Yesaya 44 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 44:1-28

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

1Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Israeli, amene ndinakusankha.

2Yehova

amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,

ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,

Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Yesuruni, amene ndinakusankha.

3Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,

ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;

ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,

ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.

4Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino

ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.

5Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’

wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;

winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’

ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

6“Yehova Mfumu

ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:

Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;

palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.

7Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.

Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe

zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,

ndi ziti zimene zidzachitike;

inde, muloleni alosere zimene zikubwera.

8Musanjenjemere, musachite mantha.

Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?

Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?

Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

9Onse amene amapanga mafano ngachabe,

ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.

Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;

ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.

10Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,

limene silingamupindulire?

11Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;

amisiri a mafano ndi anthu chabe.

Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;

onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo

ndipo amachiyika pa makala amoto;

ndi dzanja lake lamphamvu

amachisula pochimenya ndi nyundo.

Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;

iye samwa madzi, ndipo amalefuka.

13Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe

ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;

amasema bwinobwino ndi chipangizo chake

ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.

Amachipanga ngati munthu,

munthu wake wokongola

kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.

14Amagwetsa mitengo ya mkungudza,

mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu

nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,

ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.

15Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;

nthambi zina amasonkhera moto wowotha,

amakolezera moto wophikira buledi

ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;

iye amapanga fano ndi kumaligwadira.

16Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto

wowotcherapo nyama imene

amadya, nakhuta.

Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,

“Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”

17Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;

amaligwadira ndi kulipembedza.

Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,

“Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”

18Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;

maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,

ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.

19Palibe amene amayima nʼkulingalira.

Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,

chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;

pa makala ake ndinaphikira buledi,

ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.

Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.

Kodi ndidzagwadira mtengo?

20Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;

motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,

“Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi

popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.

Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;

iwe Israeli, sindidzakuyiwala.

22Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,

ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.

Bwerera kwa Ine,

popeza ndakupulumutsa.”

23Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;

fuwula, iwe dziko lapansi.

Imbani nyimbo, inu mapiri,

inu nkhalango ndi mitengo yonse,

chifukwa Yehova wawombola Yakobo,

waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24Yehova Mpulumutsi wanu, amene

anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,

amene anapanga zinthu zonse,

ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,

ndinayala ndekha dziko lapansi.

25Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,

ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.

Ndimasokoneza anthu a nzeru,

ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.

26Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake

ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.

Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.

Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.

27Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’

ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.

28Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’

ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;

iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’

ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 44:1-28

以色列蒙拣选

1“我的仆人雅各

我所拣选的以色列啊,

现在你要留心听。

2造你、使你在母胎中成形、

帮助你的耶和华说,

‘我的仆人雅各

我所拣选的耶书仑44:2 耶书仑”是以色列的昵称。啊,

不要害怕。

3我要用水浇灌干渴之地,

使河流滋润干旱之土。

我要用我的灵浇灌你的后裔,

使我的福泽临到你的子孙。

4他们要滋长如青草,

又如溪旁杨柳。’

5这个说,‘我属于耶和华’,

那个说,‘我是雅各的子孙’,

还有人手上写着,‘耶和华之民’,

称自己属于以色列

6“耶和华,以色列的君王和救赎主,

万军之耶和华说,

‘我是首先的,我是末后的,

除我以外再没有真神。

7谁能与我相比?让他告诉我。

自从我设立这古老的民族以来所发生的事和将要发生的事,

让他告诉我。

8不要恐惧,不要害怕,

我不是早已告诉过你们吗?

你们是我的证人。

除我以外还有真神吗?

没有,没有别的磐石,

一个也没有。’”

9制造偶像的真是无用,他们珍爱的偶像毫无价值。拜神像的人目盲眼瞎,愚昧无知,自找羞辱。 10制造神像、雕刻无益偶像的是谁? 11看啊,制造神像的工匠不过是人,他们必羞愧。让他们一起来对质吧,他们必恐惧、羞愧。 12铁匠把铁块放在炭火里烧,用他强壮的臂膀挥动铁锤把它打成偶像。他饥饿时就会无力,口渴时就会疲乏。 13木匠拉线测量木料,用笔勾出形状,用圆规画出模样,仿照人的样子用凿子做成逼真的神像,放在庙宇里。 14他砍伐香柏木,或从林中选取柏木和橡木。他栽种松树,雨水使它长大。 15这树可以用来作燃料,他取一些木料生火取暖、烤饼,又制成神像来祭拜,雕成偶像来叩拜。 16他用一半木头烤肉,饱餐一顿,并用火取暖,说:“啊!我这里有火,真暖和。” 17他用另一半木头造了一个神,一个偶像,向它俯伏叩拜、祷告说:“你是我的神明,求你拯救我。” 18他们愚昧无知,因为眼睛被封住以致看不见,心窍被塞住以致不明白。 19他们无人思想,无人明白,无人醒悟说:“我用一半木头当柴烤饼、烤肉吃,我岂能用另一半木头造可憎的神像?我岂能向一块木头叩拜?” 20他们以灰为食,心智迷糊,走入歧途,不能自救,也不会说:“我右手拿的神像不是假的吗?”

耶和华救赎以色列

21雅各啊,以色列啊,

要记住这些事,

因为你是我的仆人。

我造了你,你是我的仆人;

以色列啊,我不会忘记你。

22我除去了你的过犯和罪恶,

使它们如云雾消散。

归向我吧,因为我救赎了你。”

23诸天啊,歌唱吧!

因为耶和华成就了这事。

地的深处啊,欢呼吧!

众山岭和林中的树木啊,

你们都要歌唱!

因为耶和华救赎了雅各

以色列彰显了祂的荣耀。

24在母腹中造你、救赎你的耶和华说:

“我是创造万物的耶和华,

我独自铺展穹苍,开辟大地。

25我使假先知的预兆无法应验,

使占卜者丑态百出;

我颠覆智者的知识,

使之愚不可及。

26我使我仆人的话应验,

使我使者的计划成就。

我说耶路撒冷必有人居住,

我说犹大的城邑必重建起来,

从废墟中重建起来。

27我对深海说,‘枯干吧!

我要使你的河流干涸’;

28我说塞鲁士是我的牧人,

他必完成我的旨意,

他会下令重建耶路撒冷

降旨奠定圣殿的根基。