Yesaya 32 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 32:1-20

Ufumu Wachilungamo

1Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,

ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.

2Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo

ndi malo obisalirapo namondwe,

adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,

ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.

3Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,

ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.

4Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,

ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.

5Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake

ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.

6Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,

amaganiza kuchita zoyipa:

Iye amachita zoyipira Mulungu,

ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;

anjala sawapatsa chakudya

ndipo aludzu sawapatsa madzi.

7Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,

iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.

Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake

ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.

8Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,

Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.

Akazi a ku Yerusalemu

9Khalani maso, inu akazi

amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji

ndipo imvani mawu anga.

Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!

10Pakapita chaka ndi masiku pangʼono

inu akazi amatama mudzanjenjemera;

chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika

ndipo zipatso sizidzaoneka.

11Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;

ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.

Vulani zovala zanu,

ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.

12Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,

ndi mphesa yawonongeka.

13Mʼdziko la anthu anga

mwamera minga ndi mkandankhuku.

Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero

ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.

14Nyumba yaufumu idzasiyidwa,

mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;

malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.

Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.

15Yehova adzatipatsa mzimu wake,

ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,

ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.

16Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama

ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.

17Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;

zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.

18Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,

mʼnyumba zodalirika,

ndi malo osatekeseka a mpumulo.

19Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala

ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,

20inutu mudzakhala odalitsika ndithu.

Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,

ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.

New International Reader’s Version

Isaiah 32:1-20

The King Who Will Do What Is Right

1A king will come who will do what is right.

His officials will govern fairly.

2Each official will be like a place to get out of the wind.

He will be like a place to hide from storms.

He’ll be like streams of water flowing in the desert.

He’ll be like the shadow of a huge rock in a dry and thirsty land.

3Then the eyes of those who see won’t be closed anymore.

The ears of those who hear will listen to the truth.

4People who are afraid will know and understand.

Tongues that stutter will speak clearly.

5Foolish people won’t be considered noble anymore.

Those who are worthless won’t be highly respected.

6Foolish people say foolish things.

Their minds are set on doing evil things.

They don’t do what is right.

They tell lies about the Lord.

They don’t give hungry people any food.

They don’t let thirsty people have any water.

7Those who are worthless use sinful methods.

They make evil plans against poor people.

They destroy them with their lies.

They do it even when those people are right.

8But those who are noble make noble plans.

And by doing noble things they succeed.

The Sinful Women in Jerusalem

9You women who are so contented,

pay attention to me.

You who feel so secure,

listen to what I have to say.

10You feel secure now.

But in a little over a year you will tremble with fear.

The grape harvest will fail.

There won’t be any fruit.

11So tremble, you contented women.

Tremble with fear, you who feel so secure.

Take off your fine clothes.

Wrap yourselves in rags.

12Beat your chests to show how sad you are.

The pleasant fields have been destroyed.

The fruitful vines have dried up.

13My people’s land is overgrown with thorns and bushes.

Mourn for all the houses that were once filled with joy.

Cry over this city that used to be full of wild parties.

14The royal palace will be left empty.

The noisy city will be deserted.

The fort and lookout tower will become

a dry and empty desert forever.

Donkeys will enjoy being there.

Flocks will eat there.

15That will continue until the Holy Spirit

is poured out on us from heaven.

Then the desert will be turned into rich farm lands.

The rich farm lands will seem like a forest.

16In the desert, the Lord will make sure people do what is right.

In the rich farm lands he will make sure they treat one another fairly.

17Doing what is right will bring peace and rest.

When my people do that, they will stay calm

and trust in the Lord forever.

18They will live in a peaceful land.

Their homes will be secure.

They will enjoy peace and quiet.

19Hail might strip the forests bare.

Cities might be completely destroyed.

20But how blessed you people will be!

You will plant your seeds by every stream.

You will let your cattle and donkeys

wander anywhere they want to.