Yesaya 45 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 45:1-25

1Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake

Koresi amene anamugwira dzanja lamanja

kuti agonjetse mitundu ya anthu

ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,

ndi kutsekula zitseko

kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:

2Ine ndidzayenda patsogolo pako,

ndi kusalaza mapiri;

ndidzaphwanya zitseko za mkuwa

ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.

3Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,

katundu wa pamalo obisika,

kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova

Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.

4Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,

chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,

Ine ndakuyitana pokutchula dzina

ndipo ndakupatsa dzina laulemu

ngakhale iwe sukundidziwa Ine.

5Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;

kupatula Ine palibenso Mulungu wina.

Ndidzakupatsa mphamvu,

ngakhale sukundidziwa Ine,

6kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo

anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

7Ndimalenga kuwala ndi mdima,

ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;

ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.

8“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;

mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.

Dziko lapansi litsekuke,

ndipo chipulumutso chiphuke kuti

chilungamo chimereponso;

Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.

9“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,

ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.

Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,

‘Kodi ukuwumba chiyani?’

Kodi ntchito yako inganene kuti,

‘Ulibe luso?’

10Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,

‘Kodi munabereka chiyani?’

Kapena amayi ake kuti,

‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’

11“Yehova

Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,

zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:

Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,

kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?

12Ndine amene ndinapanga dziko lapansi

ndikulenga munthu kuti akhalemo.

Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;

ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.

13Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:

ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.

Iye adzamanganso mzinda wanga

ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,

wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,

akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

14Yehova akuti,

“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.

Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba

adzabwera kwa inu

ndipo adzakhala anthu anu;

iwo adzidzakutsatani pambuyo panu

ali mʼmaunyolo.

Adzakugwadirani

ndi kukupemphani, ponena kuti,

‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;

palibenso mulungu wina.’ ”

15Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika

amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.

16Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.

Adzakhala osokonezeka maganizo.

17Koma Yehova adzapulumutsa Israeli

ndi chipulumutso chamuyaya;

simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka

mpaka kalekale.

18Yehova

analenga zinthu zakumwamba,

Iye ndiye Mulungu;

amene akulenga dziko lapansi,

ndi kulikhazikitsa,

sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,

koma analipanga kuti anthu akhalemo.

Iyeyu akunena kuti:

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

19Ine sindinayankhule mwachinsinsi,

pamalo ena a mdima;

Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,

“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”

Ine Yehova, ndimayankhula zoona;

ndikunena zolungama.

20Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;

yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.

Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,

amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.

21Fotokozani mlandu wanu,

mupatsane nzeru nonse pamodzi.

Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?

Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?

Kodi si Ineyo Yehova?

Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,

Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,

palibenso wina kupatula Ine.

22“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,

inu anthu onse a pa dziko lapansi,

pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.

23Ndalumbira ndekha,

pakamwa panga patulutsa mawu owona,

mawu amene sadzasinthika konse akuti,

bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;

anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.

24Iwo adzanene kwa Ine kuti,

‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”

Onse amene anamuwukira Iye

adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.

25Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli

zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

King James Version

Isaiah 45:1-25

1Thus saith the LORD to his anointed, to Cyrus, whose right hand I have holden, to subdue nations before him; and I will loose the loins of kings, to open before him the two leaved gates; and the gates shall not be shut;45.1 have…: or, strengthened 2I will go before thee, and make the crooked places straight: I will break in pieces the gates of brass, and cut in sunder the bars of iron: 3And I will give thee the treasures of darkness, and hidden riches of secret places, that thou mayest know that I, the LORD, which call thee by thy name, am the God of Israel. 4For Jacob my servant’s sake, and Israel mine elect, I have even called thee by thy name: I have surnamed thee, though thou hast not known me.

5¶ I am the LORD, and there is none else, there is no God beside me: I girded thee, though thou hast not known me: 6That they may know from the rising of the sun, and from the west, that there is none beside me. I am the LORD, and there is none else. 7I form the light, and create darkness: I make peace, and create evil: I the LORD do all these things. 8Drop down, ye heavens, from above, and let the skies pour down righteousness: let the earth open, and let them bring forth salvation, and let righteousness spring up together; I the LORD have created it. 9Woe unto him that striveth with his Maker! Let the potsherd strive with the potsherds of the earth. Shall the clay say to him that fashioneth it, What makest thou? or thy work, He hath no hands? 10Woe unto him that saith unto his father, What begettest thou? or to the woman, What hast thou brought forth?

11Thus saith the LORD, the Holy One of Israel, and his Maker, Ask me of things to come concerning my sons, and concerning the work of my hands command ye me. 12I have made the earth, and created man upon it: I, even my hands, have stretched out the heavens, and all their host have I commanded. 13I have raised him up in righteousness, and I will direct all his ways: he shall build my city, and he shall let go my captives, not for price nor reward, saith the LORD of hosts.45.13 direct: or, make straight 14Thus saith the LORD, The labour of Egypt, and merchandise of Ethiopia and of the Sabeans, men of stature, shall come over unto thee, and they shall be thine: they shall come after thee; in chains they shall come over, and they shall fall down unto thee, they shall make supplication unto thee, saying, Surely God is in thee; and there is none else, there is no God. 15Verily thou art a God that hidest thyself, O God of Israel, the Saviour. 16They shall be ashamed, and also confounded, all of them: they shall go to confusion together that are makers of idols. 17But Israel shall be saved in the LORD with an everlasting salvation: ye shall not be ashamed nor confounded world without end. 18For thus saith the LORD that created the heavens; God himself that formed the earth and made it; he hath established it, he created it not in vain, he formed it to be inhabited: I am the LORD; and there is none else. 19I have not spoken in secret, in a dark place of the earth: I said not unto the seed of Jacob, Seek ye me in vain: I the LORD speak righteousness, I declare things that are right.

20¶ Assemble yourselves and come; draw near together, ye that are escaped of the nations: they have no knowledge that set up the wood of their graven image, and pray unto a god that cannot save. 21Tell ye, and bring them near; yea, let them take counsel together: who hath declared this from ancient time? who hath told it from that time? have not I the LORD? and there is no God else beside me; a just God and a Saviour; there is none beside me. 22Look unto me, and be ye saved, all the ends of the earth: for I am God, and there is none else. 23I have sworn by myself, the word is gone out of my mouth in righteousness, and shall not return, That unto me every knee shall bow, every tongue shall swear. 24Surely, shall one say, in the LORD have I righteousness and strength: even to him shall men come; and all that are incensed against him shall be ashamed.45.24 Surely…: or, Surely he shall say of me, In the LORD is all righteousness and strength45.24 righteousness: Heb. righteousnesses 25In the LORD shall all the seed of Israel be justified, and shall glory.