Yesaya 29 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 29:1-24

Tsoka kwa Mzinda wa Davide

1Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,

mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!

Papite chaka chimodzi kapena ziwiri

ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.

2Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli

ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,

mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.

3Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;

ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo

ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.

4Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,

mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,

adzamveka ngati a mzukwa.

Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.

5Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.

Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.

Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,

6Yehova Wamphamvuzonse adzabwera

ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,

kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.

7Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli

nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,

chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,

gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.

8Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,

koma podzuka ali nayobe njala;

kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,

koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.

Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse

chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.

9Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.

Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,

ledzerani, koma osati ndi vinyo,

dzandirani, koma osati ndi mowa.

10Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.

Watseka maso anu, inu aneneri;

waphimba mitu yanu, inu alosi.

11Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”

13Ambuye akuti,

“Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo,

ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso.

Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.

14Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira

kuwachitira ntchito zodabwitsa;

nzeru za anthu anzeru zidzatha,

luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”

15Tsoka kwa amene amayesetsa

kubisira Yehova maganizo awo,

amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti,

“Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”

16Inu mumazondotsa zinthu

ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya.

Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti

“Sunandipange ndi iwe?”

Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti,

“Iwe sudziwa chilichonse?”

17Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde,

ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?

18Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku,

ndipo anthu osaona amene

ankakhala mu mdima adzapenya.

19Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova;

ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.

20Koma anthu ankhanza adzazimirira,

oseka anzawo sadzaonekanso,

ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.

21Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa,

kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu

ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.

22Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti,

“Anthu anga sadzachitanso manyazi;

nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.

23Akadzaona ana awo ndi

ntchito ya manja anga pakati pawo,

adzatamanda dzina langa loyera;

adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo,

ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.

24Anthu opusa adzapeza nzeru;

onyinyirika adzalandira malangizo.”

New International Reader’s Version

Isaiah 29:1-24

The Lord Will Judge Jerusalem

1Jerusalem, how terrible it will be for you!

Ariel, you are the city where David made his home.

The years will come and go.

Keep on celebrating your regular feasts.

2The Lord says, “Ariel, I will surround you.

Jerusalem, I will get ready to attack you.

Your people will mourn.

They will sing songs of sadness.

I will make you like the front of an altar

covered with blood.

3I will be like an army camped against you on all sides.

I will surround you with towers in order to attack you.

I will build my ramps all around you and set up my ladders.

4You will be brought down to the grave.

You will speak from deep down inside the ground.

Your words will be barely heard out of the dust.

Your voice will sound like the voice of a ghost

coming from under the ground.

Your words will sound like a whisper out of the dust.”

5Jerusalem, all your enemies will become like fine dust.

Their terrifying armies will become like straw

that the wind blows away.

All of a sudden, in an instant,

6the Lord who rules over all will come.

He will come with thunder, earthquakes and a lot of noise.

He’ll bring windstorms and rainstorms with him.

He’ll send a blazing fire that will burn up everything.

7Armies from all the nations will fight against Ariel.

They will attack it and its fort.

They’ll surround it completely.

But suddenly those armies will disappear like a dream.

They will vanish like a vision in the night.

8It will be as when a hungry person dreams of eating,

but wakes up still hungry.

It will be as when a thirsty person dreams of drinking,

but wakes up weak and still thirsty.

In the same way, the armies from all the nations

that fight against Mount Zion will disappear.

9People of Jerusalem, be shocked and amazed.

Make yourselves blind so you can’t see anything.

Get drunk, but not from wine.

Be unsteady on your feet, but not because of beer.

10The Lord has made you fall into a deep sleep.

He has closed the eyes of your prophets.

He has covered the heads of your seers so they can’t see.

11For you, this whole vision is like words that are sealed up in a scroll. Suppose you give it to someone who can read. And suppose you say, “Please read this for us.” Then they’ll answer, “I can’t. It’s sealed up.” 12Or suppose you give the scroll to someone who can’t read. And suppose you say, “Please read this for us.” Then they’ll answer, “I don’t know how to read.”

13The Lord says,

“These people worship me only with their words.

They honor me by what they say.

But their hearts are far away from me.

Their worship doesn’t mean anything to me.

They teach nothing but human rules that they have been taught.

14So once more I will shock these people

with many wonderful acts.

I will destroy the wisdom of those who think they are so wise.

I will do away with the cleverness of those who think they are so smart.”

15How terrible it will be for people who try hard

to hide their plans from the Lord!

They do their work in darkness.

They think, “Who sees us? Who will know?”

16They turn everything upside down.

How silly they are to think that potters are like the clay they work with!

Can what is made say to the one who made it,

“You didn’t make me”?

Can the pot say to the potter,

“You don’t know anything”?

17In a very short time, Lebanon will be turned into rich farm lands.

The rich farm lands will seem like a forest.

18At that time those who can’t hear will hear what is read from the scroll.

Those who are blind will come out of gloom and darkness.

They will be able to see.

19Those who aren’t proud will once again find their joy in the Lord.

And those who are in need will find their joy in the Holy One of Israel.

20Those who don’t show any pity will vanish.

Those who make fun of others will disappear.

All those who look for ways to do what is evil will be cut off.

21Without any proof, they claim that a person is guilty.

In court they try to trap

the one who speaks up for others.

By using dishonest witnesses they keep people who aren’t guilty

from being treated fairly.

22Long ago the Lord saved Abraham from trouble. Now he says to Jacob’s people,

“You will not be ashamed anymore.

Your faces will no longer grow pale with fear.

23You will see your children living among you.

I myself will give you those children.

Then you will honor my name.

You will recognize how holy I am.

I am the Holy One of Jacob.

You will have great respect for me.

I am the God of Israel.

24I will give understanding to you

who find yourselves going astray.

You who are always speaking against others

will accept what I teach you.”