Ufumu Wachilungamo
1Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo,
ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
2Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo
ndi malo obisalirapo namondwe,
adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu,
ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
3Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka,
ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
4Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa,
ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
5Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake
ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
6Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru,
amaganiza kuchita zoyipa:
Iye amachita zoyipira Mulungu,
ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova;
anjala sawapatsa chakudya
ndipo aludzu sawapatsa madzi.
7Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso,
iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa.
Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake
ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
8Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino,
Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Akazi a ku Yerusalemu
9Khalani maso, inu akazi
amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji
ndipo imvani mawu anga.
Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
10Pakapita chaka ndi masiku pangʼono
inu akazi amatama mudzanjenjemera;
chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika
ndipo zipatso sizidzaoneka.
11Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu;
ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu.
Vulani zovala zanu,
ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
12Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde,
ndi mphesa yawonongeka.
13Mʼdziko la anthu anga
mwamera minga ndi mkandankhuku.
Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero
ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
14Nyumba yaufumu idzasiyidwa,
mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu;
malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya.
Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
15Yehova adzatipatsa mzimu wake,
ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde,
ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
16Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama
ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
17Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo;
zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
18Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere,
mʼnyumba zodalirika,
ndi malo osatekeseka a mpumulo.
19Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala
ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
20inutu mudzakhala odalitsika ndithu.
Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse,
ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Den retfærdige Konge
1Der vil komme en retfærdig Konge, og hans ledere vil regere retfærdigt. 2De vil give læ for vinden og ly for regnen og være som en oase i ørkenen og en kølende skygge fra en vældig klippe i et trøstesløst land. 3De, som har øjne at se med, skal få øjnene op for det. De, der har ører at høre med, skal fatte det. 4De tankeløse bliver fornuftige, og de stammende taler klart og tydeligt. 5Til den tid skal tåberne ikke regnes for gode ledere, og de rige bedragere ikke blive æret som magtfulde borgere. 6Tåberne spreder jo løgne om Gud, lægger onde planer og handler imod Guds vilje. De giver ikke de sultende mad at spise eller de tørstende noget at drikke. 7De rige bedrageres ondskab skal afsløres. Deres løgnagtige udnyttelse af forsvarsløse mennesker, som har retten på deres side, vil blive gennemskuet. 8Men de gode ledere vil give gode råd og udføre ædle handlinger.
Den forestående ulykke
9Hør efter, I sorgløse kvinder! Lyt til mig, I husmødre uden problemer! 10Om et års tid får I noget at bekymre jer over, I ubekymrede. For vinhøsten slår fejl, og frugthøsten udebliver. 11I vil komme til at skælve af skræk, I sorgløse og magelige kvinder. Læg jeres fine tøj til side og klæd jer i sæk og aske. 12Slå jer for brystet i fortvivlelse over den skæbne, som vil overgå jeres frugtbare marker og bugnende frugthaver. 13Jeres jord vil gro til med tjørn og tidsel. Jeres sorgløse hjem og glade byer vil blive ødelagt. 14Byens fæstningsanlæg lægges i ruiner, og alle folk må flygte. Vildæsler, får og geder vil græsse ved ruinerne og de forladte vagttårne for evigt.
Håb for fremtiden
15Men når Ånden fra Himlen udgydes over os, bliver ødemarken igen til frugthaver, og frugttræerne skal stå så tæt som i en skov. 16Retfærdighed og ret skal blomstre i landet, 17og fredens frugt vokse frem. Da bliver der ro og tryghed for evigt. 18Mit folk vil bo i fred og tryghed, i ro og sikkerhed. 19Hvis haglene falder, skal de ikke ramme jer, og de, der bor i skoven, skal være lige så trygge som dem i byen.32,19 Oversat ud fra LXX. Den hebraiske tekst er uklar, men kan muligvis oversættes som: „Når haglene falder i skoven, vil byen blive mejet ned.” 20I oplever Guds velsignelse, når I kan plante ved hvert et vandløb og lade kvæg og æsler gå frit omkring og græsse i fred.