Yesaya 2 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 2:1-22

Phiri la Yehova

1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

2Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,

lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,

tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

6Inu Yehova mwawakana anthu anu,

nyumba ya Yakobo.

Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;

amawombeza mawula ngati Afilisti,

ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.

7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;

ndipo chuma chawo ndi chosatha.

Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;

ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.

8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;

iwo amapembedza ntchito ya manja awo,

amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.

9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa

ndi kutsitsidwa.

Inu Yehova musawakhululukire.

10Lowani mʼmatanthwe,

bisalani mʼmaenje,

kuthawa kuopsa kwa Yehova

ndi ulemerero wa ufumu wake!

11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku

limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,

ndipo adzagonjetsa

onse amphamvu,

13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,

ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,

14tsiku la mapiri onse ataliatali

ndiponso la zitunda zonse zazitali,

15tsiku la nsanja zonse zazitali

ndiponso malinga onse olimba,

16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi

ndiponso la mabwato onse okongola.

17Kudzikuza kwa munthu kudzatha

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,

18ndipo mafano onse adzatheratu.

19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndi mʼmaenje a nthaka,

kuthawa mkwiyo wa Yehova,

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

20Tsiku limenelo anthu adzatayira

mfuko ndi mileme

mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,

amene anawapanga kuti aziwapembedza.

21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka

kuthawa mkwiyo wa Yehova

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22Lekani kudalira munthu,

amene moyo wake sukhalira kutha.

Iye angathandize bwanji wina aliyense?

Hoffnung für Alle

Jesaja 2:1-22

Jerusalem, der Mittelpunkt eines neuen Reiches

1In einer Vision empfing Jesaja, der Sohn von Amoz, diese Botschaft für Juda und Jerusalem:

2Am Ende der Zeit wird der Berg, auf dem der Tempel des Herrn steht, alle anderen Berge und Hügel weit überragen. Menschen aller Nationen strömen dann herbei. 3Viele Völker ziehen los und rufen einander zu: »Kommt, wir wollen auf den Berg des Herrn steigen, zum Tempel des Gottes Israels! Dort wird er uns seinen Weg zeigen, und wir werden lernen, so zu leben, wie er es will.«

Denn vom Berg Zion aus wird der Herr seine Weisungen geben, dort in Jerusalem wird er der ganzen Welt seinen Willen verkünden. 4Gott selbst schlichtet den Streit zwischen den Völkern, und den vielen Nationen spricht er Recht. Dann schmieden sie ihre Schwerter zu Pflugscharen um und ihre Speere zu Winzermessern. Kein Volk wird mehr das andere angreifen; niemand lernt mehr, Krieg zu führen.2,4 Vgl. Micha 4,1‒3.

5Kommt, ihr Nachkommen von Jakob, wir wollen schon jetzt mit dem Herrn leben. Er ist unser Licht!

Der schreckliche Gerichtstag Gottes

6Herr, du hast dich von deinem Volk Israel abgewandt, weil sie die heidnischen Bräuche aus dem Osten übernommen haben. Sie treiben Zauberei wie ihre Nachbarn im Westen, die Philister. Bedenkenlos haben sie sich anderen Völkern angepasst. 7Israel hat in jeder Hinsicht Überfluss: Das Land ist voll von Gold, Silber und anderen Schätzen; Pferde und Streitwagen sind in großer Zahl vorhanden. 8Doch auch mit Götzenstatuen ist das Land übersät. Vor selbst gemachten Figuren werfen die Menschen sich nieder und beten sie an. 9Verzeih ihnen das nicht! Du wirst jeden in die Knie zwingen, alle müssen sich vor dir beugen.

10Ja, versteckt euch in den Höhlen, kriecht in die Erdlöcher! Denn der Herr verbreitet Furcht und Schrecken, wenn er sich in seiner Pracht und Majestät zeigt. 11Es kommt der Tag, an dem der Hochmut der Menschen ein Ende hat und ihr Stolz gebrochen wird. Dann wird nur einer groß sein: der Herr! 12Der allmächtige Gott hat einen Tag bestimmt, an dem er über die stolzen und hochmütigen Menschen Gericht hält und sie erniedrigt. 13Alle hochgewachsenen Zedern auf dem Libanon und die mächtigen Eichen in der Baschan-Ebene wird er umhauen, 14jeden hohen Berg und Hügel einebnen, 15gewaltige Türme und feste Mauern einreißen; 16alle Handelsschiffe2,16 Wörtlich: Tarsis-Schiffe. – So wurden große Handelsschiffe bezeichnet, die in der Lage waren, die weite Strecke bis nach Tarsis (im heutigen Spanien) zu segeln. und prunkvollen Boote wird er versenken. 17-18So macht er den Hochmut der Menschen zunichte. Die stolzen Herren liegen dann im Staub, und mit den Götzen ist es aus und vorbei. An diesem Tag wird nur einer groß sein: der Herr!

19Wenn der Herr sich in seiner Pracht und Majestät zum Gericht erhebt und die Erde in Schrecken versetzt, fliehen seine Feinde voller Angst in die Felsenklüfte und verkriechen sich in Erdlöchern. 20Sie werfen ihre silbernen und goldenen Götzenfiguren, die sie mit viel Mühe angefertigt haben, achtlos den Ratten und Fledermäusen hin, 21um so schnell wie möglich in Felsspalten und Höhlen zu verschwinden. Angst und Grauen wird sie packen, wenn der Herr sich in seiner Pracht und Majestät erhebt, um Gericht zu halten. 22Hört endlich auf, euch auf Menschen zu verlassen! Sie vergehen wie ein Lufthauch. Was kann man schon von ihnen erwarten?