Yesaya 39 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 39:1-8

Nthumwi Zochokera ku Babuloni

1Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira. 2Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.

3Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?”

Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”

4Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?”

Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”

5Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse: 6Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe. 7Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”

8Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 39:1-8

巴比倫的使者

1那時,巴比倫王——巴拉但的兒子米羅達·巴拉但聽說希西迦患病、後來痊癒,便派人送去書信和禮物。 2希西迦欣然接見使者,讓他們觀看國庫裡的金銀、香料、珍貴膏油、所有兵器和一切寶物。希西迦把宮中及國內的一切都給他們看。

3以賽亞先知來見希西迦王,問他:「這些人說了些什麼?他們從哪裡來?」

希西迦答道:「他們從遙遠的巴比倫來。」

4以賽亞問:「他們在你宮中看見了什麼?」

希西迦答道:「他們看到了我宮中的一切。我把國庫裡的一切都給他們看了。」

5以賽亞希西迦說:「你聽著,萬軍之耶和華說, 6『終有一天,你王宮中的一切和你祖先積攢到現在的一切,必一件不留地被擄到巴比倫。這是耶和華說的。 7你的子孫當中必有人被擄去,在巴比倫王的宮中做太監。』」 8希西迦以賽亞說:「耶和華藉你說的話很好。」因為他想:「我有生之年將平安穩妥。」