Yesaya 28 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 28:1-29

Tsoka kwa Efereimu

1Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu.

Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa

limene lili pa mutu pa anthu

oledzera a mʼchigwa chachonde.

2Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga.

Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga,

ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho;

ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.

3Ulamuliro wa atsogoleri oledzera

a ku Efereimu adzawuthetsa.

4Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa

lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja,

udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa

imene munthu akangoyiona amayithyola

nthawi yokolola isanakwane.

5Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse

adzakhala ngati nkhata yaufumu,

chipewa chokongola

kwa anthu ake otsala.

6Iye adzapereka mtima

wachilungamo kwa oweruza,

adzakhala chilimbikitso kwa

amene amabweza adani pa zipata za mzinda.

7Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo

ndipo akusochera chifukwa cha mowa:

ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa

ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo;

akusochera chifukwa cha mowa,

akudzandira pamene akuona masomphenya,

kupunthwa pamene akupereka chigamulo.

8Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha

ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.

9Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani?

Uthengawu akufuna kufotokozera yani?

Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa,

kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?

10Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono

lemba ndi lemba, mzere ndi mzere,

phunziro ndi phunziro.

Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”

11Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino.

Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene

12anakuwuzani kuti,

“Malo opumulira ndi ano,

otopa apumule, malo owusira ndi ano.”

Koma inu simunamvere.

13Choncho Yehova adzakuphunzitsani

pangʼonopangʼono lemba ndi lemba,

mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro.

Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo,

adzapweteka ndi kukodwa mu msampha

ndipo adzakutengani ku ukapolo.

14Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova,

inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.

15Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa,

ife tachita mgwirizano ndi manda.

Pamene mliri woopsa ukadzafika

sudzatikhudza ife,

chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu

ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.”

16Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi:

“Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri

ngati maziko mu Ziyoni,

mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu;

munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.

17Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake,

ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere;

matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza,

ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.

18Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa;

mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa.

Pakuti mliri woopsa udzafika,

ndipo udzakugonjetsani.

19Ndipo ukadzangofika udzakutengani.

Udzafika mmawa uliwonse,

usiku ndi usana.”

Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu

adzaopsedwa kwambiri.

20Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo;

ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.

21Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu

adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni;

adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo,

ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.

22Tsopano lekani kunyoza,

mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri;

Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti,

“Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”

23Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga;

mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.

24Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha?

Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?

25Pamene iye wasalaza mundawo,

kodi samafesa mawere ndi chitowe?

Kodi suja samadzala tirigu

ndi barele mʼmizere yake,

nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?

26Mulungu wake amamulangiza

ndi kumuphunzitsa njira yabwino.

27Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero,

kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta;

mawere amapuntha ndi ndodo

ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.

28Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi,

komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke.

Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta,

koma akavalo ake satekedza tiriguyo.

29Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,

wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 28:1-29

北国必遭审判

1以法莲酒徒引以为荣的华冠有祸了!

它坐落在醉酒者肥美的山谷顶上,

它的荣美如将残之花。

2看啊,主已经派来一位强壮有力的人,

他像冰雹和毁灭的暴风,

又像汹涌泛滥的洪水,

他必把那华冠猛力摔在地上。

3以法莲酒徒引以为荣的华冠必被践踏。

4那肥美山谷上将残的荣美之花,

必像夏季到来之前早熟的无花果,

人一看见它就把它摘去吞掉。

5到那日,万军之耶和华必做祂余民的荣冠和华冕。

6祂必使审判官公正断案,

赐力量给守城退敌之人。

7但祭司和先知也因喝酒而摇摇晃晃,

因烈酒而东倒西歪。

他们因烈酒而摇摇晃晃、

酩酊大醉、东倒西歪,

他们错解异象,糊涂判案。

8桌子上到处都是呕吐之物,

一片狼藉。

9他们抱怨我说:

“他想教导谁知识呢?

他想把信息解释给谁呢?

是刚刚断奶、离开母怀的婴孩吗?

10因为他的教导只是命命令令、命命令令、律律例例、律律例例、这里一点、那里一点。”

11因此,耶和华必用外族人的口和语言来教训他们。

12耶和华曾对他们说:

“这是安歇之地,

让疲乏的人安歇吧。

这是安歇之地。”

他们却不肯听。

13所以,对他们来说,

耶和华的话成了命命令令、命命令令、律律例例、律律例例、这里一点、那里一点,

以致他们走路时仰面跌倒,摔伤,落网,被捉。

14你们这些好讥讽、在耶路撒冷统管百姓的人啊,

要听耶和华的话。

15你们说:

“我们已经和死亡立约,

与阴间结盟。

灾难席卷而来的时候,

我们会安然无恙,

因为我们以谎言为庇护所,

以诡诈为藏身处。”

16所以主耶和华说:

“看啊,我要在锡安放一块基石,

一块经过考验的石头,

一块根基稳固的宝贵房角石,

信靠的人必不致蒙羞。

17我必以公平为准绳,

以公义作线锤。

冰雹必砸碎你们虚谎的庇护所,

洪水必淹没你们的藏身处。

18你们和死亡所立的约必被废弃,

与阴间的结盟必不能长久。

灾难席卷而来的时候,

你们必遭毁灭。

19灾难必不分昼夜、日复一日地扫过,

每次扫过都必将你们掳去。”

明白这信息的人都必惊恐万分。

20你们的床太小,不能舒身;

你们的被子太窄,不足裹身。28:20 此处的床和被子象征他们虚假的安全感。

21耶和华必像在毗拉心山一样挺身而出,

像在基遍谷一样发怒,

要完成祂奇异的作为,

成就祂不寻常的工作。

22现在你们不要再讥讽了,

以免捆绑你们的绳索勒得更紧,

因为我已从主——万军之耶和华那里听到毁灭全国的谕旨。

23你们要侧耳听我的声音,

留心听我的话语。

24难道农夫会一直耕地而不撒种吗?

难道他会一直犁地、耙地吗?

25他耙平土地之后,

难道不种小茴香、大茴香吗?

不按行种小麦,

在合适的地方种大麦,

在田边种粗麦吗?

26因为上帝指点他,教导他耕种之道。

27打小茴香不用大槌,用棍子;

打大茴香不用石磙,用棒子。

28做饼的粮食要磨碎,

没有人会不停地在场上碾压粮食。

马拉着石磙在场上轧过,

也不会把麦子磨碎。

29这些知识都是万军之耶和华所赐的,

祂有奇妙的谋略和伟大的智慧。