Yesaya 2 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 2:1-22

Phiri la Yehova

1Nazi zinthu zokhudza Yuda ndi Yerusalemu, zimene Yesaya mwana wa Amozi anaziona mʼmasomphenya:

2Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,

lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.

3Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

4Iye adzaweruza pakati pa mayiko,

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

5Inu nyumba ya Yakobo, bwerani,

tiyeni tiyende mʼkuwala kwa Yehova.

Tsiku la Yehova

6Inu Yehova mwawakana anthu anu,

nyumba ya Yakobo.

Iwo adzaza ndi zamatsenga zochokera Kummawa;

amawombeza mawula ngati Afilisti,

ndipo amayanjana ndi anthu osapembedza Mulungu.

7Dziko lawo ndi lodzaza ndi siliva ndi golide;

ndipo chuma chawo ndi chosatha.

Dziko lawo ndi lodzaza ndi akavalo;

ndipo magaleta awo ankhondo ngosawerengeka.

8Dziko lawo ndi lodzaza ndi mafano;

iwo amapembedza ntchito ya manja awo,

amagwadira zomwe anapanga ndi zala zawo.

9Tsono munthu aliyense adzachepetsedwa

ndi kutsitsidwa.

Inu Yehova musawakhululukire.

10Lowani mʼmatanthwe,

bisalani mʼmaenje,

kuthawa kuopsa kwa Yehova

ndi ulemerero wa ufumu wake!

11Kudzikuza kwa anthu kudzatha,

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa;

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu pa tsiku limenelo.

12Yehova Wamphamvuzonse wakonzeratu tsiku

limene adzatsitse onse onyada ndi odzitama,

ndipo adzagonjetsa

onse amphamvu,

13tsiku la mikungudza yonse ya ku Lebanoni, yayitali ndi yoonekera patali,

ndiponso la mitengo yonse ya thundu ya ku Basani,

14tsiku la mapiri onse ataliatali

ndiponso la zitunda zonse zazitali,

15tsiku la nsanja zonse zazitali

ndiponso malinga onse olimba,

16tsiku la sitima zapamadzi zonse za ku Tarisisi

ndiponso la mabwato onse okongola.

17Kudzikuza kwa munthu kudzatha

ndipo kudzitama kwa anthu kudzawonongedwa,

Yehova yekha ndiye adzapatsidwe ulemu tsiku limenelo,

18ndipo mafano onse adzatheratu.

19Anthu adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndi mʼmaenje a nthaka,

kuthawa mkwiyo wa Yehova,

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

20Tsiku limenelo anthu adzatayira

mfuko ndi mileme

mafano awo asiliva ndi mafano awo agolide,

amene anawapanga kuti aziwapembedza.

21Adzathawira mʼmapanga a matanthwe

ndiponso mʼmingʼalu ya nthaka

kuthawa mkwiyo wa Yehova

ndiponso ulemerero wa ufumu wake,

pamene Iye adzuka kugwedeza dziko lapansi.

22Lekani kudalira munthu,

amene moyo wake sukhalira kutha.

Iye angathandize bwanji wina aliyense?

La Bible du Semeur

Esaïe 2:1-22

Le mont de l’Eternel

1Voici le message que Dieu a révélé à Esaïe, fils d’Amots, au sujet de Juda et de Jérusalem.

2Dans l’avenir, il adviendra

que le mont ╵sur lequel est le temple ╵de l’Eternel2.2 C’est-à-dire le mont Sion.

sera fermement établi ╵au-dessus des montagnes,

et il s’élèvera ╵par-dessus toutes les hauteurs,

et tous les peuples étrangers ╵y afflueront2.2 Les v. 2-4 sont repris en Mi 4.2-4..

3Oui, de nombreux peuples viendront,

en se disant les uns aux autres :

« Venez, montons ╵au mont de l’Eternel,

au temple du Dieu de Jacob !

Il nous enseignera ╵les voies qu’il a prescrites ;

nous suivrons ses sentiers. »

Car de Sion viendra la Loi,

et de Jérusalem, ╵la Parole de l’Eternel.

4Et il sera l’arbitre ╵entre les nations ;

oui, il sera le juge ╵de nombreux peuples.

Martelant leurs épées, ╵ils forgeront des socs ╵pour leurs charrues,

et, de leurs lances, ╵ils feront des faucilles2.4 Voir Jl 4.10..

Plus aucune nation ╵ne brandira l’épée ╵contre une autre nation,

et l’on n’apprendra plus la guerre.

5Descendants de Jacob,

venez donc et marchons ╵à la lumière ╵de l’Eternel.

6Tu as abandonné ton peuple, ╵la communauté de Jacob,

car il est envahi ╵par les superstitions ╵qui viennent de l’Orient ;

les devins y pullulent ╵autant qu’en Philistie.

On pactise avec l’étranger.

7Le pays est rempli ╵d’argent et d’or

et de trésors sans fin.

Il est plein de chevaux,

et ses chars de combat ╵ne peuvent se compter.

8Le pays est rempli d’idoles

et les gens se prosternent

devant leurs propres œuvres

fabriquées de leurs mains.

9Mais les hommes s’inclineront,

ils seront humiliés.

Ne leur pardonne pas2.9 Autre traduction : ne les relève pas. !

10Réfugiez-vous dans les rochers

et cachez-vous sous terre

à cause des terreurs ╵que l’Eternel provoque,

de l’éclat de sa majesté2.10 Voir Ap 6.15..

11L’homme au regard hautain ╵devra baisser les yeux,

l’orgueil humain sera brisé,

car en ce jour-là, l’Eternel ╵sera seul honoré.

12Car l’Eternel, ╵le Seigneur des armées célestes, ╵tient en réserve un jour

où il se dressera ╵contre tous les hautains, ╵les arrogants,

les orgueilleux, ╵pour qu’ils soient abaissés ;

13contre les cèdres du Liban, ╵qui s’élèvent bien haut,

et contre tous les chênes ╵des plateaux du Basan2.13 Région à l’est du Jourdain et au nord de Galaad, réputée pour ses chênes (Ez 27.6) et ses troupeaux (Ez 39.18).,

14et contre les hautes montagnes

et contre les collines ╵qui sont altières,

15contre toutes les tours ╵qui sont très élevées

et toutes les murailles ╵qui sont fortifiées,

16contre les vaisseaux au long cours2.16 Voir 1 R 10.22 et note.

et leurs denrées précieuses2.16 Autre traduction : contre les navires somptueux. :

17il courbera ╵la fierté des humains

et il abaissera ╵l’orgueil humain.

Car, en ce jour-là, l’Eternel ╵sera seul honoré.

18Et toutes les idoles ╵disparaîtront ensemble.

19On se réfugiera ╵dans les cavernes des rochers

et dans les antres de la terre

à cause des terreurs ╵que l’Eternel provoque,

de l’éclat de sa majesté

quand il se lèvera ╵pour terrifier la terre.

20En ce jour-là,

les hommes jetteront aux taupes

et aux chauves-souris

les idoles d’argent

et les idoles d’or

qu’ils se sont fabriquées ╵pour se prosterner devant elles.

21Ils se réfugieront ╵dans les cavernes

et dans les fentes des rochers

à cause des terreurs ╵que l’Eternel provoque,

de l’éclat de sa majesté

quand il se lèvera ╵pour terrifier la terre.

22C’est pourquoi, cessez donc ╵de vous confier en l’homme

dont la vie ne tient qu’à un souffle,

car, quelle est sa valeur ?