Yesaya 46 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 46:1-13

Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake

1Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;

nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.

Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.

Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.

2Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;

sizikutha kupulumutsa katunduyo,

izo zomwe zikupita ku ukapolo.

3Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,

inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,

Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,

ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.

4Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi

ndidzakusamalirani ndithu.

Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,

ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.

5“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?

Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?

6Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo

ndipo amayeza siliva pa masikelo;

amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,

kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.

7Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;

amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.

Singathe kusuntha pamalo pakepo.

Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;

kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.

8“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,

Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.

9Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;

chifukwa Ine ndine Mulungu

ndipo palibe wina ofanana nane.

10Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.

Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.

Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.

Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.

11Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.

Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.

Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;

zimene ndafuna ndidzazichitadi.

12Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,

inu amene muli kutali ndi chipulumutso.

13Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;

sichili kutali.

Tsikulo layandikira

ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani

ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 46:1-13

巴比倫的假神

1彼勒屈膝跪下,

尼波彎腰降服。

這些巴比倫的偶像成為野獸和牲畜背上的重負,

使其疲憊不堪。

2它們一同屈膝降服,

不但救不了被擄的巴比倫人,

自己也被擄去。

3耶和華說:「雅各家啊,以色列家的餘民啊,要聽我說。

你們一出生,我就照顧你們;

一出母胎,我就呵護你們。

4即使你們年老髮白的時候,

我仍然一如既往地扶持你們。

我造了你們,必照顧你們,

扶持你們,拯救你們。

5「你們拿誰與我相比,

使之與我同等呢?

你們把誰比作我,

使之與我相同呢?

6有些人從囊中取金子,

又用天平稱銀子,

雇銀匠製造神像,

然後向它俯伏叩拜。

7他們把神像抬起來扛在肩上,

找個地方把它安置好,

它就在那裡呆立不動。

人向它呼求,它不能回應,

也不能救人脫離困境。

8「你們這些悖逆的人啊,

要將這些事銘記在心。

9你們要記住古時發生的事,

因為我是獨一無二的上帝,

再沒有誰能與我相比。

10我從太初就預言末後的事,

從亙古就宣佈將來的事。

我的旨意必成就,

我的計劃必實現。

11我從東方召來鷙鳥,

從遙遠的地方召人來成就我的計劃。

我言出必行,

必成就自己的計劃。

12你們這些冥頑不靈、

遠離公義的人啊,聽我說。

13我要親自施行公義,

那一天已經不遠,

我的救恩很快就會來臨。

我要在錫安賜下救恩,

把我的榮耀賜給以色列