Yesaya 24 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 24:1-23

Chilango cha Yehova pa Dziko Lapansi

1Taonani, Yehova adzawononga dziko lapansi

ndi kulisandutsa chipululu;

Iye adzasakaza maonekedwe ake

ndi kumwaza anthu ake onse.

2Aliyense zidzamuchitikira mofanana:

wansembe chimodzimodzi munthu wamba,

antchito aamuna mofanananso ndi ambuye awo aamuna,

antchito aakazi chimodzimodzi ambuye awo aakazi,

wogula chimodzimodzi wogulitsa,

wobwereka chimodzimodzi wobwereketsa,

okongola chimodzimodzi okongoza.

3Dziko lapansi lidzawonongedwa kwathunthu

ndi kusakazikiratu.

Yehova wanena mawu awa.

4Dziko lapansi likulira ndipo likufota,

dziko lonse likuvutika ndipo likuwuma,

anthu omveka a dziko lapansi akuvutika.

5Anthu ayipitsa dziko lapansi;

posamvera malangizo ake;

pophwanya mawu ake

ndi pangano lake lamuyaya.

6Nʼchifukwa chake matemberero akuwononga dziko lapansi;

anthu a mʼdzikomo akuzunzika chifukwa cha kulakwa kwawo,

iwo asakazika

ndipo atsala ochepa okha.

7Vinyo watsopano watha ndipo mphesa zikufota;

onse okonda zosangalatsa ali ndi chisoni.

8Kulira kokometsera kwa matambolini kwatha,

phokoso la anthu osangalala latha,

zeze wosangalatsa wati zii.

9Anthu sadzayimbanso akumwa vinyo;

akadzamwa zaukali zidzakhala zowawa mʼkamwa mwawo.

10Mzinda wachisokonezo uja wawonongeka;

nyumba iliyonse yatsekedwa.

11Anthu akulira mʼmisewu kufuna vinyo;

chimwemwe chonse chatheratu,

palibenso chisangalalo pa dziko lapansi.

12Mzinda wasanduka bwinja

zipata zake zagumuka.

13Zimenezi ndizo zidzachitikire mitundu yonse ya dziko lapansi

ndiponso pakati pa mitundu ya anthu.

Zidzakhala ngati pamene mitengo ya olivi yayoyoledwa,

kapena ngati nthawi ya kunkha la mphesa atatsiriza kukolola.

14Koma otsala onse akufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe;

anthu akumadzulo akutamanda ukulu wa Yehova.

15Nʼchifukwa chake inu akummawa, tamandani Yehova;

ndi inu okhala mʼmphepete mwa nyanja kwezani dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli.

16Kuchokera kumalekezero a dziko lapansi tikumva kuyimba kotamanda

“Wolungamayo.”

Koma ine ndinati, “Ndatheratu, ndatheratu!

Tsoka kwa ine!

Anthu achinyengo akupitirizabe kuchita zachinyengo,

inde chinyengo chawo chikunkerankera mʼtsogolo.”

17Inu anthu adziko lapansi, zoopsa, dzenje

ndi msampha zikukudikirani.

18Aliyense wothawa phokoso la zoopsa

adzagwa mʼdzenje;

ndipo aliyense wotuluka mʼdzenjemo

adzakodwa ndi msampha.

Zitseko zakumwamba zatsekulidwa,

ndipo maziko a dziko lapansi agwedezeka.

19Dziko lapansi lathyokathyoka,

ndipo lagawika pakati,

dziko lapansi lagwedezeka kotheratu.

20Dziko lapansi likudzandira ngati munthu woledzera

likugwedezeka ndi mphepo ngati chisimba;

lalemedwa ndi machimo ake.

Lidzagwa ndipo silidzadzukanso.

21Tsiku limenelo Yehova adzalanga

amphamvu a kumwamba

ndiponso mafumu apansi pano.

22Mulungu adzawasonkhanitsa pamodzi

ngati amʼndende amene ali mʼdzenje.

Adzawatsekera mʼndende

ndipo adzalangidwa patapita nthawi yayitali.

23Mwezi udzanyazitsidwa, dzuwa lidzachita manyazi;

pakuti Yehova Wamphamvuzonse adzakhala mfumu ndipo adzalamulira;

pa Phiri la Ziyoni ndi ku Yerusalemu,

ndipo adzaonetsa ulemerero wake pamaso pa akuluakulu.

Bibelen på hverdagsdansk

Esajasʼ Bog 24:1-23

Guds dom over Israel og hele verden

1Hør efter! Herren gør jorden24,1 Eller: „Herren gør landet tomt og øde.” Teksten bruger et ord, som kan betyde landet, jorden eller verden. Det er ofte uklart, om der tænkes på Israels land, jorden eller hele verden. tom og øde. Han lægger Israels land øde og spreder dets indbyggere. 2Det går menigmand som præst, slave som herre, slavepige som frue, køber som sælger, udlåner som låner. Ikke en eneste undslipper. 3Landet bliver plyndret totalt og tømt. Det er Herrens ord.

4-5Befolkningen vil lide under følgen af deres synder. Jorden vrider sig i smerte, og afgrøderne visner, for himlen nægter at give regn. Landet er ødelagt af ondskab og forbrydelser. Folket har overtrådt Guds lov og brudt hans ubrydelige pagt. 6Derfor hænger Guds forbandelse over dem, og de må bære straffen for deres synd. Befolkningen svinder ind, og kun få vil overleve.

7Vinhøsten er slået fejl, vinen er brugt op og lystigheden vendt til sorg. 8Harpens melodiøse akkorder og tamburinens lystige rytmer er forstummet, al jubel er ophørt. 9Ingen vin kan inspirere til sang, og øllet smager bittert.

10Tomhedens by er brudt ned. Alle døre er låste og barrikaderede. 11Folk strejfer om i gaderne og råber på vin. Glæden er gået i sort, lystigheden forsvundet. 12Byen er ødelagt, dens porte slået ind. 13Som når man har slået oliven ned fra træets grene eller plukket druer i vinmarken, sådan bliver det blandt alle folkeslagene ud over jorden: kun en rest bliver tilbage.

14Men de, som er tilbage, skal råbe højt af glæde. I Vesten lovsynger de Guds storhed. 15-16I Østen skal lovsangen give ekko tilbage. Fjerne øer skal lovprise Herren, Israels Herre. Fra jordens ender synger de: „Æren er Guds, for han er retfærdig.”

Men mit hjerte er tungt af sorg, jeg holder det ikke ud. Ondskaben vinder stadig frem, troløshed ligger på lur overalt. 17Terror, ulykker og undertrykkelse rammer alle jordens folk. 18Undslipper I terror, vil I styrte i en faldgrube. Kravler I op af faldgruben, bliver I fanget i en fælde.

Straffen kommer ned fra himlen. Jorden ryster i sin grundvold. 19Den slår revner og bryder sammen, ryster og skælver. 20Verden vakler som en beruset, svajer som et faldefærdigt skur. Den segner under vægten af sin skyld og rejser sig ikke igen.

21Til den tid vil Herren straffe himlens åndemagter såvel som jordens stolte herskere. 22De bliver stuvet sammen som fanger og lænket i mørkets hule. Der må de vente til dommens dag. 23Fuldmånen vil skjule sit ansigt og solen gemme sig væk, for Herren, den Almægtige, skal regere fra Zions bjerg i Jerusalem, og hans folks ledere skal se hans herlighed.