Yesaya 20 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 20:1-6

Za Chilango cha Igupto ndi Kusi

1Mʼchaka chimene mkulu wankhondo wotumidwa ndi mfumu ya ku Asiriya, anabwera ku Asidodi ndi kuwuthira nkhondo ndi kuwulanda, 2nthawi imeneyo Yehova anawuza Yesaya mwana wa Amozi kuti, “Pita kavule chiguduli ndi nsapato zako.” Ndipo iye anaterodi, ankangoyenda wamaliseche ndiponso wopanda nsapato.

3Kenaka Yehova anati, “Monga momwe mtumiki wanga Yesaya wakhala akuyendera wamaliseche ndiponso wopanda nsapato kwa zaka zitatu ngati chizindikiro ndi chenjezo kwa dziko la Igupto ndi Kusi, 4momwemonso mfumu ya ku Asiriya idzatenga ukapolo anthu a ku Igupto ndi a ku Kusi, anyamata ndi okalamba. Iwo adzakhala amaliseche ndi opanda nsapato, matako ali pa mtunda. Zimenezi zidzachititsa manyazi Igupto. 5Amene ankadalira Kusi, ndiponso amene ankadzitukumula chifukwa cha Igupto adzakhumudwa ndi kuchita manyazi. 6Tsiku limenelo anthu amene amakhala mʼmbali mwa nyanja adzati, ‘Taonani zomwe zawachitikira amene ife tinkawadalira, amene ife tinkathawirako kuti atithandize ndi kutipulumutsa kwa mfumu ya ku Asiriya! Nanga ife tidzapulumuka bwanji?’ ”

La Bible du Semeur

Esaïe 20:1-6

Signe prophétique contre l’Egypte

1L’année où le généralissime envoyé par Sargon20.1 Sargon: roi d’Assyrie de 722 à 705 av. J.-C. C’est lui qui s’empara de Samarie et qui en déporta les habitants (2 R 17.6). Il s’est emparé d’Ashdod en 711 av. J.-C., roi d’Assyrie, vint attaquer Ashdod20.1 Ashdod: l’une des cinq villes principales de la Philistie (Jos 11.22 ; 15.46 ; 1 S 5.1)., et s’en empara, 2l’Eternel parla par l’intermédiaire d’Esaïe, fils d’Amots. Il dit : Va, détache l’habit de toile de sac qui couvre tes reins et retire tes sandales.

Le prophète obéit et se promena nu et déchaussé. 3L’Eternel dit alors : Mon serviteur Esaïe a marché nu et déchaussé pendant trois ans pour servir de signe et de présage au sujet de l’Egypte et de l’Ethiopie. 4Ainsi le roi d’Assyrie emmènera en déportation des captifs égyptiens et éthiopiens, des jeunes et des vieillards, nus et déchaussés et les reins découverts, à la honte de l’Egypte. 5Et tous ceux qui avaient mis leur confiance en l’Ethiopie et se faisaient une fierté de l’Egypte, seront terrifiés et couverts de honte. 6Les habitants de ces régions du littoral diront en ce jour-là : « Voilà à quoi en sont réduits ceux auprès de qui nous espérions nous réfugier pour trouver de l’aide et du secours contre le roi d’Assyrie. Et nous, maintenant, comment échapperons-nous ? »