Yesaya 41 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 41:1-29

Mulungu Thandizo la Israeli

1“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!

Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;

tiyeni tikhale pamodzi

kuti atiweruze.

2“Ndani anadzutsa wochokera kummawa

uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?

Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake

ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa

ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi

nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.

3Amawalondola namayenda mosavutika,

mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.

4Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,

si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?

Ine Yehova, ndine chiyambi

ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”

5Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;

anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.

Akuyandikira pafupi, akubwera;

6aliyense akuthandiza mnzake

ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”

7Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,

ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo

amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.

Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”

Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.

8“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,

Yakobo amene ndakusankha,

Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.

9Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,

ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.

Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’

Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.

10Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;

usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.

Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,

ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

11“Onse amene akupsera mtima

adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;

onse amene akukangana nawe

sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.

12Udzafunafuna adani ako,

koma sadzapezeka.

Iwo amene akuchita nawe nkhondo

sadzakhalanso kanthu.

13Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,

amene ndikukugwira dzanja lako lamanja

ndipo ndikuti, usaope;

ndidzakuthandiza.

14Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,

iwe wochepa mphamvu Israeli,

chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”

akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.

15“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu

chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.

Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,

ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.

16Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso

adzamwazika ndi kamvuluvulu.

Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,

ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:

17“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,

koma sakuwapeza;

ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.

Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;

Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.

18Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,

ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.

Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi

ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.

19Mʼchipululu ndidzameretsa

mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi.

Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo

ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,

20kuti anthu aone ndi kudziwa;

inde, alingalire ndi kumvetsa,

kuti Yehova ndiye wachita zimenezi;

kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.

21“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’

Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’

22Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze

zomwe zidzachitike mʼtsogolo.

Tifotokozereni zinthu zamakedzana

tiziganizire

ndi kudziwa zotsatira zake.

Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,

23tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,

ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu.

Chitani chinthu chabwino kapena choyipa,

ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.

24Koma inu sindinu kanthu

ndipo zochita zanu nʼzopandapake;

amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.

25“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,

munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana.

Amapondaponda olamulira ngati matope,

ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.

26Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,

kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’

Palibe amene ananena,

palibe analengeza zimenezi,

palibe anamva mawu anu.

27Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’

Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.

28Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,

palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu,

palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.

29Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!

Zochita zawo si kanthu konse;

mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

Hoffnung für Alle

Jesaja 41:1-29

Der Herr fordert die Götter heraus

1So spricht der Herr: »Ihr Bewohner der Inseln und der fernen Küsten, seid still und hört mir zu! Nehmt euren ganzen Mut zusammen, ihr Völker, und kommt her! Hier könnt ihr eure Sache vorbringen. Lasst uns die Gerichtsverhandlung beginnen.

2Wer hat den Mann aus dem Osten41,2 Gemeint ist der persische König Kyrus. Vgl. Kapitel 44,28–45,5; 46,11; 48,14‒16. berufen, um für Gerechtigkeit einzutreten? Wer verhilft ihm zum Sieg über ganze Völker? Wer lässt ihn Könige stürzen, sie mit seinen Waffen bezwingen und wie Staub und Spreu durch die Luft wirbeln? 3Er scheint zu fliegen, wenn er ihnen nachjagt. Seine Füße berühren kaum den Boden. Niemand kann ihm Schaden zufügen. 4Wer steht dahinter, wer bewirkt das alles? Es ist derselbe, der von Anfang an die Geschichte der Menschheit gelenkt hat: ich, der Herr! Vor der ersten Generation war ich schon da, und auch bei der letzten bin ich noch derselbe.«

5Als die Bewohner der Inseln und der fernen Länder sahen, was geschah, bekamen sie es mit der Angst zu tun. Zitternd liefen sie zusammen. 6Einer hilft nun dem anderen, gegenseitig sprechen sie sich Mut zu. 7Sie setzen ihre Hoffnung auf eine neue Götterstatue. Der Kunsthandwerker glättet die gegossene Figur mit dem Hammer und fordert den Goldschmied auf: »Beeil dich!« Der hämmert das Goldblech und überzieht damit sorgfältig die Statue. »Das wird gut halten«, sagt er. Schließlich wird das Standbild auf einem Sockel festgenagelt, damit es nicht wackelt.

Hab keine Angst, denn ich bin dein Gott

8Der Herr sagt: »Israel, du bist das Volk, das mir dient. Du Nachkommenschaft Jakobs, dich habe ich erwählt. Du stammst von meinem Freund Abraham ab, 9dich allein habe ich vom Ende der Erde herbeigeholt. Von weit her habe ich dich gerufen und zu dir gesagt: ›Du sollst mir dienen!‹ Dich habe ich erwählt und nicht verstoßen. 10Fürchte dich nicht, denn ich stehe dir bei; hab keine Angst, denn ich bin dein Gott! Ich mache dich stark, ich helfe dir, mit meiner siegreichen Hand41,10 Wörtlich: mit der rechten Hand meiner Gerechtigkeit. beschütze ich dich! 11Alle, die voller Wut gegen dich toben, werden am Ende in Schimpf und Schande dastehen. Die Männer, die dich bekämpfen, werden zugrunde gehen. Niemand redet dann mehr von ihnen. 12Vergeblich wirst du dich umsehen nach denen, die Krieg mit dir führten – du wirst sie nicht mehr finden. Wo sind sie geblieben, deine Feinde? Sie sind verschwunden, als ob es sie nie gegeben hätte. 13Denn ich bin der Herr, dein Gott. Ich nehme dich an deiner rechten Hand und sage: Hab keine Angst! Ich helfe dir.

14Israel, du kleines Volk, das von Jakob abstammt, hab keine Angst, auch wenn du schwach und hilflos bist. Ich helfe dir; ich, der Herr, der heilige Gott Israels, bin dein Erlöser. 15Ich mache dich zu einem neuen Dreschschlitten mit scharfen Zähnen. Berge und Hügel wirst du dreschen und zu Staub zermalmen. 16Du wirst sie mit einer Schaufel in die Luft werfen wie Getreide, damit der Wind sie wie Spreu fortträgt und in alle Himmelsrichtungen zerstreut. Du aber wirst jubeln über mich, den Herrn; den heiligen Gott Israels wirst du rühmen.«

Gott gibt Wasser in der Wüste

17Der Herr sagt: »Mein Volk steckt tief im Elend. Sie suchen Wasser, aber finden keins. Vor Durst klebt ihnen die Zunge am Gaumen. Doch ich, der Herr, antworte auf ihre Hilfeschreie. Ich bin der Gott Israels und lasse mein Volk nicht im Stich. 18Auf den kahlen Hügeln lasse ich Bäche hervorbrechen, und in öden Tälern sollen Quellen entspringen. Ich verwandle die Wüste in fruchtbares Land mit Teichen und sprudelnden Quellen. 19Viele Bäume pflanze ich dort an: Zedern, Akazien und Myrten, Ölbäume und Wacholder, Platanen und Zypressen. 20Wer das sieht, wird erkennen, dass ich, der Herr, hier eingegriffen habe; jeder soll wissen: Der heilige Gott Israels hat dies alles gemacht.«

Die Götter sind nichts und können nichts

21Der Herr, der König Israels, sagt zu den Göttern der Völker: »Jetzt habt ihr Gelegenheit, euch vor Gericht zu verteidigen. Legt eure Beweise vor! 22Zeigt eure Macht und lasst uns wissen, was sich alles ereignet. Ihr wisst doch, was in der Vergangenheit geschah. Was hat es zu bedeuten? Erklärt es uns, damit wir es verstehen können! Oder sagt uns jetzt die Zukunft voraus, damit wir sehen, ob es eintrifft. 23Kündigt an, was einmal geschehen wird, damit wir erkennen, dass ihr Götter seid! Sagt uns, was kommt, ganz gleich ob es etwas Gutes oder Schlimmes ist. Dann werden wir große Achtung vor euch haben. 24Aber dazu seid ihr gar nicht in der Lage: Ihr seid nichts und könnt nichts! Wer euch verehrt, ist mir zuwider.

25Ich habe den Mann aus dem Norden berufen und auf den Weg geschickt. Er, der meinen Namen anruft, tritt seinen Siegeszug an und stürmt von Osten herbei. Er wird mächtige Fürsten wie Lehmklumpen zertreten, so wie ein Töpfer den Ton stampft und knetet. 26Hat etwa einer von euch Göttern das lange Zeit im Voraus angekündigt, so dass man es wiedererkennt, wenn es eintrifft? Dann hätten wir gerufen: ›Richtig, so hat er es vorausgesagt!‹ Aber keiner hat es prophezeit, keiner hat es angekündigt. Niemand hörte von euch auch nur ein einziges Wort darüber! 27Ich bin der Erste und Einzige, der Jerusalem die Befreiung durch diesen Mann angekündigt hat. Ich schickte einen Boten mit dieser frohen Nachricht zum Berg Zion.

28Doch wenn ich diese Götter anschaue, so finde ich keinen, den ich um Rat fragen könnte. Von keinem einzigen kann ich eine Antwort erwarten. 29Sie alle sind nichts als ein großer Betrug. Gar nichts bringen sie zustande. In ihren Statuen ist kein Leben. Diese Götter sind hohl und leer!«