Yesaya 46 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 46:1-13

Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake

1Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;

nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.

Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.

Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.

2Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;

sizikutha kupulumutsa katunduyo,

izo zomwe zikupita ku ukapolo.

3Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,

inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,

Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,

ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.

4Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi

ndidzakusamalirani ndithu.

Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,

ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.

5“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?

Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?

6Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo

ndipo amayeza siliva pa masikelo;

amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,

kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.

7Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;

amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.

Singathe kusuntha pamalo pakepo.

Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;

kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.

8“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,

Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.

9Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;

chifukwa Ine ndine Mulungu

ndipo palibe wina ofanana nane.

10Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.

Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.

Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.

Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.

11Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.

Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.

Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;

zimene ndafuna ndidzazichitadi.

12Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,

inu amene muli kutali ndi chipulumutso.

13Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;

sichili kutali.

Tsikulo layandikira

ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani

ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

New International Version – UK

Isaiah 46:1-13

Gods of Babylon

1Bel bows down, Nebo stoops low;

their idols are borne by beasts of burden.46:1 Or are but beasts and cattle

The images that are carried about are burdensome,

a burden for the weary.

2They stoop and bow down together;

unable to rescue the burden,

they themselves go off into captivity.

3‘Listen to me, you descendants of Jacob,

all the remnant of the people of Israel,

you whom I have upheld since your birth,

and have carried since you were born.

4Even to your old age and grey hairs

I am he, I am he who will sustain you.

I have made you and I will carry you;

I will sustain you and I will rescue you.

5‘With whom will you compare me or count me equal?

To whom will you liken me that we may be compared?

6Some pour out gold from their bags

and weigh out silver on the scales;

they hire a goldsmith to make it into a god,

and they bow down and worship it.

7They lift it to their shoulders and carry it;

they set it up in its place, and there it stands.

From that spot it cannot move.

Even though someone cries out to it, it cannot answer;

it cannot save them from their troubles.

8‘Remember this, keep it in mind,

take it to heart, you rebels.

9Remember the former things, those of long ago;

I am God, and there is no other;

I am God, and there is none like me.

10I make known the end from the beginning,

from ancient times, what is still to come.

I say, “My purpose will stand,

and I will do all that I please.”

11From the east I summon a bird of prey;

from a far-off land, a man to fulfil my purpose.

What I have said, that I will bring about;

what I have planned, that I will do.

12Listen to me, you stubborn-hearted,

you who are now far from my righteousness.

13I am bringing my righteousness near,

it is not far away;

and my salvation will not be delayed.

I will grant salvation to Zion,

my splendour to Israel.