Yesaya 35 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 35:1-10

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

1Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;

dziko lowuma lidzakondwa

ndi kuchita maluwa. 2Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka

lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.

Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,

maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,

ukulu wa Mulungu wathu.

3Limbitsani manja ofowoka,

limbitsani mawondo agwedegwede;

4nenani kwa a mitima yamantha kuti;

“Limbani mtima, musachite mantha;

Mulungu wanu akubwera,

akubwera kudzalipsira;

ndi kudzabwezera chilango adani anu;

akubwera kudzakupulumutsani.”

5Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso

ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.

6Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,

ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.

Akasupe adzatumphuka mʼchipululu

ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,

7mchenga wotentha udzasanduka dziwe,

nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.

Pamene panali mbuto ya ankhandwe

padzamera udzu ndi bango.

8Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;

ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.

Anthu odetsedwa

sadzayendamo mʼmenemo;

zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.

9Kumeneko sikudzakhala mkango,

ngakhale nyama yolusa sidzafikako;

sidzapezeka konse kumeneko.

Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.

10Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.

Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;

kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.

Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,

ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 35:1-10

圣洁之路

1沙漠和干旱之地必欢喜;

旷野必快乐,开满鲜花,

2姹紫嫣红,

喜乐漫溢,发出欢呼,

散发着黎巴嫩的荣耀、

迦密沙仑的荣美。

人们必看见耶和华的荣耀,

我们上帝的光辉。

3你们要使软弱的人强壮,

使双腿无力的人站稳。

4要对胆怯的人说:

“你们要刚强,不要惧怕。

看啊,你们的上帝必来拯救你们,为你们复仇,

施行报应。”

5那时,瞎子的眼必看见,

聋子的耳必听见,

6瘸子必跳跃如鹿,

哑巴必欢呼歌唱;

旷野上泉水涌流,

沙漠里河川奔腾;

7炙热的沙漠变成池塘,

旱地涌出甘泉;

豺狼的巢穴长出青草、

芦苇和蒲草。

8那里必有一条大路,

被称为“圣洁之路”,

专供蒙救赎的人行走。

污秽的人都不能走这条路,

愚昧的人也不能踏在上面。

9那里必没有狮子,

也没有恶兽,

没有它们的踪影,

只有蒙救赎的人行走。

10耶和华救赎的子民必欢唱着回到锡安

洋溢着永远的快乐。

他们必欢喜快乐,

忧愁和叹息都消失无踪。