Uthenga Wotsutsa Damasiko
1Uthenga wonena za Damasiko:
“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,
koma udzasanduka bwinja.
2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu
ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi
popanda wina woziopseza.
3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,
ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;
Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu
monga anthu a ku Israeli,”
akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;
ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.
5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu
umene anatsiriza kukolola.
Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu
anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.
6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale
monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni
kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi
mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”
akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.
7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo
ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.
8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,
ntchito ya manja awo,
ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,
ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.
9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.
10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;
simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.
Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,
ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,
11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo
ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,
komabe zimenezi sizidzakupindulirani
pa tsiku la mavuto.
12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,
akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!
Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,
akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!
13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,
koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.
Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,
ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.
14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,
ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.
Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,
gawo la amene amatibera zinthu zathu.
Syrien und Israel werden in Trümmern liegen
1Dies ist Gottes Botschaft über Damaskus: »Die Stadt Damaskus wird verschwinden, nur ein Trümmerhaufen bleibt von ihr übrig. 2Auch Aroër und die Städte in der Nähe liegen dann verlassen da. Friedlich weiden Schafe und Ziegen zwischen den Ruinen, niemand jagt sie weg. 3Auch das Nordreich Israel wird seine starken Befestigungen verlieren, und das Königreich von Damaskus wird verschwinden. Die überlebenden Syrer trifft das gleiche Schicksal wie die Israeliten: Von ihrem früheren Glanz bleibt nicht viel. Darauf gebe ich, der Herr, der allmächtige Gott, mein Wort.
4Es kommt der Tag, da wird die Pracht der Nachkommen von Jakob gänzlich verblassen. Israels fetter Leib magert bis auf die Knochen ab. 5Dann gleicht es den Weizenfeldern in der Refaïm-Ebene: In der Erntezeit fasst man die Ähren mit der Hand, mäht sie ab und sammelt zuletzt noch ein, was am Boden liegt. 6Doch ein kleiner Rest des Volkes wird übrig bleiben, so wie die wenigen Oliven, die nach der Ernte noch am Baum hängen. Zwei oder drei bleiben oben im Wipfel zurück und vielleicht noch einige unter den Blättern. Das verspreche ich, der Herr, der Gott Israels.
7Dann endlich werden die Menschen wieder an mich, ihren Schöpfer, denken und ihren Blick wieder auf den heiligen Gott Israels richten. 8Ihre selbst gemachten Altäre würdigen sie keines Blickes. Sie verehren keine heiligen Pfähle mehr und verbrennen keinen Weihrauch zu Ehren fremder Götter.
9Es kommt eine Zeit, in der die befestigten Städte der Israeliten verlassen daliegen. Sie gleichen den ausgestorbenen Dörfern in den Wäldern und auf den Bergen, die von den Bewohnern des Landes einst aus Angst vor den Israeliten verlassen wurden. Das Land wird zur Einöde, 10weil du, Volk Israel, mich, deinen Gott, der dich rettet, vergessen hast. Du hast keinen Gedanken mehr übrig für deinen Gott, der dich schützt wie ein mächtiger Fels. Nein, du legst lieber schöne Gärten für andere Götter an und bepflanzt sie mit exotischen Reben. 11Du zäunst sie sorgfältig ein und bringst sie noch am selben Morgen zum Blühen. Doch das alles hilft dir nichts! Wenn du glaubst, die Früchte deiner Mühen einsammeln zu können, wirst du nur tiefe Wunden und unsägliches Leid ernten.«
Vergeblicher Ansturm der Völker
12Hört ihr den Lärm? Ganze Völkermassen kommen auf uns zu, riesige Heere stürmen heran! Es klingt wie das Brausen gewaltiger Meereswogen, 13wie das Donnern wütender Wellen in sturmgepeitschter See. Doch Gott bringt sie zum Schweigen. Nur ein Wort – und sie suchen das Weite. Sie werden auseinandergejagt wie Spreu, die der Wind davonbläst, wie dürres Laub, das der Sturm vor sich herwirbelt. 14Am Abend sind wir alle noch vor Schreck wie gelähmt, doch bevor der Morgen graut, gibt es die Feinde nicht mehr. So geht es allen, die uns überfallen und ausplündern wollen! Sie werden keinen Erfolg haben!