Yesaya 47 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 47:1-15

Kugwa kwa Babuloni

1“Tsika, ndi kukhala pa fumbi,

iwe namwali, Babuloni;

khala pansi wopanda mpando waufumu,

iwe namwali, Kaldeya

pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera

kumugwira mosamala.

2Tenga mphero ndipo upere ufa;

chotsa nsalu yako yophimba nkhope

kwinya chovala chako mpaka ntchafu

ndipo woloka mitsinje.

3Maliseche ako adzakhala poyera

ndipo udzachita manyazi.

Ndidzabwezera chilango

ndipo palibe amene adzandiletse.”

4Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,

dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

5“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,

iwe namwali, Kaldeya;

chifukwa sadzakutchulanso

mfumukazi ya maufumu.

6Ndinawakwiyira anthu anga,

osawasamalanso.

Ndinawapereka manja mwako,

ndipo iwe sunawachitire chifundo.

Iwe unachitira nkhanza

ngakhale nkhalamba.

7Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse

ngati mfumukazi.’

Koma sunaganizire zinthu izi

kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

8“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,

amene ukukhala mosatekesekawe,

umaganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.

Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,

ndipo ana anga sadzamwalira.’

9Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,

zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:

ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.

Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu

ngakhale ali ndi amatsenga ambiri

ndi mawula amphamvu.

10Iwe unkadalira kuyipa kwako

ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’

Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,

choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,

‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’

11Ngozi yayikulu idzakugwera

ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.

Mavuto adzakugwera

ndipo sudzatha kuwachotsa;

chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa

chidzakugwera mwadzidzidzi.

12“Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,

pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,

wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.

Mwina udzatha kupambana

kapena kuopsezera nazo adani ako.

13Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!

Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.

Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi

zimene ziti zidzakuchitikire.

14Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;

adzapsa ndi moto.

Sangathe kudzipulumutsa okha

ku mphamvu ya malawi a moto.

Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;

kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.

15Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,

anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito

ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.

Onse adzamwazika ndi mantha,

sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”

New International Version

Isaiah 47:1-15

The Fall of Babylon

1“Go down, sit in the dust,

Virgin Daughter Babylon;

sit on the ground without a throne,

queen city of the Babylonians.47:1 Or Chaldeans; also in verse 5

No more will you be called

tender or delicate.

2Take millstones and grind flour;

take off your veil.

Lift up your skirts, bare your legs,

and wade through the streams.

3Your nakedness will be exposed

and your shame uncovered.

I will take vengeance;

I will spare no one.”

4Our Redeemer—the Lord Almighty is his name—

is the Holy One of Israel.

5“Sit in silence, go into darkness,

queen city of the Babylonians;

no more will you be called

queen of kingdoms.

6I was angry with my people

and desecrated my inheritance;

I gave them into your hand,

and you showed them no mercy.

Even on the aged

you laid a very heavy yoke.

7You said, ‘I am forever—

the eternal queen!’

But you did not consider these things

or reflect on what might happen.

8“Now then, listen, you lover of pleasure,

lounging in your security

and saying to yourself,

‘I am, and there is none besides me.

I will never be a widow

or suffer the loss of children.’

9Both of these will overtake you

in a moment, on a single day:

loss of children and widowhood.

They will come upon you in full measure,

in spite of your many sorceries

and all your potent spells.

10You have trusted in your wickedness

and have said, ‘No one sees me.’

Your wisdom and knowledge mislead you

when you say to yourself,

‘I am, and there is none besides me.’

11Disaster will come upon you,

and you will not know how to conjure it away.

A calamity will fall upon you

that you cannot ward off with a ransom;

a catastrophe you cannot foresee

will suddenly come upon you.

12“Keep on, then, with your magic spells

and with your many sorceries,

which you have labored at since childhood.

Perhaps you will succeed,

perhaps you will cause terror.

13All the counsel you have received has only worn you out!

Let your astrologers come forward,

those stargazers who make predictions month by month,

let them save you from what is coming upon you.

14Surely they are like stubble;

the fire will burn them up.

They cannot even save themselves

from the power of the flame.

These are not coals for warmth;

this is not a fire to sit by.

15That is all they are to you—

these you have dealt with

and labored with since childhood.

All of them go on in their error;

there is not one that can save you.