Yesaya 46 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 46:1-13

Za Kupasuka kwa Babuloni ndi Mafano Ake

1Beli wagwada pansi, Nebo wawerama;

nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo.

Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe.

Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.

2Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo;

sizikutha kupulumutsa katunduyo,

izo zomwe zikupita ku ukapolo.

3Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo,

inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli,

Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu,

ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.

4Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi

ndidzakusamalirani ndithu.

Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani,

ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.

5“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani?

Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?

6Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo

ndipo amayeza siliva pa masikelo;

amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu,

kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.

7Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo;

amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo.

Singathe kusuntha pamalo pakepo.

Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha;

kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.

8“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi,

Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.

9Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana;

chifukwa Ine ndine Mulungu

ndipo palibe wina ofanana nane.

10Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe.

Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike.

Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi.

Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.

11Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa.

Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa.

Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi;

zimene ndafuna ndidzazichitadi.

12Ndimvereni, inu anthu owuma mtima,

inu amene muli kutali ndi chipulumutso.

13Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa;

sichili kutali.

Tsikulo layandikira

ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani

ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 46:1-13

巴比伦的假神

1彼勒屈膝跪下,

尼波弯腰降服。

这些巴比伦的偶像成为野兽和牲畜背上的重负,

使其疲惫不堪。

2它们一同屈膝降服,

不但救不了被掳的巴比伦人,

自己也被掳去。

3耶和华说:“雅各家啊,以色列家的余民啊,要听我说。

你们一出生,我就照顾你们;

一出母胎,我就呵护你们。

4即使你们年老发白的时候,

我仍然一如既往地扶持你们。

我造了你们,必照顾你们,

扶持你们,拯救你们。

5“你们拿谁与我相比,

使之与我同等呢?

你们把谁比作我,

使之与我相同呢?

6有些人从囊中取金子,

又用天平称银子,

雇银匠制造神像,

然后向它俯伏叩拜。

7他们把神像抬起来扛在肩上,

找个地方把它安置好,

它就在那里呆立不动。

人向它呼求,它不能回应,

也不能救人脱离困境。

8“你们这些悖逆的人啊,

要将这些事铭记在心。

9你们要记住古时发生的事,

因为我是独一无二的上帝,

再没有谁能与我相比。

10我从太初就预言末后的事,

从亘古就宣布将来的事。

我的旨意必成就,

我的计划必实现。

11我从东方召来鸷鸟,

从遥远的地方召人来成就我的计划。

我言出必行,

必成就自己的计划。

12你们这些冥顽不灵、

远离公义的人啊,听我说。

13我要亲自施行公义,

那一天已经不远,

我的救恩很快就会来临。

我要在锡安赐下救恩,

把我的荣耀赐给以色列