Yesaya 39 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 39:1-8

Nthumwi Zochokera ku Babuloni

1Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira. 2Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.

3Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”

4Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?”

Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”

5Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse: 6Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe. 7Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”

8Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

New International Version – UK

Isaiah 39:1-8

Envoys from Babylon

1At that time Marduk-Baladan son of Baladan king of Babylon sent Hezekiah letters and a gift, because he had heard of his illness and recovery. 2Hezekiah received the envoys gladly and showed them what was in his storehouses – the silver, the gold, the spices, the fine olive oil – his entire armoury and everything found among his treasures. There was nothing in his palace or in all his kingdom that Hezekiah did not show them.

3Then Isaiah the prophet went to King Hezekiah and asked, ‘What did those men say, and where did they come from?’

‘From a distant land,’ Hezekiah replied. ‘They came to me from Babylon.’

4The prophet asked, ‘What did they see in your palace?’

‘They saw everything in my palace,’ Hezekiah said. ‘There is nothing among my treasures that I did not show them.’

5Then Isaiah said to Hezekiah, ‘Hear the word of the Lord Almighty: 6the time will surely come when everything in your palace, and all that your predecessors have stored up until this day, will be carried off to Babylon. Nothing will be left, says the Lord. 7And some of your descendants, your own flesh and blood who will be born to you, will be taken away, and they will become eunuchs in the palace of the king of Babylon.’

8‘The word of the Lord you have spoken is good,’ Hezekiah replied. For he thought, ‘There will be peace and security in my lifetime.’