Yesaya 25 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 25:1-12

Nyimbo Yotamanda Yehova

1Yehova ndinu Mulungu wanga;

ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,

pakuti mwachita zodabwitsa

zimene munakonzekeratu kalekale

mokhulupirika kwambiri.

2Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.

Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,

linga la anthu achilendo lero si mzindanso

ndipo sidzamangidwanso.

3Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;

mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.

4Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,

mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.

Mwakhala ngati pobisalirapo

pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.

Pakuti anthu ankhanza

ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,

5ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.

Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.

Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,

inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.

6Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera

anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.

Phwando la nyama yonona

ndi vinyo wabwino kwambiri.

7Iye adzachotsa kulira

kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.

Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.

8Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,

Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso

mwa munthu aliyense;

adzachotsa manyazi a anthu ake

pa dziko lonse lapansi,

Yehova wayankhula.

9Tsiku limenelo iwo adzati,

“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;

ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.

Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;

tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”

10Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;

ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,

ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.

11Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,

ngati mmene amachitira munthu wosambira.

Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo

ngakhale luso la manja awo.

12Iye adzagumula malinga awo ataliatali

ndipo adzawagwetsa

ndi kuwaponya pansi,

pa fumbi penipeni.

Het Boek

Jesaja 25:1-12

God voert zijn plannen uit

1Here, ik zal uw naam eren en prijzen, want U bent mijn God, U doet zulke wonderbaarlijke dingen! U hebt uw plannen lang geleden vastgesteld en nu hebt U ze uitgevoerd, precies zoals U Zich had voorgenomen. 2Een machtige stad hebt U veranderd in een ruïne. Van het sterkste fort hebt U slechts puinhopen laten overblijven. Het paleis van de vreemdeling hebt U doen verdwijnen. Het zal nooit worden herbouwd. 3Daarom zullen sterke naties beven van angst voor U, meedogenloze volken gehoorzamen U en prijzen uw naam.

4Maar voor de armen, o Here, bent U een schuilplaats in de storm, een schaduw tijdens de hitte. Een toevluchtsoord tegen genadeloze volken die lijken op een slagregen die een aarden wal doorweekt en laat instorten. 5Zoals een heet en droog land door de schaduw van wolken wordt verkoeld, zo zult U de trots van meedogenloze volken bekoelen.

6Hier op de berg Sion in Jeruzalem zal de Here van de hemelse legers een indrukwekkend feest houden voor iedereen op aarde, een prachtig feest met heerlijk voedsel, met wijn van een goed jaar en het beste vlees. 7Dan zal Hij de schemer van hopeloosheid en de sluier van de dood die over de volken van de aarde ligt, wegnemen, 8Hij zal de dood voor altijd opslokken. De Here God zal alle tranen afvegen en voor altijd de beledigingen en de spot tegen zijn land en volk wegnemen. De Here heeft gesproken, Hij zal dit zeker doen!

9Op die dag zullen de mensen verklaren: ‘Dit is onze God, op wie wij vertrouwden en op wie wij wachtten. Hij is gekomen om ons te redden, laat ons daarom blij zijn over onze bevrijding!’ 10Want de goede hand van de Here zal op Jeruzalem rusten en Moab zal als stro onder zijn voeten worden vertrapt en worden achtergelaten om te verrotten. 11Gods hand zal hen wegduwen zoals een zwemmer het water met zijn handen wegduwt. Hij zal een einde maken aan hun trots en slechte daden. 12De hoge, steile muren van Moab zullen worden vernield en tot stof worden verpulverd.