Nyimbo Yotamanda Yehova
1Yehova ndinu Mulungu wanga;
ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,
pakuti mwachita zodabwitsa
zimene munakonzekeratu kalekale
mokhulupirika kwambiri.
2Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.
Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,
linga la anthu achilendo lero si mzindanso
ndipo sidzamangidwanso.
3Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;
mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.
4Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,
mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.
Mwakhala ngati pobisalirapo
pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.
Pakuti anthu ankhanza
ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,
5ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.
Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.
Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,
inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.
6Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera
anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.
Phwando la nyama yonona
ndi vinyo wabwino kwambiri.
7Iye adzachotsa kulira
kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.
Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.
8Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,
Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso
mwa munthu aliyense;
adzachotsa manyazi a anthu ake
pa dziko lonse lapansi,
Yehova wayankhula.
9Tsiku limenelo iwo adzati,
“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;
ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.
Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;
tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”
10Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;
ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,
ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.
11Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,
ngati mmene amachitira munthu wosambira.
Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo
ngakhale luso la manja awo.
12Iye adzagumula malinga awo ataliatali
ndipo adzawagwetsa
ndi kuwaponya pansi,
pa fumbi penipeni.
Louvem o Senhor
1Senhor, tu és o meu Deus;
eu te exaltarei e louvarei o teu nome,
pois com grande perfeição
tens feito maravilhas,
coisas há muito planejadas.
2Fizeste da cidade um monte de entulho,
da cidade fortificada uma ruína,
da cidadela dos estrangeiros
uma cidade inexistente
que jamais será reconstruída.
3Por isso um povo forte te honrará;
a cidade das nações cruéis te temerá.
4Tens sido refúgio para os pobres,
refúgio para o necessitado em sua aflição,
abrigo contra a tempestade
e sombra contra o calor
quando o sopro dos cruéis
é como tempestade contra um muro
5e como o calor do deserto.
Tu silencias o bramido dos estrangeiros;
assim como diminui o calor com a sombra de uma nuvem,
assim a canção dos temíveis é emudecida.
6Neste monte o Senhor dos Exércitos
preparará um farto banquete para todos os povos,
um banquete de vinho envelhecido,
com carnes suculentas e o melhor vinho.
7Neste monte ele destruirá o véu
que envolve todos os povos,
a cortina que cobre todas as nações;
8destruirá a morte para sempre.
O Soberano, o Senhor, enxugará as lágrimas de todo rosto
e retirará de toda a terra a zombaria do seu povo.
Foi o Senhor quem o disse!
9Naquele dia, dirão:
“Este é o nosso Deus;
nós confiamos nele, e ele nos salvou.
Este é o Senhor, nós confiamos nele;
exultemos e alegremo-nos, pois ele nos salvou”.
10Pois a mão do Senhor repousará sobre este monte;
mas Moabe será pisoteado em seu próprio lugar,
como a palha é pisoteada na esterqueira.
11Ali Moabe estenderá as mãos
como faz o nadador para nadar,
mas o Senhor abaterá o seu orgulho,
apesar da habilidade das suas mãos.
12Abaterá as torres altas dos seus altos muros e os derrubará;
ele os lançará ao pó da terra.