Yesaya 31 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 31:1-9

Tsoka kwa Amene Amadalira Igupto

1Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo,

amene amadalira akavalo,

nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo

ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo,

koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli,

kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.

2Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga,

ndipo sasintha chimene wanena.

Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa,

komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.

3Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu;

akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu.

Yehova akangotambasula dzanja lake,

amene amapereka chithandizo adzapunthwa,

amene amalandira chithandizocho adzagwa;

onsewo adzathera limodzi.

4Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi:

“Monga mkango kapena msona wamkango umabangula

ukagwira nyama yake,

ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka

ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo,

momwemonso palibe chingaletse

Yehova Wamphamvuzonse

kubwera kudzatchinjiriza

phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.

5Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake,

Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu;

ndi kumupulumutsa,

iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”

6Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu. 7Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.

8“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu.

Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga.

Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo

adzagwira ntchito yathangata.

9Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha,

ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha

kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.”

Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni,

ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 31:1-9

要倚靠主,而非埃及

1那些到埃及尋求幫助的人有禍了!

他們仰賴戰馬,倚靠眾多的戰車和強壯的騎兵,

卻不仰望以色列的聖者,

不尋求耶和華。

2然而,耶和華有智慧,

會降災,

從不收回自己的話。

祂必懲罰惡人之家及其幫兇。

3埃及人不過是人,並非上帝;

埃及的戰馬是血肉之軀,

並非神靈。

耶和華一伸手,

那些幫兇必踉蹌,

受幫助的必跌倒,

他們必一同滅亡。

4耶和華又對我說:

「猛獅守護獵物,發出咆哮。

即使眾多牧人一起攻擊牠,

牠也不會因他們的呐喊而懼怕,

不會因他們的叫嚷而畏縮。

同樣,萬軍之耶和華必降臨在錫安山上爭戰。

5萬軍之耶和華必保護耶路撒冷

就像飛鳥展翅保護幼雛一樣。

祂必護衛它,拯救它。」

6以色列人啊,你們曾經嚴重地悖逆耶和華,現在歸向祂吧! 7到那日,你們都要拋棄自己用罪惡雙手製造的金銀偶像。

8亞述人必喪身刀下,

但並非死於人的刀下。

他們必逃避這刀,

他們的青年必受奴役。

9他們的堡壘必因恐懼而倒塌,

他們的將領一看見戰旗必驚慌失措。」

這是耶和華說的,

祂的火在錫安,祂的火爐在 耶路撒冷