Yesaya 48 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 48:1-22

Israeli ndi Nkhutukumve

1“Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,

inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,

ndinu a fuko la Yuda,

inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,

ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,

ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.

2Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika

ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,

amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:

3Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,

zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;

tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.

4Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve

wa nkhongo gwaa,

wa mutu wowuma.

5Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;

zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe

kuti unganene kuti,

‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,

kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’

6Inu munamva zinthu zimenezi.

Kodi inu simungazivomereze?

“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano

zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.

7Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;

munali musanazimve mpaka lero lino.

Choncho inu simunganene kuti,

‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’

8Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;

makutu anu sanali otsekuka.

Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti

chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.

9Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.

Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.

Sindidzakuwonongani kotheratu.

10Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;

ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.

11Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.

Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?

Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.

Kumasulidwa kwa Israeli

12“Tamvera Ine, iwe Yakobo,

Israeli, amene ndinakuyitana:

Mulungu uja Woyamba

ndi Wotsiriza ndine.

13Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,

dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.

Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba

ndi dziko lapansi.

14“Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:

Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?

Wokondedwa wa Yehova uja adzachita

zomwe Iye anakonzera Babuloni;

dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.

15Ine, Inetu, ndayankhula;

ndi kumuyitana

ndidzamubweretsa ndine

ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.

16“Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:

“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;

pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”

Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake

ndi kundituma.

17Yehova, Mpulumutsi wanu,

Woyerayo wa Israeli akuti,

“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,

ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.

18Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,

bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,

ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.

19Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,

ana ako akanachuluka ngati fumbi;

dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga

ndipo silikanafafanizidwa konse.”

20Tulukani mʼdziko la Babuloni!

Thawani dziko la Kaldeya!

Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo

ndipo muzilalikire

mpaka kumathero a dziko lapansi;

muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”

21Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;

anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;

anangʼamba thanthwelo ndipo

munatuluka madzi.

22“Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.

King James Version

Isaiah 48:1-22

1Hear ye this, O house of Jacob, which are called by the name of Israel, and are come forth out of the waters of Judah, which swear by the name of the LORD, and make mention of the God of Israel, but not in truth, nor in righteousness. 2For they call themselves of the holy city, and stay themselves upon the God of Israel; The LORD of hosts is his name. 3I have declared the former things from the beginning; and they went forth out of my mouth, and I shewed them; I did them suddenly, and they came to pass. 4Because I knew that thou art obstinate, and thy neck is an iron sinew, and thy brow brass;48.4 obstinate: Heb. hard 5I have even from the beginning declared it to thee; before it came to pass I shewed it thee: lest thou shouldest say, Mine idol hath done them, and my graven image, and my molten image, hath commanded them. 6Thou hast heard, see all this; and will not ye declare it? I have shewed thee new things from this time, even hidden things, and thou didst not know them. 7They are created now, and not from the beginning; even before the day when thou heardest them not; lest thou shouldest say, Behold, I knew them. 8Yea, thou heardest not; yea, thou knewest not; yea, from that time that thine ear was not opened: for I knew that thou wouldest deal very treacherously, and wast called a transgressor from the womb.

9¶ For my name’s sake will I defer mine anger, and for my praise will I refrain for thee, that I cut thee not off. 10Behold, I have refined thee, but not with silver; I have chosen thee in the furnace of affliction.48.10 with…: or, for silver 11For mine own sake, even for mine own sake, will I do it: for how should my name be polluted? and I will not give my glory unto another.

12¶ Hearken unto me, O Jacob and Israel, my called; I am he; I am the first, I also am the last. 13Mine hand also hath laid the foundation of the earth, and my right hand hath spanned the heavens: when I call unto them, they stand up together.48.13 my…: or, the palm of my right hand hath spread out 14All ye, assemble yourselves, and hear; which among them hath declared these things? The LORD hath loved him: he will do his pleasure on Babylon, and his arm shall be on the Chaldeans. 15I, even I, have spoken; yea, I have called him: I have brought him, and he shall make his way prosperous.

16¶ Come ye near unto me, hear ye this; I have not spoken in secret from the beginning; from the time that it was, there am I: and now the Lord GOD, and his Spirit, hath sent me. 17Thus saith the LORD, thy Redeemer, the Holy One of Israel; I am the LORD thy God which teacheth thee to profit, which leadeth thee by the way that thou shouldest go. 18O that thou hadst hearkened to my commandments! then had thy peace been as a river, and thy righteousness as the waves of the sea: 19Thy seed also had been as the sand, and the offspring of thy bowels like the gravel thereof; his name should not have been cut off nor destroyed from before me.

20¶ Go ye forth of Babylon, flee ye from the Chaldeans, with a voice of singing declare ye, tell this, utter it even to the end of the earth; say ye, The LORD hath redeemed his servant Jacob. 21And they thirsted not when he led them through the deserts: he caused the waters to flow out of the rock for them: he clave the rock also, and the waters gushed out. 22There is no peace, saith the LORD, unto the wicked.