Yesaya 18 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 18:1-7

Za Kulangidwa kwa Kusi

1Tsoka kwa anthu a ku Kusi.

Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.

2Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo,

mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi,

ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro,

kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala,

ndi woopedwa ndi anthu.

Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena.

Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”

3Inu nonse anthu a pa dziko lonse,

inu amene mumakhala pa dziko lapansi,

pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri

yangʼanani,

ndipo pamene lipenga lilira

mumvere.

4Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti,

“Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana,

monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha,

monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”

5Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka

ndiponso mphesa zitayamba kupsa,

Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira,

ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.

6Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama

ndiponso zirombo zakuthengo;

mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe,

ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.

7Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse,

zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala,

kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe,

mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo,

anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.

Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.

Nova Versão Internacional

Isaías 18:1-7

Profecia contra a Etiópia

1Ai da terra do zumbido de insetos18.1 Ou gafanhotos

ao longo dos rios da Etiópia18.1 Hebraico: de Cuxe.,

2que manda emissários pelo mar

em barcos de papiro sobre as águas.

Vão, ágeis mensageiros,

a um povo alto e de pele macia,

a um povo temido pelos que estão perto

e pelos que estão longe,

nação agressiva e de fala estranha,

cuja terra é dividida por rios.

3Todos vocês, habitantes do mundo,

vocês que vivem na terra,

quando a bandeira for erguida

sobre os montes, vocês a verão,

e, quando soar a trombeta,

vocês a ouvirão.

4Assim diz o Senhor:

“Do lugar onde moro ficarei olhando, quieto

como o ardor do sol reluzente,

como a nuvem de orvalho no calor do tempo da colheita”.

5Pois, antes da colheita, quando a floração der lugar ao fruto

e as uvas amadurecerem,

ele cortará os brotos com a podadeira

e tirará os ramos longos.

6Serão todos entregues aos abutres das montanhas

e aos animais selvagens;

as aves se alimentarão deles todo o verão,

e os animais selvagens, todo o inverno.

7Naquela ocasião, dádivas serão trazidas ao Senhor dos Exércitos

da parte de um povo alto e de pele macia,

da parte de um povo temido pelos que estão perto

e pelos que estão longe,

nação agressiva e de fala estranha,

cuja terra é dividida por rios.

As dádivas serão trazidas ao monte Sião, ao local do nome do Senhor dos Exércitos.