Yesaya 40 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 40:1-31

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

1Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,

akutero Mulungu wanu.

2Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu

ndipo muwawuzitse

kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,

tchimo lawo lakhululukidwa.

Ndawalanga mokwanira

chifukwa cha machimo awo onse.

3Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,

“Konzani njira ya Yehova

mʼchipululu;

wongolani njira zake;

msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.

4Chigwa chilichonse achidzaze.

Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;

Dziko lokumbikakumbika alisalaze,

malo azitundazitunda awasandutse zidikha.

5Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,

ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,

pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

6Wina ananena kuti, “Lengeza.”

Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu

ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.

7Udzu umanyala ndipo maluwa amafota

chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”

Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.

8Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,

koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

9Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,

kwera pa phiri lalitali.

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,

fuwula kwambiri,

kweza mawu, usachite mantha;

uza mizinda ya ku Yuda kuti,

“Mulungu wanu akubwera!”

10Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,

ndipo dzanja lake likulamulira,

taonani akubwera ndi mphotho yake

watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.

11Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:

Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake

ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake

ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,

kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?

Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,

kapena kuyeza kulemera kwa

mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?

13Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova

kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?

14Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,

kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?

Iye anapempha nzeru kwa yani

ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.

Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;

mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.

16Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,

ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.

17Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;

Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu

ndi cha chabechabe.

18Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?

Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

19Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga

ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide

naliveka mkanda wasiliva.

20Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere

amasankha mtengo umene sudzawola,

nafunafuna mʼmisiri waluso woti

amupangire fano limene silingasunthike.

21Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?

Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?

22Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,

Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.

Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,

nayikunga ngati tenti yokhalamo.

23Amatsitsa pansi mafumu amphamvu

nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.

24Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene

kapena kufesedwa chapompano,

ndi kungoyamba kuzika mizu kumene

ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa

ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?

Kapena kodi alipo wofanana nane?”

26Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.

Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?

Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,

nayitana iliyonse ndi dzina lake.

Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,

palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena

ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,

“Yehova sakudziwa mavuto anga,

Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”

28Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,

ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.

Iye sadzatopa kapena kufowoka

ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.

29Iye amalimbitsa ofowoka

ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.

30Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,

ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;

31koma iwo amene amakhulupirira Yehova

adzalandira mphamvu zatsopano.

Adzawuluka ngati chiwombankhanga;

adzathamanga koma sadzalefuka,

adzayenda koma sadzatopa konse.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 40:1-31

上帝對祂子民的安慰

1你們的上帝說:

「你們要安慰我的子民。

2要溫柔地告訴耶路撒冷

她的苦難已經結束,

她的罪惡已經被除去。

她因自己的一切罪已受到耶和華加倍的懲罰40·2 她因自己的一切罪已受到耶和華加倍的懲罰」或譯「她的一切罪已得到耶和華雙倍的赦免」。。」

3聽啊,有人高喊:

「在曠野預備耶和華的道,

在沙漠修直我們上帝的路。

4一切山谷將被填滿,

大山小丘將被削平;

坎坷之地將變得平坦,

崎嶇的地面將成為平原。

5耶和華的榮耀必彰顯,

世人必一同看見。

這是耶和華親口說的。」

6有聲音說:「呼喊吧!」

我問道:「我呼喊什麼呢?」

那聲音說:「芸芸眾生盡如草,

榮華富貴像野地的花。

7耶和華吹一口氣,

草就枯乾,花也凋殘。

人類誠然像草。

8草必枯乾,花必凋殘,

唯有我們上帝的話永遠長存。」

9錫安報告好消息的人啊,

要登上高山!

耶路撒冷報告好消息的人啊,

要大聲宣告!

要提高聲音,不要懼怕!

要高聲對猶大的城邑說:

「你們的上帝來了!」

10看啊,主耶和華帶著能力來了,

祂的臂膀執掌王權;

祂帶著賞賜而來,

要酬勞祂的子民。

11祂像牧人一樣牧養自己的羊群,

用臂膀把羊羔聚在一起,

抱在懷中,

溫柔地引導母羊。

12誰曾用手心量海水?

誰曾用手掌度蒼天?

誰曾用升斗盛大地的塵土?

誰曾用秤稱高山,用天平稱丘陵?

13誰曾測度耶和華的心?

誰曾做祂的謀士指點祂?

14祂請教過誰?

誰教過祂正道?

誰教過祂知識?

誰指點過祂領悟之道?

15看啊,列國就像水桶中的一滴水,

又如天平上的塵埃。

祂舉起眾海島,好像捧起微塵。

16黎巴嫩的樹木不夠作獻祭的燃料,

林中的走獸也不夠作燔祭。

17萬國在祂面前都算不得什麼,

在祂看來不過是虛無。

18你們拿誰與上帝相比呢?

你們用什麼形像比作上帝呢?

19偶像是工匠製造的,

銀匠替它包上金子、打造銀鏈。

20買不起這種偶像的人就選一塊耐用的木頭,

找個精巧的工匠,

雕出一個可以站立不倒的偶像。

21難道你們不知道嗎?

難道你們沒有聽過嗎?

難道不是從起初就告訴過你們嗎?

難道從大地奠立根基以來,

你們一直沒有明白嗎?

22上帝的寶座設立在大地的圓圈之上,

地上的人類好像蚱蜢。

祂鋪展諸天,就像鋪展幔子、鋪展人居住的帳篷。

23祂使掌權者歸於無有,

使世上的審判官化為虛無。

24他們像草一樣剛被栽上,

剛被種上,

剛在土裡扎根,

上帝一口氣吹來,便都枯乾了,

暴風將他們像禾稭一樣吹去。

25那位聖者說:「你們拿誰與我相比,

使之與我同等呢?」

26你們向天舉目,

看看是誰創造了這萬象?

是誰把眾星一一領出來,

給它們取名?

祂的權柄和能力極大無比,

它們一個也不會少。

27雅各啊,你怎能說耶和華看不見你的遭遇呢?

以色列啊,你怎能說上帝並不顧念你的冤情呢?

28難道你不知道?

難道你沒有聽見過?

永恆的上帝耶和華——創造地極的主宰不會疲乏也不會困倦,

祂的智慧深不可測。

29祂賜疲乏的人能力,

給軟弱的人力量。

30即使青年也會疲乏困倦,

強壯的人也會踉蹌跌倒;

31但仰望耶和華的人必重新得力。

他們必像鷹一樣展翅高飛,

他們奔跑也不困倦,

他們行走也不疲乏。