Phiri la Yehova
1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:
2Mʼmasiku otsiriza,
phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,
lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,
“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,
ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,
ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
kapena kuphunziranso za nkhondo.
5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,
tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.
Tsiku la Yehova
6Inu Yehova mwawakana anthu anu,
nyumba ya Yakobo.
Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;
amawombeza mawula ngati Afilisti,
ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.
7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;
ndipo chuma chawo ndi chosatha.
Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;
ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.
8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;
iwo amapembedza ntchito ya manja awo,
amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.
9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa
ndi kutsitsidwa.
Inu Yehova musawakhululukire.
10Lowani mʼmatanthwe,
bisalani mʼmaenje,
kuthawa kuopsa kwa Yehova
ndi ulemerero wa ufumu wake!
11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,
ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.
12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku
limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,
ndipo adzagonjetsa
onse amphamvu,
13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,
ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,
14tsiku la mapiri onse ataliatali
ndiponso la zitunda zonse zazitali,
15tsiku la nsanja zonse zazitali
ndiponso malinga onse olimba,
16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi
ndiponso la mabwato onse okongola.
17Kudzikuza kwa munthu kudzatha
ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,
Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,
18ndipo mafano onse adzatheratu.
19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe
ndi mʼmaenje a nthaka,
kuthawa mkwiyo wa Yehova,
ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
20Tsiku limenelo anthu adzatayira
mfuko ndi mileme
mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,
amene anawapanga kuti aziwapembedza.
21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe
ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka
kuthawa mkwiyo wa Yehova
ndiponso ulemerero wa ufumu wake,
pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.
22Lekani kudalira munthu,
amene moyo wake sukhalira kutha.
Iye angathandize bwanji wina aliyense?
The Mountain of the Lord
1This is what Isaiah son of Amoz saw concerning Judah and Jerusalem:
2In the last days
the mountain of the Lord’s temple will be established
as the highest of the mountains;
it will be exalted above the hills,
and all nations will stream to it.
3Many peoples will come and say,
“Come, let us go up to the mountain of the Lord,
to the temple of the God of Jacob.
He will teach us his ways,
so that we may walk in his paths.”
The law will go out from Zion,
the word of the Lord from Jerusalem.
4He will judge between the nations
and will settle disputes for many peoples.
They will beat their swords into plowshares
and their spears into pruning hooks.
Nation will not take up sword against nation,
nor will they train for war anymore.
5Come, descendants of Jacob,
let us walk in the light of the Lord.
The Day of the Lord
6You, Lord, have abandoned your people,
the descendants of Jacob.
They are full of superstitions from the East;
they practice divination like the Philistines
and embrace pagan customs.
7Their land is full of silver and gold;
there is no end to their treasures.
Their land is full of horses;
there is no end to their chariots.
8Their land is full of idols;
they bow down to the work of their hands,
to what their fingers have made.
9So people will be brought low
and everyone humbled—
do not forgive them.2:9 Or not raise them up
10Go into the rocks, hide in the ground
from the fearful presence of the Lord
and the splendor of his majesty!
11The eyes of the arrogant will be humbled
and human pride brought low;
the Lord alone will be exalted in that day.
12The Lord Almighty has a day in store
for all the proud and lofty,
for all that is exalted
(and they will be humbled),
13for all the cedars of Lebanon, tall and lofty,
and all the oaks of Bashan,
14for all the towering mountains
and all the high hills,
15for every lofty tower
and every fortified wall,
16for every trading ship2:16 Hebrew every ship of Tarshish
and every stately vessel.
17The arrogance of man will be brought low
and human pride humbled;
the Lord alone will be exalted in that day,
18and the idols will totally disappear.
19People will flee to caves in the rocks
and to holes in the ground
from the fearful presence of the Lord
and the splendor of his majesty,
when he rises to shake the earth.
20In that day people will throw away
to the moles and bats
their idols of silver and idols of gold,
which they made to worship.
21They will flee to caverns in the rocks
and to the overhanging crags
from the fearful presence of the Lord
and the splendor of his majesty,
when he rises to shake the earth.
22Stop trusting in mere humans,
who have but a breath in their nostrils.
Why hold them in esteem?