Yesaya 30 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 30:1-33

Tsoka kwa Mtundu Wopanduka

1Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira

amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine,

nachita mgwirizano wawowawo

koma osati motsogozedwa ndi Ine.

Choncho amanka nachimwirachimwira.

2Amapita ku Igupto kukapempha thandizo

koma osandifunsa;

amathawira kwa Farao kuti awateteze,

ku Igupto amafuna malo opulumulira.

3Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu,

malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.

4Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani,

ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,

5aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi

chifukwa cha anthu opanda nawo phindu,

amene sabweretsa thandizo kapena phindu,

koma manyazi ndi mnyozo.”

6Uthenga wonena za nyama za ku Negevi:

Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa,

mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi,

mphiri ndi njoka zaululu.

Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo,

kupita nazo kwa mtundu wa anthu

umene sungawathandize.

7Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe.

Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha

Rahabe chirombo cholobodoka.

8Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita,

ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona

ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha

masiku a mʼtsogolo.

9Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi

osafuna kumvera malangizo a Yehova.

10Iwo amawuza alosi kuti,

‘Musationerenso masomphenya!’

Ndipo amanena kwa mneneri kuti,

‘Musatinenerenso zoona,’

mutiwuze zotikomera,

munenere za mʼmutu mwanu.

11Patukani pa njira ya Yehova,

lekani kutsata njira ya Yehova;

ndipo tisamvenso mawu

a Woyerayo uja wa Israeli!”

12Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti,

“Popeza inu mwakana uthenga uwu,

mumakhulupirira zopondereza anzanu

ndipo mumadalira kuchita zoyipa,

13choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu

pa khoma lalitali ndi lopendama

limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.

14Lidzaphwanyika ngati mbiya

imene yanyenyekeratu,

mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale

lopalira moto mʼngʼanjo

kapena lotungira madzi mʼchitsime.”

15Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi:

“Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka,

ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu,

koma inu munakana zimenezi.

16Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa,

tidzakwera pa akavalo aliwiro.’

Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro,

koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.

17Anthu 1,000 mwa inu adzathawa

poona mdani mmodzi;

poona adani asanu okha

nonsenu mudzathawa.

Otsala anu

adzakhala ngati mbendera pa phiri,

ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”

18Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima,

iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo.

Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo.

Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!

19Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani. 20Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo. 21Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.” 22Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”

23Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka. 24Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo. 25Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono. 26Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.

27Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali,

ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka.

Iye wayankhula mwaukali kwambiri,

ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.

28Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira,

wa madzi ofika mʼkhosi.

Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza;

Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo,

kuti ziwasocheretse.

29Ndipo inu mudzayimba

mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika.

Mudzasangalala

ngati anthu oyimba zitoliro

popita ku phiri la Yehova,

thanthwe la Israeli.

30Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova

ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo

ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa,

mphenzi, namondwe ndi matalala.

31Asiriya adzaopa liwu la Yehova,

ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.

32Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo,

anthu ake adzakhala akuvina nyimbo

zoyimbira matambolini ndi azeze,

Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.

33Malo otenthera zinthu akonzedwa kale;

anakonzera mfumu ya ku Asiriya.

Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu,

ndipo muli nkhuni zambiri;

mpweya wa Yehova,

wangati mtsinje wa sulufule,

udzayatsa motowo pa nkhunizo.

Hoffnung für Alle

Jesaja 30:1-33

Ägyptens Versprechungen sind wertlos

1So spricht der Herr: »Wehe euch, ihr widerspenstigen Kinder! Lasst euch warnen! Ihr führt eure eigenen Pläne aus, die nicht von mir stammen. Ihr schließt Verträge ab, die nicht meinem Willen entsprechen. So ladet ihr immer mehr Schuld auf euch. 2Ohne mich zu fragen, sucht ihr in Ägypten Zuflucht und wollt euch den Schutz des Pharaos sichern. 3Doch euer Vertrauen in den Pharao wird enttäuscht werden: Am Ende werdet ihr ohne den erhofften Schutz von Ägypten dastehen, gedemütigt und beschämt. 4Zwar haben eure führenden Männer die Stadt Zoan erreicht; die Boten, die ihr gesandt habt, sind bis nach Hanes im Süden gekommen. 5Trotzdem wird euch ein Bündnis mit diesem Volk nichts nützen! Es bringt euch keine Hilfe und keinerlei Vorteile, sondern nur Schimpf und Schande.«

6Dies ist Gottes Botschaft über die Tiere, die auf dem Weg durch das Südland sind:

»Eine Karawane zieht durch die grauenvolle Wüste, in der überall Gefahren lauern. Da gibt es Löwen, giftige Vipern und fliegende Schlangen. Die Abgesandten aus Juda haben ihre Esel und Kamele mit reichen Schätzen schwer beladen, denn sie wollten sich die Freundschaft eines Volkes erkaufen. Aber dieses Volk wird ihnen nichts nützen: 7Ägyptens Versprechungen sind wertlos, seine Hilfe kommt vergeblich. Daher nenne ich es ›Rahab, der lahme Drache‹.«

8Der Herr befahl mir: »Geh nun und schreib meine Worte vor den Augen dieser Leute auf eine Tafel! Ritz die Buchstaben tief ein, damit sie nicht verwittern, sondern für alle Zeiten erhalten bleiben. 9Denn mein Volk ist ein widerspenstiges Volk. Wie missratene, verlogene Kinder sind sie, die sämtliche Weisungen von mir in den Wind schlagen. 10Sie verbieten den Propheten zu weissagen. ›Wir wollen die Wahrheit gar nicht hören‹, wehren sie ab. ›Prophezeit uns lieber, was uns gefällt. Lasst uns in schönen Trugbildern leben, täuscht uns ruhig. 11Biegt doch die Wahrheit ein wenig zurecht! Nur lasst uns endlich in Ruhe, verschont uns mit diesem heiligen Gott Israels.‹

12Doch ich, der heilige Gott Israels, antworte ihnen: Ihr haltet es nicht für nötig, auf meine Warnungen und Befehle zu hören. Lieber verlasst ihr euch auf Gewalt und Intrigen. 13Doch das wird euch zum Verhängnis werden. Dann gleicht ihr einer hohen Mauer, die einen Riss bekommen hat. Er wird immer größer und tiefer, bis die Mauer plötzlich zusammenbricht. 14Ihr werdet wie ein Tonkrug sein, der schonungslos in tausend Stücke zerschmettert wird. Keine der Scherben ist noch groß genug, um damit Glut aus der Feuerstelle zu holen oder Wasser aus dem Teich zu schöpfen.«

Vertraut mir, habt Geduld!

15So spricht der Herr, der heilige Gott Israels: »Kehrt doch um zu mir und werdet ruhig, dann werdet ihr gerettet! Vertraut mir und habt Geduld, dann seid ihr stark! Doch das wollt ihr nicht.

16Stattdessen prahlt ihr: ›Wir haben gute Pferde, auf ihnen jagen wir so schnell wie der Wind davon.‹ Jawohl, ihr werdet davonjagen – auf der Flucht vor euren Feinden! Selbst wenn ihr noch so schnell rennt – eure Verfolger bleiben euch auf den Fersen! 17Ein Einziger von ihnen schlägt tausend von euch in die Flucht; und wenn nur fünf euch angreifen, dann lauft ihr alle schon davon. Zuletzt bleibt nur ein kleines Häufchen von euch übrig, einsam und verlassen wie eine Fahnenstange auf der Bergspitze.«

18Doch sehnt sich der Herr danach, euch gnädig zu sein. Bald wird er zu euch kommen und sich wieder über euch erbarmen, denn er ist ein gerechter Gott. Wie glücklich können sich alle schätzen, die auf seine Hilfe warten!

19Ihr Einwohner von Jerusalem, ihr Menschen aus Zion, ihr müsst nicht mehr weinen! Der Herr wird euch wieder in Liebe annehmen, darauf könnt ihr euch verlassen. Sobald er euer Schreien hört, kommt er euch zu Hilfe. 20Und lässt er auch schlimme Zeiten anbrechen, in denen Sorge und Leid euer tägliches Brot sind,30,20 Oder: in denen Brot und Wasser knapp werden. so werdet ihr doch nicht umkommen. Der Herr wird sich nicht länger vor euch verborgen halten, sondern er wird euch unterweisen. Mit eigenen Augen werdet ihr ihn als euren Lehrer erkennen. 21Und kommt ihr vom richtigen Weg ab, so hört ihr hinter euch eine Stimme: »Halt, dies ist der Weg, den ihr einschlagen sollt!« 22Dann sind eure geschnitzten und gegossenen, mit Gold und Silber überzogenen Götzenfiguren für euch auf einmal nur noch Abfall. Verächtlich ruft ihr: »Bloß weg mit diesem Dreck!«

23Eure bestellten Felder wird der Herr mit Regen tränken. Üppig steht euer Korn da, ihr bringt eine reiche Ernte ein. Eure Herden weiden auf weiten, saftigen Wiesen. 24Die Rinder und Esel, mit denen ihr die Felder bearbeitet, bekommen Kraftfutter aus Getreide zu fressen, das man sorgfältig von der Spreu getrennt hat. 25An dem Tag, an dem Gott mit den Feinden abrechnet und ihre Festungen einreißt, da werden Bäche voller Wasser von allen Bergen und Hügeln herabfließen. 26Der Mond leuchtet so hell wie die Sonne, und die Sonne scheint siebenmal heller als sonst, als würde sie das Licht einer ganzen Woche verbreiten. An diesem Tag wird der Herr die Wunden, die er seinem Volk zugefügt hat, verbinden und ihre Brüche heilen.

Der Herr rechnet mit den Assyrern ab

27Seht ihr den Herrn nahen? Er selbst kommt von weit her, gepackt von glühendem Zorn. Mit Gewalt erhebt er sich. Seine Lippen beben vor Wut, und seine Zunge sprüht Feuer. 28Sein Atem reißt alles mit sich fort wie ein tosender Bach, der einem bis zum Hals reicht. Er kommt, um die Völker im Sieb zu schütteln und die wertlosen Stoppeln wegzuwerfen. Wie wilde Pferde wird er sie bändigen, er wird ihnen Zaumzeug anlegen und sie daran ins Verderben führen.

29Ihr aber werdet Lieder singen wie in den Nächten, in denen ihr heilige Feste feiert. Ihr werdet fröhlich sein wie die Pilger, die unter Flötenspiel zum Berg des Herrn ziehen, zum schützenden Fels des Volkes Israel.

30Der Herr lässt seine Donnerstimme hören; in schrecklichem Zorn schlägt er zu, mit loderndem Feuer, Wolkenbruch, Sturm und Hagel. 31Die Assyrer werden zu Tode erschrecken, wenn sie die Donnerstimme des Herrn hören und seine Stockschläge spüren. 32Sie bekommen die vom Herrn verhängte Strafe; ein Rutenhieb nach dem anderen klatscht auf sie nieder, begleitet von Trommelwirbel und Klängen der Laute. Ja, Gott selbst wird gegen sie kämpfen! 33Der Platz ihrer Hinrichtung ist längst vorbereitet. Auch auf den König wartet der Scheiterhaufen. Die Feuerstelle wurde ausgehoben, tief und weit; eine große Menge Brennholz hat man aufgeschichtet. Der Atem des Herrn, feurig wie ein glühender Lavastrom, setzt alles in Brand.