Yesaya 33 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 33:1-24

Msautso ndi Thandizo

1Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,

amene sunawonongedwepo!

Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri,

iwe amene sunanyengedwepo!

Iwe ukadzaleka kuwononga,

udzawonongedwa,

ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga,

ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.

2Inu Yehova, mutikomere mtima ife;

tikulakalaka Inu.

Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu,

ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.

3Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;

pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.

4Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.

Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.

5Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse

adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.

6Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,

adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka;

kuopa Yehova ngati madalitso.

7Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;

akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.

8Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,

mʼmisewu mulibe anthu a paulendo.

Mdaniyo ndi wosasunga pangano.

Iye amanyoza mboni.

Palibe kulemekezana.

9Dziko likulira ndipo likunka likutha.

Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota.

Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala.

Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.

10Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka

ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga,

ndipo ndidzakwezedwa.

11Zolingalira zanu nʼzachabechabe

ngati udzu wamanyowa.

Mpweya wamoto udzakupserezani.

12Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;

ndi ngati minga yodulidwa.”

13Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;

inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga

14Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;

anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera:

Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa?

Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”

15Angathe kuti ndi amene amachita zolungama

ndi kuyankhula zoona,

amene amakana phindu lolipeza monyenga

ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,

amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo

ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.

16Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,

kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.

Azidzalandira chakudya chake

ndipo madzi sadzamusowa.

17Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola

ndi kuona dziko lotambasukira kutali.

18Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:

“Ali kuti mkulu wa Asilikali uja?

Ali kuti wokhometsa misonkho uja?

Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”

19Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,

anthu aja achiyankhulo chosadziwika,

chachilendo ndi chosamveka.

20Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;

maso anu adzaona Yerusalemu,

mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa,

zikhomo zake sizidzazulidwa,

kapena zingwe zake kuduka.

21Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake

ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu.

Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo,

sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.

22Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,

Yehova ndiye wotilamulira,

Yehova ndiye mfumu yathu;

ndipo ndiye amene adzatipulumutse.

23Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,

sizikutha kulimbitsa mlongoti wake,

matanga ake sakutheka kutambasuka.

Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri

ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.

24Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”

ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.