Yesaya 40 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 40:1-31

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

1Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,

akutero Mulungu wanu.

2Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu

ndipo muwawuzitse

kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,

tchimo lawo lakhululukidwa.

Ndawalanga mokwanira

chifukwa cha machimo awo onse.

3Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,

“Konzani njira ya Yehova

mʼchipululu;

wongolani njira zake;

msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.

4Chigwa chilichonse achidzaze.

Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;

Dziko lokumbikakumbika alisalaze,

malo azitundazitunda awasandutse zidikha.

5Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,

ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,

pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

6Wina ananena kuti, “Lengeza.”

Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu

ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.

7Udzu umanyala ndipo maluwa amafota

chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”

Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.

8Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,

koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

9Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,

kwera pa phiri lalitali.

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,

fuwula kwambiri,

kweza mawu, usachite mantha;

uza mizinda ya ku Yuda kuti,

“Mulungu wanu akubwera!”

10Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,

ndipo dzanja lake likulamulira,

taonani akubwera ndi mphotho yake

watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.

11Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:

Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake

ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake

ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,

kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?

Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,

kapena kuyeza kulemera kwa

mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?

13Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova

kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?

14Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,

kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?

Iye anapempha nzeru kwa yani

ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.

Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;

mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.

16Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,

ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.

17Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;

Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu

ndi cha chabechabe.

18Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?

Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

19Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga

ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide

naliveka mkanda wasiliva.

20Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere

amasankha mtengo umene sudzawola,

nafunafuna mʼmisiri waluso woti

amupangire fano limene silingasunthike.

21Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?

Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?

22Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,

Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.

Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,

nayikunga ngati tenti yokhalamo.

23Amatsitsa pansi mafumu amphamvu

nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.

24Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene

kapena kufesedwa chapompano,

ndi kungoyamba kuzika mizu kumene

ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa

ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?

Kapena kodi alipo wofanana nane?”

26Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.

Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?

Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,

nayitana iliyonse ndi dzina lake.

Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,

palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena

ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,

“Yehova sakudziwa mavuto anga,

Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”

28Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,

ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.

Iye sadzatopa kapena kufowoka

ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.

29Iye amalimbitsa ofowoka

ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.

30Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,

ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;

31koma iwo amene amakhulupirira Yehova

adzalandira mphamvu zatsopano.

Adzawuluka ngati chiwombankhanga;

adzathamanga koma sadzalefuka,

adzayenda koma sadzatopa konse.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 40:1-31

上帝对祂子民的安慰

1你们的上帝说:

“你们要安慰我的子民。

2要温柔地告诉耶路撒冷

她的苦难已经结束,

她的罪恶已经被除去。

她因自己的一切罪已受到耶和华加倍的惩罚40:2 她因自己的一切罪已受到耶和华加倍的惩罚”或译“她的一切罪已得到耶和华双倍的赦免”。。”

3听啊,有人高喊:

“在旷野预备耶和华的道,

在沙漠修直我们上帝的路。

4一切山谷将被填满,

大山小丘将被削平;

坎坷之地将变得平坦,

崎岖的地面将成为平原。

5耶和华的荣耀必彰显,

世人必一同看见。

这是耶和华亲口说的。”

6有声音说:“呼喊吧!”

我问道:“我呼喊什么呢?”

那声音说:“芸芸众生尽如草,

荣华富贵像野地的花。

7耶和华吹一口气,

草就枯干,花也凋残。

人类诚然像草。

8草必枯干,花必凋残,

唯有我们上帝的话永远长存。”

9锡安报告好消息的人啊,

要登上高山!

耶路撒冷报告好消息的人啊,

要大声宣告!

要提高声音,不要惧怕!

要高声对犹大的城邑说:

“你们的上帝来了!”

10看啊,主耶和华带着能力来了,

祂的臂膀执掌王权;

祂带着赏赐而来,

要酬劳祂的子民。

11祂像牧人一样牧养自己的羊群,

用臂膀把羊羔聚在一起,

抱在怀中,

温柔地引导母羊。

12谁曾用手心量海水?

谁曾用手掌度苍天?

谁曾用升斗盛大地的尘土?

谁曾用秤称高山,用天平称丘陵?

13谁曾测度耶和华的心?

谁曾做祂的谋士指点祂?

14祂请教过谁?

谁教过祂正道?

谁教过祂知识?

谁指点过祂领悟之道?

15看啊,列国就像水桶中的一滴水,

又如天平上的尘埃。

祂举起众海岛,好像捧起微尘。

16黎巴嫩的树木不够作献祭的燃料,

林中的走兽也不够作燔祭。

17万国在祂面前都算不得什么,

在祂看来不过是虚无。

18你们拿谁与上帝相比呢?

你们用什么形象比作上帝呢?

19偶像是工匠制造的,

银匠替它包上金子、打造银链。

20买不起这种偶像的人就选一块耐用的木头,

找个精巧的工匠,

雕出一个可以站立不倒的偶像。

21难道你们不知道吗?

难道你们没有听过吗?

难道不是从起初就告诉过你们吗?

难道从大地奠立根基以来,

你们一直没有明白吗?

22上帝的宝座设立在大地的圆圈之上,

地上的人类好像蚱蜢。

祂铺展诸天,就像铺展幔子、铺展人居住的帐篷。

23祂使掌权者归于无有,

使世上的审判官化为虚无。

24他们像草一样刚被栽上,

刚被种上,

刚在土里扎根,

上帝一口气吹来,便都枯干了,

暴风将他们像禾秸一样吹去。

25那位圣者说:“你们拿谁与我相比,

使之与我同等呢?”

26你们向天举目,

看看是谁创造了这万象?

是谁把众星一一领出来,

给它们取名?

祂的权柄和能力极大无比,

它们一个也不会少。

27雅各啊,你怎能说耶和华看不见你的遭遇呢?

以色列啊,你怎能说上帝并不顾念你的冤情呢?

28难道你不知道?

难道你没有听见过?

永恒的上帝耶和华——创造地极的主宰不会疲乏也不会困倦,

祂的智慧深不可测。

29祂赐疲乏的人能力,

给软弱的人力量。

30即使青年也会疲乏困倦,

强壮的人也会踉跄跌倒;

31但仰望耶和华的人必重新得力。

他们必像鹰一样展翅高飞,

他们奔跑也不困倦,

他们行走也不疲乏。