Yesaya 29 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 29:1-24

Tsoka kwa Mzinda wa Davide

1Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,

mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!

Papite chaka chimodzi kapena ziwiri

ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.

2Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli

ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,

mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.

3Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;

ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo

ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.

4Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,

mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,

adzamveka ngati a mzukwa.

Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.

5Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.

Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.

Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,

6Yehova Wamphamvuzonse adzabwera

ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,

kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.

7Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli

nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,

chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,

gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.

8Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,

koma podzuka ali nayobe njala;

kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,

koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.

Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse

chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.

9Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.

Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,

ledzerani, koma osati ndi vinyo,

dzandirani, koma osati ndi mowa.

10Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.

Watseka maso anu, inu aneneri;

waphimba mitu yanu, inu alosi.

11Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”

13Ambuye akuti,

“Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo,

ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso.

Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.

14Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira

kuwachitira ntchito zodabwitsa;

nzeru za anthu anzeru zidzatha,

luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”

15Tsoka kwa amene amayesetsa

kubisira Yehova maganizo awo,

amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti,

“Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”

16Inu mumazondotsa zinthu

ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya.

Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti

“Sunandipange ndi iwe?”

Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti,

“Iwe sudziwa chilichonse?”

17Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde,

ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?

18Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku,

ndipo anthu osaona amene

ankakhala mu mdima adzapenya.

19Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova;

ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.

20Koma anthu ankhanza adzazimirira,

oseka anzawo sadzaonekanso,

ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.

21Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa,

kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu

ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.

22Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti,

“Anthu anga sadzachitanso manyazi;

nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.

23Akadzaona ana awo ndi

ntchito ya manja anga pakati pawo,

adzatamanda dzina langa loyera;

adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo,

ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.

24Anthu opusa adzapeza nzeru;

onyinyirika adzalandira malangizo.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 29:1-24

耶路撒冷被围

1耶和华说:“亚利伊勒29:1 亚利伊勒”在此处用来指锡安/耶路撒冷,2节、7节同。亚利伊勒

大卫安营的城啊!

你有祸了!

尽管你年复一年地守节期,

2我还是要叫你受苦。

你必悲伤哀号,

在我面前成为一座祭坛。

3我必把你团团围住,

屯兵围困你,

修筑高台攻打你。

4你必一败涂地,

躺在尘土中说话,

你细微的声音从土中传来,

好像地下幽灵的声音。

你耳语般的低声从土中传来。

5但你的众仇敌必像纤细的尘埃一样消散,

众多的残暴之徒必如被风刮去的糠秕。

突然,刹那之间,

6万军之耶和华必带着雷轰、地震、巨响、旋风、暴风和烈火来临。

7攻打、围困耶路撒冷及其堡垒的各国军队必如梦幻,

如夜间的异象一样消失。

8他们好像饥饿的人梦中吃饭,

醒来仍然饥饿;

像口渴的人梦中喝水,

醒来仍然渴得发昏。

攻打锡安山的各国军队结局都必如此。”

9你们驻足惊奇吧!

你们自我蒙蔽,继续瞎眼吧!

你们醉了,但不是因为酒;

你们东倒西歪,但不是因为烈酒。

10因为耶和华把沉睡的灵倾倒在你们身上,

祂封住你们的眼睛,

盖住你们的头。

你们的眼睛就是先知,

你们的头就是先见。

11对你们而言,所有的启示都好像封了印的书卷。你们把书卷交给识字的人读,他会说:“我不能读,这书卷是封着的。” 12你们把书卷交给不识字的人读,他会说:“我不识字。”

13主说:“这些人嘴上亲近我,

尊崇我,心却远离我。

他们敬拜我不过是遵行人定的规条。

14所以,我要再次行奇妙无比的事,使他们震惊。

他们智者的智慧必泯灭,

明哲的聪明必消失。”

15那些向耶和华深藏计谋的人有祸了!

他们暗中行事,

自以为无人看见也无人知道。

16他们太愚蠢了!

窑匠怎能跟泥土相提并论?

被造的怎能对造它的说:

“你没有造我”?

陶器怎能对陶匠说:

“你什么也不懂”?

17再过不久,黎巴嫩将变成沃野,

沃野上庄稼茂密如林。

18那时,聋子必听见那书卷上的话,

黑暗中的瞎子必能看见。

19卑微的人必因耶和华而欢喜,

贫穷的人必因以色列的圣者而快乐。

20残暴之徒必消失,

嘲讽者必绝迹,

所有心怀不轨者必被铲除。

21他们诬陷人,

暗算审判官,

冤枉无辜。

22因此,关于雅各家,

救赎亚伯拉罕的耶和华说:

雅各的子孙必不再羞愧,

脸上再无惧色。

23因为他们看见我赐给他们的子孙时,

必尊我的名为圣,

必尊雅各的圣者为圣,

必敬畏以色列的上帝。

24心里迷惘的必明白真理,

发怨言的必欣然受教。”