama Katonda wo

akuyigiriza okukulaakulana,

akukulembera mu kkubo ly’oteekwa okutambuliramu.

1848:18 a Ma 32:29 b Zab 119:165; Is 66:12 c Is 45:8Singa kale wali owulirizza ebiragiro byange!

Wandibadde n’emirembe egikulukuta ng’omugga!

Era n’obutuukirivu bwo ng’amayengo g’ennyanja,

1948:19 a Lub 22:17 b Is 56:5; 66:22ezzadde lyo lyandibadde ng’omusenyu

abaana bo ng’obuweke bwagwo.

Erinnya lyabwe teryandivuddewo

wadde okuzikirira nga wendi.”

2048:20 a Yer 50:8; 51:6, 45; Zek 2:6-7; Kub 18:4 b Is 49:13 c Is 52:9; 63:9Muve mu Babulooni,

mudduke Abakaludaaya.

Mugende nga mutegeeza amawulire gano n’essanyu.

Mugalangirire wonna wonna

n’okutuusa ku nkomerero y’ensi.

Mugambe nti, “Mukama anunudde omuddu we Yakobo!”

2148:21 a Is 41:17 b Is 30:25 c Kuv 17:6; Kbl 20:11; Zab 105:41; Is 35:6So tebaalumwa nnyonta bwe yabayisa mu malungu.

Yabakulukusiza amazzi mu lwazi:

yayasa olwazi

amazzi ne gavaamu.

2248:22 Is 57:21“Tewali mirembe eri aboonoonyi,” bw’ayogera Mukama.