Yesaya 17 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.

Nova Versão Internacional

Isaías 17:1-14

Mensagem contra Damasco

1Advertência contra Damasco:

Damasco deixará de ser cidade;

vai se tornar um monte de ruínas.

2Suas cidades serão abandonadas;

serão entregues aos rebanhos que ali se deitarão,

e ninguém os espantará.

3Efraim deixará de ser uma fortaleza,

e Damasco uma realeza;

o remanescente de Arã será

como a glória dos israelitas,

anuncia o Senhor dos Exércitos.

4Naquele dia, a glória de Jacó se definhará,

e a gordura do seu corpo se consumirá.

5Será como quando um ceifeiro junta o trigo

e colhe as espigas com o braço,

como quando se apanham os feixes de trigo

no vale de Refaim.

6Contudo, restarão algumas espigas,

como, quando se sacode uma oliveira,

ficam duas ou três azeitonas nos galhos mais altos

e umas quatro ou cinco nos ramos mais produtivos,

anuncia o Senhor, o Deus de Israel.

7Naquele dia, os homens olharão para aquele que os fez

e voltarão os olhos para o Santo de Israel.

8Não olharão para os altares,

obra de suas mãos,

e não darão a mínima atenção aos postes sagrados

e aos altares de incenso que os seus dedos fizeram.

9Naquele dia, as suas cidades fortes, que tinham sido abandonadas por causa dos israelitas, serão como lugares entregues aos bosques e ao mato. E tudo será desolação.

10Porque vocês se esqueceram de Deus, do seu Salvador,

e não se lembraram da Rocha, da fortaleza de vocês.

Por isso, embora vocês cultivem as melhores plantas,

videiras importadas,

11as façam crescer no dia em que as semearem

e as façam florescer de manhã,

não haverá colheita

no dia da tristeza e do mal irremediável.

12Ah! O bramido das numerosas nações;

bramam como o mar!

Ah, o rugido dos povos;

rugem como águas impetuosas!

13Embora os povos rujam como ondas encapeladas,

quando ele os repreender, fugirão para longe,

carregados pelo vento como palha nas colinas,

como galhos arrancados pela ventania.

14Ao cair da tarde, pavor repentino!

Antes do amanhecer, já se foram!

Esse é o destino dos que nos saqueiam,

essa é a parte que caberá aos que roubam.