Yesaya 4 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 4:1-6

1Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri

adzagwira mwamuna mmodzi,

nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu,

ndi kuvala zovala zathu;

inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu.

Tichotseni manyazi aumbeta!”

Nthambi ya Yehova

2Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. 3Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. 4Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. 5Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. 6Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

New International Version

Isaiah 4:1-6

1In that day seven women

will take hold of one man

and say, “We will eat our own food

and provide our own clothes;

only let us be called by your name.

Take away our disgrace!”

The Branch of the Lord

2In that day the Branch of the Lord will be beautiful and glorious, and the fruit of the land will be the pride and glory of the survivors in Israel. 3Those who are left in Zion, who remain in Jerusalem, will be called holy, all who are recorded among the living in Jerusalem. 4The Lord will wash away the filth of the women of Zion; he will cleanse the bloodstains from Jerusalem by a spirit4:4 Or the Spirit of judgment and a spirit4:4 Or the Spirit of fire. 5Then the Lord will create over all of Mount Zion and over those who assemble there a cloud of smoke by day and a glow of flaming fire by night; over everything the glory4:5 Or over all the glory there will be a canopy. 6It will be a shelter and shade from the heat of the day, and a refuge and hiding place from the storm and rain.