Yesaya 45 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 45:1-25

1Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake

Koresi amene anamugwira dzanja lamanja

kuti agonjetse mitundu ya anthu

ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,

ndi kutsekula zitseko

kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:

2Ine ndidzayenda patsogolo pako,

ndi kusalaza mapiri;

ndidzaphwanya zitseko za mkuwa

ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.

3Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,

katundu wa pamalo obisika,

kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova

Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.

4Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,

chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,

Ine ndakuyitana pokutchula dzina

ndipo ndakupatsa dzina laulemu

ngakhale iwe sukundidziwa Ine.

5Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;

kupatula Ine palibenso Mulungu wina.

Ndidzakupatsa mphamvu,

ngakhale sukundidziwa Ine,

6kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo

anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

7Ndimalenga kuwala ndi mdima,

ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;

ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.

8“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;

mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.

Dziko lapansi litsekuke,

ndipo chipulumutso chiphuke kuti

chilungamo chimereponso;

Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.

9“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,

ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.

Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,

‘Kodi ukuwumba chiyani?’

Kodi ntchito yako inganene kuti,

‘Ulibe luso?’

10Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,

‘Kodi munabereka chiyani?’

Kapena amayi ake kuti,

‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’

11“Yehova

Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,

zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:

Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,

kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?

12Ndine amene ndinapanga dziko lapansi

ndikulenga munthu kuti akhalemo.

Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;

ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.

13Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:

ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.

Iye adzamanganso mzinda wanga

ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,

wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,

akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

14Yehova akuti,

“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.

Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba

adzabwera kwa inu

ndipo adzakhala anthu anu;

iwo adzidzakutsatani pambuyo panu

ali mʼmaunyolo.

Adzakugwadirani

ndi kukupemphani, ponena kuti,

‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;

palibenso mulungu wina.’ ”

15Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika

amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.

16Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.

Adzakhala osokonezeka maganizo.

17Koma Yehova adzapulumutsa Israeli

ndi chipulumutso chamuyaya;

simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka

mpaka kalekale.

18Yehova

analenga zinthu zakumwamba,

Iye ndiye Mulungu;

amene akulenga dziko lapansi,

ndi kulikhazikitsa,

sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,

koma analipanga kuti anthu akhalemo.

Iyeyu akunena kuti:

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

19Ine sindinayankhule mwachinsinsi,

pamalo ena a mdima;

Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,

“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”

Ine Yehova, ndimayankhula zoona;

ndikunena zolungama.

20Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;

yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.

Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,

amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.

21Fotokozani mlandu wanu,

mupatsane nzeru nonse pamodzi.

Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?

Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?

Kodi si Ineyo Yehova?

Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,

Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,

palibenso wina kupatula Ine.

22“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,

inu anthu onse a pa dziko lapansi,

pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.

23Ndalumbira ndekha,

pakamwa panga patulutsa mawu owona,

mawu amene sadzasinthika konse akuti,

bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;

anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.

24Iwo adzanene kwa Ine kuti,

‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”

Onse amene anamuwukira Iye

adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.

25Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli

zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

New Russian Translation

Исаия 45:1-25

Пророчество о Кире

1Так Господь говорит Своему помазаннику Киру,

которого Он держит45:1 Букв.: «Я держу». за правую руку,

чтобы смирить перед ним народы

и отобрать у царей их оружие,

чтобы открыть перед ним двери,

ворота, что не затворятся:

2– Я пойду пред тобой

и горы45:2 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «опухоли». сровняю;

разломаю бронзовые ворота

и сломаю железные засовы.

3Я отдам тебе сокровища, спрятанные во тьме,

богатства, хранимые в тайниках,

чтобы познал ты, что Я – Господь,

Бог Израиля, называющий тебя по имени.

4Ради слуги Моего Иакова,

ради Израиля, избранного Моего,

Я зову тебя по имени,

славное имя тебе дарую,

хотя ты Меня и не знаешь.

5Я – Господь, и другого нет;

нет Бога кроме Меня.

Я укреплю тебя,

хотя ты Меня и не знаешь,

6чтобы от солнечного восхода

и до места его заката

знали, что нет никого, кроме Меня;

Я – Господь, и другого нет.

7Я создаю свет и творю тьму,

даю благополучие и творю беду;

Я, Господь, создаю все это.

8Небеса, изливайте свыше праведность,

пусть хлынут ею облака.

Пусть раскроется земля,

чтобы взошло спасение;

пусть растет с ним и праведность.

Я, Господь, творю все это.

9Горе тому, кто препирается со своим Создателем,

кто лишь черепок среди черепков земных!

Скажет ли глина горшечнику:

«Что ты делаешь?»

Скажет ли дело твое:

«Ты такой безрукий!»?

10Горе тому, кто говорит своему отцу:

«Кого ты породил?» –

или своей матери:

«Кого ты произвела на свет?»

11Так говорит Господь,

Святой Израиля и Создатель его, о делах грядущих:

– Вам ли спрашивать Меня о Моих детях

или указывать Мне в деле Моих рук?

12Я создал землю

и сотворил на ней человека.

Я Своими руками распростер небеса

и построил их звездное воинство.

13Я воздвигну Кира45:13 Букв.: «его». в праведности;

все пути его сделаю ровными.

Он отстроит город

и отпустит Моих пленников,

но не за выкуп или подарки, –

говорит Господь Сил.

Спасение для всех народов

14Так говорит Господь:

– Богатство Египта, доход Куша

и севеяне, рослый народ,

к тебе перейдут и будут твоими;

они последуют за тобой,

придут к тебе в цепях.

Они поклонятся тебе

и будут умолять тебя, говоря:

«Только с тобою Бог, и другого нет;

кроме Него нет Бога».

15Воистину, Ты – Бог сокровенный,

Бог Израиля, Спаситель.

16Все, кто делает идолов, будут постыжены и опозорены;

в бесчестие отойдут они все вместе.

17Но Господь спасет Израиль,

вечным спасением;

не постыдитесь и не опозоритесь вы во веки и веки.

18Ведь так говорит Господь,

сотворивший небеса (Он – Бог,

образовавший, создавший землю;

Он утвердил ее; не сотворил ее пустошью,

но сотворил ее, чтобы она заселилась):

– Я – Господь, и другого нет.

19Я говорил не в тайне,

не из земли тьмы;

Я не говорил потомкам Иакова:

«Ищите Меня впустую».

Я, Господь, говорю истину;

Я возвещаю правду.

20Соберитесь и придите,

сойдитесь вместе, уцелевшие из народов.

Невежды те, что носят идолов деревянных,

молятся богу, который не спасает.

21Объявите и изложите свое дело;

пусть они совещаются вместе.

Кто предсказал это издавна,

издревле кто возвестил?

Разве не Я, Господь?

Нет Бога, кроме Меня,

Бога праведного, Спасителя;

нет другого, кроме Меня.

22Обратитесь ко Мне и будете спасены,

все края земли,

потому что Я – Бог, и другого нет.

23Я поклялся Самим Собой,

в праведности из уст Моих вышло

слово, которое не возвратится:

Преклонится предо Мной каждое колено.

Мною будет клясться каждый язык.

24Будут говорить обо Мне: «Только в Господе

пребывают праведность и сила».

Все, кто враждовал с Ним,

придут к Нему и устыдятся.

25В Господе оправдаются и прославятся

все потомки Израиля.