Mulungu Thandizo la Israeli
1“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!
Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;
tiyeni tikhale pamodzi
kuti atiweruze.
2“Ndani anadzutsa wochokera kummawa
uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?
Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake
ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa
ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi
nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3Amawalondola namayenda mosavutika,
mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,
si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?
Ine Yehova, ndine chiyambi
ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;
anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.
Akuyandikira pafupi, akubwera;
6aliyense akuthandiza mnzake
ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,
ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo
amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.
Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”
Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,
Yakobo amene ndakusankha,
Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,
ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.
Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’
Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;
usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.
Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,
ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11“Onse amene akupsera mtima
adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;
onse amene akukangana nawe
sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12Udzafunafuna adani ako,
koma sadzapezeka.
Iwo amene akuchita nawe nkhondo
sadzakhalanso kanthu.
13Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,
amene ndikukugwira dzanja lako lamanja
ndipo ndikuti, usaope;
ndidzakuthandiza.
14Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,
iwe wochepa mphamvu Israeli,
chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”
akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu
chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.
Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,
ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso
adzamwazika ndi kamvuluvulu.
Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,
ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,
koma sakuwapeza;
ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.
Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;
Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,
ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.
Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi
ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19Mʼchipululu ndidzameretsa
mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi.
Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo
ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20kuti anthu aone ndi kudziwa;
inde, alingalire ndi kumvetsa,
kuti Yehova ndiye wachita zimenezi;
kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’
Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze
zomwe zidzachitike mʼtsogolo.
Tifotokozereni zinthu zamakedzana
tiziganizire
ndi kudziwa zotsatira zake.
Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,
ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu.
Chitani chinthu chabwino kapena choyipa,
ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24Koma inu sindinu kanthu
ndipo zochita zanu nʼzopandapake;
amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,
munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana.
Amapondaponda olamulira ngati matope,
ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,
kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’
Palibe amene ananena,
palibe analengeza zimenezi,
palibe anamva mawu anu.
27Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’
Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,
palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu,
palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!
Zochita zawo si kanthu konse;
mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.
L’Eternel suscite un Libérateur
Le grand Vainqueur
1Tenez-vous en silence ╵devant moi, vous, les îles ╵et les régions côtières !
Que les peuples lointains ╵raniment leur courage :
qu’ils approchent, qu’ils parlent !
Oui, allons ensemble en justice.
2Qui a fait lever de l’orient
celui que la justice41.2 Il s’agit de Cyrus, roi des Perses. Il est devenu le roi des Mèdes en 549 av. J.-C. puis s’est emparé de Babylone en 539 (voir 41.25 ; 44.28 ; etc.). ╵entraîne sur ses pas ?
Qui lui a livré les nations
et qui a abaissé des rois ?
Son épée pulvérise ╵les peuples devant lui
et son arc les disperse ╵comme un fétu de paille ╵emporté par le vent.
3Il les poursuit ╵et va plus loin, indemne,
par un chemin ╵que son pied n’avait pas foulé ╵auparavant.
4Qui accomplit cela ? ╵Qui le fait arriver ?
Qui appelle à la vie
les générations d’hommes ╵dès le commencement ?
Moi, l’Eternel, ╵moi, qui suis le premier
et qui suis avec les derniers, ╵oui, c’est bien moi !
5Les habitants des îles ╵et des régions côtières ╵ont vu ce que j’ai fait ╵et sont saisis de crainte ;
ceux qui ont pour demeure ╵les confins de la terre ╵se sont mis à trembler.
Ils approchent, ils viennent,
6ils s’aident mutuellement,
chacun dit à son frère : ╵« Courage ! »
7L’artisan encourage le fondeur.
Le polisseur soutient ╵celui qui bat l’enclume.
Il dit de la soudure : ╵« Voilà du bon travail ! »
Et il fixe l’idole avec des clous
afin qu’elle ne bouge pas.
L’Eternel délivre Israël
8Quant à toi, Israël, ╵mon serviteur,
Jacob, que j’ai choisi,
et descendance d’Abraham, ╵qui était mon ami,
9toi que je suis allé chercher ╵aux confins de la terre
et que j’ai appelé ╵de ses extrémités,
toi à qui j’avais dit :
« Tu es mon serviteur »,
je t’ai choisi
et non pas rejeté.
10Ne sois pas effrayé,
car je suis avec toi ;
ne sois pas angoissé,
car moi je suis ton Dieu.
Je t’affermis,
je viens à ton secours,
pour sûr, je te soutiens ╵de mon bras droit ╵qui fait justice.
11Tous ceux qui sont irrités contre toi,
sombreront dans la honte ╵et dans le déshonneur.
Tes adversaires ╵seront réduits à rien, ╵ils périront.
12Tu auras beau chercher, ╵tu ne trouveras plus
ceux qui te querellaient.
Ils seront tous anéantis, ╵réduits à rien
ceux qui t’ont fait la guerre.
13Car c’est moi, l’Eternel, ╵qui suis ton Dieu,
je saisis ta main droite,
je te dis : Sois sans crainte,
je suis là pour t’aider.
14Sois donc sans crainte, ╵vermisseau de Jacob,
ô petit Israël,
car je viens à ton aide,
l’Eternel le déclare ;
celui qui te délivre ╵c’est le Saint d’Israël.
15Voici je fais de toi
un traîneau de battage ╵tout neuf,
armé de pointes,
tu battras les montagnes, ╵tu les broieras,
tu rendras les collines ╵semblables à la paille.
16Oui, tu les vanneras,
et le vent les emportera,
l’ouragan les dispersera.
Mais toi, tu placeras ta joie ╵en l’Eternel,
et ta fierté ╵dans le Saint d’Israël.
17Les opprimés, les pauvres
cherchent de l’eau sans en trouver,
et la soif dessèche leur langue.
Moi, l’Eternel, ╵je les exaucerai,
moi, le Dieu d’Israël, ╵je ne les délaisserai pas.
18Je ferai sourdre des rivières ╵du sommet des montagnes
et je ferai jaillir des sources ╵au milieu des vallées,
je transformerai le désert ╵en étang rempli d’eau
et le pays aride ╵en sources jaillissantes.
19Je planterai dans le désert ╵le cèdre et l’acacia,
le myrte et l’olivier.
Je ferai croître dans la steppe
le cyprès, le pin et le buis,
20pour que tous voient et reconnaissent,
et qu’ils observent, qu’ils comprennent,
que c’est la main de l’Eternel ╵qui a fait tout cela,
que le Saint d’Israël ╵en est le créateur.
L’Eternel en face des faux dieux
21Vous, dieux des autres peuples, ╵présentez votre cause,
dit l’Eternel,
et exposez vos arguments,
dit le roi de Jacob.
22Qu’ils les exposent donc,
qu’ils nous annoncent
ce qui doit arriver !
Déclarez-nous ╵quels sont les faits passés ╵que vous avez prédits,
pour que nous les examinions
et que nous constations ╵leur accomplissement,
ou faites-nous entendre ╵ce qui doit arriver !
23Annoncez-nous ╵les événements à venir,
et nous saurons ╵que vous êtes des dieux.
Oui, faites quelque chose, ╵que ce soit bien ou mal,
afin qu’en le voyant
la crainte nous remplisse41.23 afin qu’en le voyant: autre traduction : afin que nous soyons terrifiés. la crainte nous remplisse: divers manuscrits et versions anciennes ont : que nous le voyons..
24Mais vous, vous êtes moins que rien !
Et toutes vos actions ╵sont moins que du néant !
Celui qui vous choisit ╵commet une abomination.
25Du nord, je fais surgir un homme,
il va venir, ╵oui, du soleil levant41.25 D’après les versions anciennes. Le texte hébreu traditionnel a : il viendra du soleil levant.,
il est appelé par son nom,
il piétine les gouverneurs ╵comme s’ils étaient de la boue,
comme un potier foule l’argile.
26Qui a prédit cela ╵dès le commencement
pour que nous le sachions ?
Qui donc l’a annoncé ╵bien longtemps à l’avance
afin que nous disions : « C’est juste ? »
Non, personne ne l’a prédit,
personne n’a rien annoncé
et personne n’a entendu ╵des paroles venant de vous.
27Mais moi, j’ai été le premier ╵qui ai dit à Sion :
« Les voici ! Les voici ! »
J’ai donné à Jérusalem ╵un messager, ╵porteur de la bonne nouvelle.
28Alors que, parmi ces dieux-là,
j’ai eu beau regarder, ╵je n’ai trouvé personne, ╵pas un seul conseiller,
personne pour répondre ╵si je les interroge.
29Eux tous, ils ne sont rien41.29 D’après le texte hébreu de Qumrân et la version syriaque. Le texte hébreu traditionnel a : ils sont iniques.,
leurs œuvres sont néant,
et leurs statues de fonte : ╵du vent, du vide.