Kugwa kwa Babuloni
1“Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
kumugwira mosamala.
2Tenga mphero ndipo upere ufa;
chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
ndipo woloka mitsinje.
3Maliseche ako adzakhala poyera
ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
ndipo palibe amene adzandiletse.”
4Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
5“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
mfumukazi ya maufumu.
6Ndinawakwiyira anthu anga,
osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
ngakhale nkhalamba.
7Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.
8“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
ndipo ana anga sadzamwalira.’
9Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
ndi mawula amphamvu.
10Iwe unkadalira kuyipa kwako
ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
11Ngozi yayikulu idzakugwera
ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
chidzakugwera mwadzidzidzi.
12“Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
kapena kuopsezera nazo adani ako.
13Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
zimene ziti zidzakuchitikire.
14Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
15Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”
The Fall of Babylon
1“Go down, sit in the dust,
Virgin Daughter Babylon;
sit on the ground without a throne,
queen city of the Babylonians.47:1 Or Chaldeans; also in verse 5
No more will you be called
tender or delicate.
2Take millstones and grind flour;
take off your veil.
Lift up your skirts, bare your legs,
and wade through the streams.
3Your nakedness will be exposed
and your shame uncovered.
I will take vengeance;
I will spare no one.”
4Our Redeemer—the Lord Almighty is his name—
is the Holy One of Israel.
5“Sit in silence, go into darkness,
queen city of the Babylonians;
no more will you be called
queen of kingdoms.
6I was angry with my people
and desecrated my inheritance;
I gave them into your hand,
and you showed them no mercy.
Even on the aged
you laid a very heavy yoke.
7You said, ‘I am forever—
the eternal queen!’
But you did not consider these things
or reflect on what might happen.
8“Now then, listen, you lover of pleasure,
lounging in your security
and saying to yourself,
‘I am, and there is none besides me.
I will never be a widow
or suffer the loss of children.’
9Both of these will overtake you
in a moment, on a single day:
loss of children and widowhood.
They will come upon you in full measure,
in spite of your many sorceries
and all your potent spells.
10You have trusted in your wickedness
and have said, ‘No one sees me.’
Your wisdom and knowledge mislead you
when you say to yourself,
‘I am, and there is none besides me.’
11Disaster will come upon you,
and you will not know how to conjure it away.
A calamity will fall upon you
that you cannot ward off with a ransom;
a catastrophe you cannot foresee
will suddenly come upon you.
12“Keep on, then, with your magic spells
and with your many sorceries,
which you have labored at since childhood.
Perhaps you will succeed,
perhaps you will cause terror.
13All the counsel you have received has only worn you out!
Let your astrologers come forward,
those stargazers who make predictions month by month,
let them save you from what is coming upon you.
14Surely they are like stubble;
the fire will burn them up.
They cannot even save themselves
from the power of the flame.
These are not coals for warmth;
this is not a fire to sit by.
15That is all they are to you—
these you have dealt with
and labored with since childhood.
All of them go on in their error;
there is not one that can save you.