Yesaya 35 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 35:1-10

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

1Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;

dziko lowuma lidzakondwa

ndi kuchita maluwa. 2Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka

lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.

Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,

maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,

ukulu wa Mulungu wathu.

3Limbitsani manja ofowoka,

limbitsani mawondo agwedegwede;

4nenani kwa a mitima yamantha kuti;

“Limbani mtima, musachite mantha;

Mulungu wanu akubwera,

akubwera kudzalipsira;

ndi kudzabwezera chilango adani anu;

akubwera kudzakupulumutsani.”

5Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso

ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.

6Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,

ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.

Akasupe adzatumphuka mʼchipululu

ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,

7mchenga wotentha udzasanduka dziwe,

nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.

Pamene panali mbuto ya ankhandwe

padzamera udzu ndi bango.

8Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;

ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.

Anthu odetsedwa

sadzayendamo mʼmenemo;

zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.

9Kumeneko sikudzakhala mkango,

ngakhale nyama yolusa sidzafikako;

sidzapezeka konse kumeneko.

Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.

10Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.

Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;

kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.

Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,

ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 35:1-10

聖潔之路

1沙漠和乾旱之地必歡喜;

曠野必快樂,開滿鮮花,

2姹紫嫣紅,

喜樂漫溢,發出歡呼,

散發著黎巴嫩的榮耀、

迦密沙崙的榮美。

人們必看見耶和華的榮耀,

我們上帝的光輝。

3你們要使軟弱的人強壯,

使雙腿無力的人站穩。

4要對膽怯的人說:

「你們要剛強,不要懼怕。

看啊,你們的上帝必來拯救你們,為你們復仇,

施行報應。」

5那時,瞎子的眼必看見,

聾子的耳必聽見,

6瘸子必跳躍如鹿,

啞巴必歡呼歌唱;

曠野上泉水湧流,

沙漠裡河川奔騰;

7炙熱的沙漠變成池塘,

旱地湧出甘泉;

豺狼的巢穴長出青草、

蘆葦和蒲草。

8那裡必有一條大路,

被稱為「聖潔之路」,

專供蒙救贖的人行走。

污穢的人都不能走這條路,

愚昧的人也不能踏在上面。

9那裡必沒有獅子,

也沒有惡獸,

沒有牠們的蹤影,

只有蒙救贖的人行走。

10耶和華救贖的子民必歡唱著回到錫安

洋溢著永遠的快樂。

他們必歡喜快樂,

憂愁和歎息都消失無蹤。