Yesaya 36 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 36:1-22

Senakeribu Awopseza Yerusalemu

1Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda. 2Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala. 3Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.

4Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti,

“Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani? 5Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine? 6Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira. 7Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’

8“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo! 9Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo. 10Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”

11Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”

12Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”

13Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya! 14Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni! 15Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’

16“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake, 17mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.

18“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya? 19Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa? 20Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”

21Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”

22Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

La Bible du Semeur

Esaïe 36:1-22

Intermède historique

L’invasion de Sennachérib

Provocation

(2 R 18.13, 17-37 ; 2 Ch 32.9-19)

1La quatorzième année du règne d’Ezéchias36.1 C’est-à-dire en 701 av. J.-C. Sennachérib, fils de Sargon II, régna de 704 à 681 av. J.-C., Sennachérib, roi d’Assyrie, vint attaquer toutes les villes fortifiées de Juda et s’en empara. 2Le roi d’Assyrie envoya de Lakish36.2 Entre Jérusalem et Gaza, à environ 35 kilomètres au sud-ouest de Jérusalem. à Jérusalem vers le roi Ezéchias, son aide de camp, accompagné d’une puissante armée. Il prit position près de l’aqueduc du réservoir supérieur, sur la route du champ du Teinturier36.2 L’aqueduc est sans doute le canal souterrain qu’Ezéchias a fait creuser (2 R 20.20) pour amener l’eau de la source du Guihôn (1 R 1.33) au réservoir de Siloé, au sud-est de la ville. Le champ du Teinturier devait se trouver près d’Eyn-Roguel, au sud de Jérusalem (voir 2 S 17.17 ; 1 R 1.9 ; Es 7.3)..

3Alors Eliaqim, fils de Hilqiya, qui avait la charge du palais royal, Shebna le secrétaire du roi et Yoah, fils d’Asaph l’archiviste, sortirent de la ville à sa rencontre. 4L’aide de camp du roi d’Assyrie leur dit : Veuillez transmettre ce message à Ezéchias : « Voici ce que déclare le grand roi, le roi d’Assyrie : En quoi mets-tu ta confiance ? 5T’imaginerais-tu36.5 D’après plusieurs manuscrits hébreux, le texte hébreu de Qumrân et 2 R 18.20. La plupart des manuscrits du texte hébreu traditionnel ont : je dis. que de simples paroles peuvent tenir lieu de stratégie et de puissance militaire ? Sur qui comptes-tu donc pour t’être révolté contre moi ? 6Tu t’appuies sur l’Egypte, ce roseau cassé qui blesse et qui transperce la main de celui qui s’appuie dessus. Oui, c’est bien là ce qu’est le pharaon, le roi d’Egypte, pour tous ceux qui se confient en lui ! 7Peut-être me diras-tu : “C’est en l’Eternel, notre Dieu, que nous nous confions.” Mais n’est-ce pas précisément ce Dieu dont Ezéchias a fait disparaître les hauts lieux et les autels, en disant aux habitants de Juda et de Jérusalem de rendre leur culte uniquement devant cet autel-ci ? 8Je te lance aujourd’hui un défi au nom de mon souverain, le roi d’Assyrie : Je te donnerai deux mille chevaux, si toi tu es capable de fournir autant d’hommes pour les monter. 9Comment t’y prendrais-tu pour repousser un seul de nos capitaines, même si c’était le moindre des serviteurs de mon maître ? Comptes-tu sur l’Egypte pour te fournir des chars avec leur équipage ? 10D’ailleurs crois-tu que c’est sans l’assentiment de l’Eternel que je suis venu attaquer ce pays pour le détruire ? C’est l’Eternel qui m’a dit : “Va dans ce pays et détruis-le36.10 Voir Es 7.20 ; 10.5-6. !” »

11Alors Eliaqim, Shebna et Yoah dirent à l’aide de camp assyrien : Voudrais-tu, s’il te plaît, parler à tes serviteurs en langue araméenne36.11 Langue diplomatique de l’époque que parlaient les hauts fonctionnaires. Elle deviendra la langue commune des Juifs à partir du ve siècle av. J.-C., car nous la comprenons. Ne nous parle pas en hébreu, alors que les gens sont là, sur les remparts, à écouter !

12Mais l’aide de camp répliqua : Crois-tu que c’est à ton souverain et à toi seulement que mon souverain m’a chargé d’adresser ce message ? Crois-tu que ce n’est pas aussi à ces gens assis sur les remparts, qui seront bientôt réduits avec vous à manger leurs excréments et à boire leur urine ?

13Puis l’aide de camp se campa là et se mit à crier d’une voix forte, en hébreu : Ecoutez ce que dit le grand roi, le roi d’Assyrie : 14« Ainsi parle le roi : Ne vous laissez pas tromper par Ezéchias. Car il ne peut pas vous délivrer. 15Ne vous laissez pas persuader par Ezéchias de vous confier en l’Eternel, s’il vous dit : “Sûrement, l’Eternel nous délivrera, cette ville ne tombera pas aux mains du roi d’Assyrie.” 16N’écoutez pas Ezéchias ; car voici ce que vous propose le roi d’Assyrie : Faites la paix avec moi, rendez-vous à moi ! Alors chacun de vous mangera les fruits de sa vigne et de son figuier36.16 Expression commune caractérisant la vie paisible et prospère (1 R 5.5 ; Os 2.14 ; Mi 4.4 ; Za 3.10)., et chacun boira de l’eau de son puits, 17en attendant que je vienne vous emmener dans un pays pareil au vôtre, un pays où il y a du blé et du vin, du pain et des vignes. 18Ne laissez pas Ezéchias vous tromper en disant : “L’Eternel nous délivrera.” Les dieux des autres peuples ont-ils délivré leur pays du roi d’Assyrie ? 19Où sont les dieux de Hamath et d’Arpad ? Où sont les dieux de Sepharvaïm36.19 Villes de Syrie. ? Ont-ils délivré Samarie ?

20De tous les dieux de ces pays, quels sont ceux qui ont délivré leur pays, pour que l’Eternel délivre Jérusalem ? »

21Ils gardèrent le silence, et ne lui répondirent pas un mot, car le roi avait donné cet ordre : « Vous ne lui répondrez pas. » 22Alors Eliaqim, fils de Hilqiya, qui avait la charge du palais, Shebna le secrétaire, et Yoah, fils d’Asaph l’archiviste, retournèrent auprès d’Ezéchias, les vêtements déchirés, et lui rapportèrent les paroles de l’aide de camp.