Yesaya 44 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 44:1-28

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

1Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Israeli, amene ndinakusankha.

2Yehova

amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,

ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,

Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Yesuruni, amene ndinakusankha.

3Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,

ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;

ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,

ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.

4Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino

ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.

5Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’

wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;

winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’

ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

6“Yehova Mfumu

ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:

Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;

palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.

7Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.

Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe

zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,

ndi ziti zimene zidzachitike;

inde, muloleni alosere zimene zikubwera.

8Musanjenjemere, musachite mantha.

Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?

Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?

Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

9Onse amene amapanga mafano ngachabe,

ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.

Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;

ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.

10Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,

limene silingamupindulire?

11Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;

amisiri a mafano ndi anthu chabe.

Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;

onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo

ndipo amachiyika pa makala amoto;

ndi dzanja lake lamphamvu

amachisula pochimenya ndi nyundo.

Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;

iye samwa madzi, ndipo amalefuka.

13Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe

ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;

amasema bwinobwino ndi chipangizo chake

ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.

Amachipanga ngati munthu,

munthu wake wokongola

kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.

14Amagwetsa mitengo ya mkungudza,

mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu

nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,

ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.

15Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;

nthambi zina amasonkhera moto wowotha,

amakolezera moto wophikira buledi

ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;

iye amapanga fano ndi kumaligwadira.

16Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto

wowotcherapo nyama imene

amadya, nakhuta.

Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,

“Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”

17Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;

amaligwadira ndi kulipembedza.

Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,

“Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”

18Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;

maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,

ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.

19Palibe amene amayima nʼkulingalira.

Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,

chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;

pa makala ake ndinaphikira buledi,

ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.

Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.

Kodi ndidzagwadira mtengo?

20Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;

motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,

“Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi

popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.

Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;

iwe Israeli, sindidzakuyiwala.

22Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,

ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.

Bwerera kwa Ine,

popeza ndakupulumutsa.”

23Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;

fuwula, iwe dziko lapansi.

Imbani nyimbo, inu mapiri,

inu nkhalango ndi mitengo yonse,

chifukwa Yehova wawombola Yakobo,

waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24Yehova Mpulumutsi wanu, amene

anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,

amene anapanga zinthu zonse,

ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,

ndinayala ndekha dziko lapansi.

25Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,

ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.

Ndimasokoneza anthu a nzeru,

ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.

26Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake

ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.

Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.

Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.

27Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’

ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.

28Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’

ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;

iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’

ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”

New International Version

Isaiah 44:1-28

Israel the Chosen

1“But now listen, Jacob, my servant,

Israel, whom I have chosen.

2This is what the Lord says—

he who made you, who formed you in the womb,

and who will help you:

Do not be afraid, Jacob, my servant,

Jeshurun,44:2 Jeshurun means the upright one, that is, Israel. whom I have chosen.

3For I will pour water on the thirsty land,

and streams on the dry ground;

I will pour out my Spirit on your offspring,

and my blessing on your descendants.

4They will spring up like grass in a meadow,

like poplar trees by flowing streams.

5Some will say, ‘I belong to the Lord’;

others will call themselves by the name of Jacob;

still others will write on their hand, ‘The Lord’s,’

and will take the name Israel.

The Lord, Not Idols

6“This is what the Lord says—

Israel’s King and Redeemer, the Lord Almighty:

I am the first and I am the last;

apart from me there is no God.

7Who then is like me? Let him proclaim it.

Let him declare and lay out before me

what has happened since I established my ancient people,

and what is yet to come—

yes, let them foretell what will come.

8Do not tremble, do not be afraid.

Did I not proclaim this and foretell it long ago?

You are my witnesses. Is there any God besides me?

No, there is no other Rock; I know not one.”

9All who make idols are nothing,

and the things they treasure are worthless.

Those who would speak up for them are blind;

they are ignorant, to their own shame.

10Who shapes a god and casts an idol,

which can profit nothing?

11People who do that will be put to shame;

such craftsmen are only human beings.

Let them all come together and take their stand;

they will be brought down to terror and shame.

12The blacksmith takes a tool

and works with it in the coals;

he shapes an idol with hammers,

he forges it with the might of his arm.

He gets hungry and loses his strength;

he drinks no water and grows faint.

13The carpenter measures with a line

and makes an outline with a marker;

he roughs it out with chisels

and marks it with compasses.

He shapes it in human form,

human form in all its glory,

that it may dwell in a shrine.

14He cut down cedars,

or perhaps took a cypress or oak.

He let it grow among the trees of the forest,

or planted a pine, and the rain made it grow.

15It is used as fuel for burning;

some of it he takes and warms himself,

he kindles a fire and bakes bread.

But he also fashions a god and worships it;

he makes an idol and bows down to it.

16Half of the wood he burns in the fire;

over it he prepares his meal,

he roasts his meat and eats his fill.

He also warms himself and says,

“Ah! I am warm; I see the fire.”

17From the rest he makes a god, his idol;

he bows down to it and worships.

He prays to it and says,

“Save me! You are my god!”

18They know nothing, they understand nothing;

their eyes are plastered over so they cannot see,

and their minds closed so they cannot understand.

19No one stops to think,

no one has the knowledge or understanding to say,

“Half of it I used for fuel;

I even baked bread over its coals,

I roasted meat and I ate.

Shall I make a detestable thing from what is left?

Shall I bow down to a block of wood?”

20Such a person feeds on ashes; a deluded heart misleads him;

he cannot save himself, or say,

“Is not this thing in my right hand a lie?”

21“Remember these things, Jacob,

for you, Israel, are my servant.

I have made you, you are my servant;

Israel, I will not forget you.

22I have swept away your offenses like a cloud,

your sins like the morning mist.

Return to me,

for I have redeemed you.”

23Sing for joy, you heavens, for the Lord has done this;

shout aloud, you earth beneath.

Burst into song, you mountains,

you forests and all your trees,

for the Lord has redeemed Jacob,

he displays his glory in Israel.

Jerusalem to Be Inhabited

24“This is what the Lord says—

your Redeemer, who formed you in the womb:

I am the Lord,

the Maker of all things,

who stretches out the heavens,

who spreads out the earth by myself,

25who foils the signs of false prophets

and makes fools of diviners,

who overthrows the learning of the wise

and turns it into nonsense,

26who carries out the words of his servants

and fulfills the predictions of his messengers,

who says of Jerusalem, ‘It shall be inhabited,’

of the towns of Judah, ‘They shall be rebuilt,’

and of their ruins, ‘I will restore them,’

27who says to the watery deep, ‘Be dry,

and I will dry up your streams,’

28who says of Cyrus, ‘He is my shepherd

and will accomplish all that I please;

he will say of Jerusalem, “Let it be rebuilt,”

and of the temple, “Let its foundations be laid.” ’