Yesaya 38 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 38:1-22

Kudwala kwa Hezekiya

1Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

4Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

7“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

9Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10Ine ndinaganiza kuti

ndidzapita ku dziko la akufa

pamene moyo ukukoma.

11Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,

mʼdziko la anthu amoyo,

sindidzaonanso mtundu wa anthu

kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.

12Nyumba yanga yasasuka

ndipo yachotsedwa.

Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,

ngati munthu wowomba nsalu;

kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.

13Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;

koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,

ndipo mwakhala mukundisiya.

14Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,

ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.

Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.

Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15Koma ine ndinganene chiyani?

Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.

Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,

ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.

16Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.

Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.

Munandichiritsa ndi

kundikhalitsa ndi moyo.

17Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere

kuti ndikhale ndi moyo;

Inu munandisunga

kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko

chifukwa mwakhululukira

machimo anga onse.

18Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,

akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.

Iwo amene akutsikira ku dzenje

sangakukhulupirireni.

19Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,

monga mmene ndikuchitira ine lero lino;

abambo amawuza ana awo za

kukhulupirika kwanu.

20Yehova watipulumutsa.

Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe

masiku onse a moyo wathu

mʼNyumba ya Yehova.

21Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

O Livro

Isaías 38:1-22

Ezequias adoece

(2 Rs 20.1-11; 2 Cr 32.24)

1Ezequias adoeceu gravemente, ficando às portas da morte. O profeta Isaías veio visitá-lo. “Põe todos os teus assuntos em ordem”, disse-lhe Isaías, “e prepara-te para morreres. O Senhor manda dizer-te que não recuperarás a saúde.”

2Ezequias voltou-se para o lado da parede e orou assim ao Senhor: 3“Ó Senhor, lembra-te de como eu tenho sido honesto e sincero contigo e como procurei obedecer a tudo o que tens dito!” E começou a chorar intensamente.

4Então o Senhor mandou outra mensagem a Isaías: 5“Vai dizer a Ezequias: O Senhor, o Deus de David, teu antepassado, ouviu a tua oração, viu as tuas lágrimas e deixar-te-á viver mais 15 anos. 6Livrar-te-ei, a ti e a esta cidade, do rei da Assíria; defenderei esta cidade. 7E esta é a prova daquilo que digo: 8Farei com que o Sol recue 10 graus, segundo o relógio de sol de Acaz.”

E o Sol recuou 10 graus.

9Quando o rei Ezequias se restabeleceu, escreveu este poema sobre a sua experiência:

10“Disse no meu íntimo:

vivi metade da minha vida e tenho de deixar tudo.

Ficarei privado do resto dos meus anos

e terei de passar as portas do mundo dos mortos.

11Nunca mais tornarei a ver o Senhor na terra dos vivos.

Nunca mais verei os meus amigos neste mundo.

12A minha vida acaba e desfaz-se como a tenda dum pastor,

como a obra dum tecelão quando chega ao fim.

De um dia para o outro, a minha vida está a ser consumida.

13Passei toda a noite a gemer;

era como se um leão me estivesse a partir os ossos.

De um dia para o outro, a minha vida está a ser consumida.

14No meu delírio chilreava como um grou ou uma andorinha,

gemia como uma pomba.

Levantava os olhos para cima, pedindo ajuda.

Ó Senhor, gritava eu, estou angustiado! Socorre-me!”

15Mas que tenho eu a dizer?

Porque foi ele próprio quem me mandou esta doença.

Todo o meu sono desapareceu,

por causa da amargura do meu coração.

16Ó Senhor, a tua disciplina é boa, dá vida e saúde.

Cura-me e faz com que eu viva!

17Agora já compreendo tudo!

Foi bom para mim passar por toda esta aflição,

porque me livraste carinhosamente da morte;

perdoaste todos os meus pecados.

18Visto que os mortos não te podem louvar,

não podem ficar cheios de esperança e de alegria.

19Os vivos, só os vivos, podem louvar-te

como eu estou a fazer agora.

A nossa geração dará a conhecer à seguinte a tua fidelidade.

20O Senhor veio salvar-me!

Todos os dias da minha vida, de agora em diante,

cantarei hinos de louvor no templo,

acompanhado de instrumentos musicais.

21Isaías tinha dito aos criados de Ezequias: “Façam uma pomada de figos e ponham-na sobre a chaga e ele sarará.”

22Ezequias, nessa altura, até tinha perguntado: “Que sinal me dará o Senhor como prova de que estarei com condições para ir ao templo?”