Yesaya 25 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 25:1-12

Nyimbo Yotamanda Yehova

1Yehova ndinu Mulungu wanga;

ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,

pakuti mwachita zodabwitsa

zimene munakonzekeratu kalekale

mokhulupirika kwambiri.

2Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.

Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,

linga la anthu achilendo lero si mzindanso

ndipo sidzamangidwanso.

3Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;

mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.

4Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,

mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.

Mwakhala ngati pobisalirapo

pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.

Pakuti anthu ankhanza

ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,

5ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.

Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.

Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,

inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.

6Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera

anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.

Phwando la nyama yonona

ndi vinyo wabwino kwambiri.

7Iye adzachotsa kulira

kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.

Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.

8Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,

Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso

mwa munthu aliyense;

adzachotsa manyazi a anthu ake

pa dziko lonse lapansi,

Yehova wayankhula.

9Tsiku limenelo iwo adzati,

“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;

ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.

Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;

tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”

10Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;

ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,

ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.

11Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,

ngati mmene amachitira munthu wosambira.

Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo

ngakhale luso la manja awo.

12Iye adzagumula malinga awo ataliatali

ndipo adzawagwetsa

ndi kuwaponya pansi,

pa fumbi penipeni.

Nova Versão Internacional

Isaías 25:1-12

Louvem o Senhor

1Senhor, tu és o meu Deus;

eu te exaltarei e louvarei o teu nome,

pois com grande perfeição

tens feito maravilhas,

coisas há muito planejadas.

2Fizeste da cidade um monte de entulho,

da cidade fortificada uma ruína,

da cidadela dos estrangeiros

uma cidade inexistente

que jamais será reconstruída.

3Por isso um povo forte te honrará;

a cidade das nações cruéis te temerá.

4Tens sido refúgio para os pobres,

refúgio para o necessitado em sua aflição,

abrigo contra a tempestade

e sombra contra o calor

quando o sopro dos cruéis

é como tempestade contra um muro

5e como o calor do deserto.

Tu silencias o bramido dos estrangeiros;

assim como diminui o calor com a sombra de uma nuvem,

assim a canção dos temíveis é emudecida.

6Neste monte o Senhor dos Exércitos

preparará um farto banquete para todos os povos,

um banquete de vinho envelhecido,

com carnes suculentas e o melhor vinho.

7Neste monte ele destruirá o véu

que envolve todos os povos,

a cortina que cobre todas as nações;

8destruirá a morte para sempre.

O Soberano, o Senhor, enxugará as lágrimas de todo rosto

e retirará de toda a terra a zombaria do seu povo.

Foi o Senhor quem o disse!

9Naquele dia, dirão:

“Este é o nosso Deus;

nós confiamos nele, e ele nos salvou.

Este é o Senhor, nós confiamos nele;

exultemos e alegremo-nos, pois ele nos salvou”.

10Pois a mão do Senhor repousará sobre este monte;

mas Moabe será pisoteado em seu próprio lugar,

como a palha é pisoteada na esterqueira.

11Ali Moabe estenderá as mãos

como faz o nadador para nadar,

mas o Senhor abaterá o seu orgulho,

apesar da habilidade das suas mãos.

12Abaterá as torres altas dos seus altos muros e os derrubará;

ele os lançará ao pó da terra.