Yesaya 43 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 43:1-28

Yehova Yekha Mpulumutsi wa Israeli

1Koma tsopano, Yehova

amene anakulenga, iwe Yakobo,

amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,

“Usaope, pakuti ndakuwombola;

Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.

2Pamene ukuwoloka nyanja,

ndidzakhala nawe;

ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,

sidzakukokolola.

Pamene ukudutsa pa moto,

sudzapsa;

lawi la moto silidzakutentha.

3Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,

Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.

Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,

ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.

4Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga,

ndipo chifukwa ndimakukonda,

ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe,

ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.

5Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe;

ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa,

ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.

6Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’

ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’

Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali,

ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;

7onsewo amadziwika ndi dzina langa;

ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga,

ndinawawumba, inde ndinawapanga.”

8Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya,

anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.

9Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi,

anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu.

Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi?

Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale?

Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona,

kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”

10Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga,

ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha,

kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha.

Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina,

ngakhale pambuyo panga

sipadzakhalaponso wina.”

11Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova,

ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.

12Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa;

ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu.

Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.

13“Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse.

Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga,

ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”

Chifundo cha Mulungu ndi Kusakhulupirika kwa Israeli

14Yehova akuti,

Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti,

“Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni

ndi kukupulumutsani.

Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.

15Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja,

Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”

16Yehova

anapanga njira pa nyanja,

anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.

17Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo,

gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu,

ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso

anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,

18“Iwalani zinthu zakale;

ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.

19Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano!

Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona?

Ine ndikulambula msewu mʼchipululu

ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.

20Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi

zinandilemekeza.

Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma

kuti ndiwapatse madzi anthu anga

osankhidwa.

21Anthu amene ndinadziwumbira ndekha

kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.

22“Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo,

munatopa nane, Inu Aisraeli.

23Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza,

kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu.

Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya

kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.

24Simunandigulire bango lonunkhira

kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu.

Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu

ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.

25“Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza

zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini,

ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.

26Mundikumbutse zakale,

ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi;

fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.

27Kholo lanu loyamba linachimwa;

ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.

28Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero,

ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe

ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

La Bible du Semeur

Esaïe 43:1-28

Un seul Sauveur pour Israël

1Maintenant, l’Eternel ╵qui t’a créé, ╵ô peuple de Jacob,

et qui t’a façonné, ╵ô Israël,

te déclare ceci :

Ne sois pas effrayé

car je t’ai délivré,

je t’ai appelé par ton nom,

tu es à moi.

2Quand tu passeras par les eaux,

je serai avec toi,

quand tu traverseras les fleuves,

ils ne te submergeront pas,

quand tu marcheras dans le feu,

il ne te fera pas de mal

et par les flammes tu ne seras pas brûlé,

3puisque moi, l’Eternel, ╵je suis ton Dieu,

le Saint d’Israël, ton Sauveur.

Je donnerai l’Egypte ╵comme rançon pour toi,

l’Ethiopie et Seba ╵en échange de toi.

4Oui, parce que tu m’es précieux,

et que tu as du prix pour moi, ╵et que je t’aime,

je donnerai des hommes ╵en échange de toi,

et des peuples contre ta vie.

5Sois donc sans crainte,

car je suis avec toi,

je ferai revenir ╵tes enfants de l’orient

je te rassemblerai ╵de l’occident.

6Je dirai au septentrion : ╵« Rends-les ! »

Et au midi : ╵« Ne les retiens donc pas !

Fais revenir mes fils ╵des pays éloignés,

fais revenir mes filles ╵des confins de la terre,

7oui, tous ceux qui portent mon nom

et que j’ai créés pour ma gloire,

que j’ai formés, oui, que j’ai faits !

8Laisse sortir le peuple ╵qui est aveugle

tout en ayant des yeux,

et qui est sourd

bien qu’il ait des oreilles ! »

Un peuple de témoins

9Que toutes les nations s’assemblent

et que les peuples se regroupent !

Qui, parmi eux, ╵avait prédit ces choses ?

Qui avait annoncé ╵les événements antérieurs ?

Qu’ils citent leurs témoins ╵et qu’ils se justifient !

Qu’on les écoute bien ╵afin de pouvoir dire :

« Oui, c’est la vérité ! »

10Mais mes témoins, c’est vous,

déclare l’Eternel,

votre peuple est le serviteur, ╵que je me suis choisi,

pour que vous le sachiez,

que vous croyiez en moi

et que vous compreniez ╵que moi seul, je suis Dieu.

Avant moi aucun dieu ╵ne fut jamais formé,

et après moi, jamais ╵il n’en existera.

11Moi, je suis l’Eternel

et, en dehors de moi, ╵il n’est pas de Sauveur.

12C’est moi qui ai prédit, ╵c’est moi qui ai sauvé, ╵je me suis fait entendre.

Pas un dieu étranger ╵ne l’a fait parmi vous,

et vous, déclare l’Eternel,

vous êtes mes témoins,

et c’est moi qui suis Dieu.

13Oui, je le suis depuis toujours

et personne ne peut ╵délivrer de ma main.

Ce que je réalise, ╵qui pourrait l’annuler ?

Dieu intervient

14Voici ce que déclare l’Eternel

votre Libérateur, ╵moi le Saint d’Israël :

C’est à cause de vous ╵que j’envoie une armée ╵combattre Babylone,

et que je fais descendre43.14 et que je fais descendre: traduction incertaine. ╵tous les Chaldéens qui s’enfuient

sur les navires mêmes ╵où ils criaient de joie.

15Moi, l’Eternel, ╵je suis votre Dieu saint,

le Créateur d’Israël, votre Roi.

Un chemin à travers le désert

16Ainsi dit l’Eternel,

qui, à travers la mer, ╵a ouvert un chemin

et, dans les grosses eaux, ╵a frayé un sentier43.16 Allusion à la traversée de la mer des Roseaux où les chars et les cavaliers du pharaon furent détruits quand Dieu a combattu contre eux (voir 51.10 ; Ex 14.28 ; 15.4).,

17qui fit sortir ╵les chars et les chevaux,

l’armée et ses guerriers.

Ils se sont tous couchés

et ne se relèveront pas,

ils se sont consumés

et ils se sont éteints ╵comme la mèche d’une lampe.

18Ne vous rappelez plus ╵les événements du passé,

ne considérez plus ╵les choses d’autrefois ;

19je vais réaliser ╵une chose nouvelle,

elle germe dès à présent,

ne la reconnaîtrez-vous pas ?

J’ouvrirai un chemin ╵à travers le désert

et je ferai jaillir ╵des fleuves dans la steppe ;

20les animaux sauvages,

les chacals, les autruches, ╵célébreront ma gloire,

car je ferai jaillir ╵de l’eau dans le désert,

des fleuves dans la steppe,

pour abreuver mon peuple, ╵celui que j’ai élu.

21Je l’ai formé pour moi :

il proclamera ma louange.

Dieu accuse

22Et pourtant, ô Jacob, ╵tu n’as pas fait appel à moi !

Tu t’es lassé de moi, ╵ô Israël !

23Tu ne m’as pas offert ╵d’agneaux en holocaustes,

tes sacrifices ╵n’étaient pas à ma gloire ;

je ne t’ai pas importuné ╵pour avoir des offrandes,

je ne t’ai pas lassé ╵pour avoir de l’encens.

24Tu n’as pas dépensé d’argent pour moi, ╵pour du roseau aromatique,

et tu ne m’as pas rassasié ╵de la graisse des sacrifices.

Mais toi, tu m’as importuné ╵par tes péchés,

tu m’as lassé ╵par tes forfaits !

Dieu pardonne

25Mais c’est moi, et moi seul, ╵qui efface tes transgressions ╵par égard pour moi-même,

je ne tiendrai plus compte ╵de tes péchés.

26Rappelle-moi ce qu’il en est, ╵entrons ensemble en jugement

et, pour te justifier, ╵expose donc ton cas.

27Déjà, ton premier père43.27 Jacob très certainement (voir Gn 25.26 ; 27.36 ; Os 12.4). ╵a péché envers moi

et ceux des tiens qui ont la charge ╵d’interpréter la Loi ╵m’ont été infidèles.

28Aussi ai-je déshonoré

les chefs du sanctuaire

et j’ai livré Jacob ╵à l’extermination,

Israël aux outrages.