Yesaya 16 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 16:1-14

1Anthu a ku Mowabu

atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa,

kuchokera ku Sela kudutsa chipululu

mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.

2Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku

akazimwaza mʼchisa,

momwemonso akazi a ku Mowabu

akuyendayenda ku madooko a Arinoni.

3Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti,

“Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite.

Inu mutiteteze kwa adani anthu.

Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo.

Mutibise,

musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.

4Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu;

mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.”

Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso,

kuwononga kudzaleka;

waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.

5Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi;

mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika.

Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo

ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.

6Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri.

Kunyada kwawo

ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo,

zonse ndi zopanda phindu.

7Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri;

iwo akulirira dziko lawo.

Akubuma momvetsa chisoni

chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.

8Minda ya ku Hesiboni yauma,

minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga.

Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda

minda ya mpesa wabwino,

imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri,

mpaka kutambalalira ku chipululu.

Mizu yake inakafika

mpaka ku tsidya la nyanja.

9Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri,

chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima.

Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali,

ndikukunyowetsani ndi misozi!

Mwalephera kupeza zokolola,

chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.

10Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso;

palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa;

palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa,

pakuti ndathetsa kufuwula.

11Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu,

mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.

12Ngakhale anthu a ku Mowabu

apite ku malo awo achipembedzo

koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe

chifukwa sizidzatheka.

13Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu. 14Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

Thai New Contemporary Bible

อิสยาห์ 16:1-14

1จงส่งลูกแกะมาเป็นเครื่องบรรณาการ

แด่ผู้ครอบครองดินแดน

ส่งมาจากเสลา ข้ามถิ่นกันดาร

มายังภูเขาของธิดาแห่งศิโยน16:1 คือ ชาวเยรูซาเล็ม

2บรรดาผู้หญิงของโมอับ

ถูกปล่อยไว้ริมตลิ่งของแม่น้ำอารโนน

เหมือนนกกระพือปีก

ซึ่งถูกผลักจากรัง

3“โปรดให้คำปรึกษา

และช่วยตัดสินใจ

ในยามเที่ยงวันโปรดให้ร่มเงา

ดั่งยามค่ำคืน

โปรดให้ที่ซ่อนแก่ผู้หนีภัย

อย่าทรยศหักหลังผู้ลี้ภัย

4ขอให้ผู้ลี้ภัยชาวโมอับพักอยู่กับท่าน

ขอเป็นที่พักพิงให้พวกเขาพ้นจากผู้ทำลาย”

ผู้กดขี่จะถึงจุดจบ

และความพินาศย่อยยับจะยุติลง

ผู้กดขี่ข่มเหงจะหมดสิ้นไปจากดินแดน

5ราชบัลลังก์หนึ่งจะได้รับการสถาปนาขึ้นด้วยความรัก

ผู้หนึ่งจากวงศ์วานของดาวิด

จะนั่งบนบัลลังก์นั้นด้วยความซื่อสัตย์

เป็นผู้ตัดสินอย่างยุติธรรม

และส่งเสริมความชอบธรรม

6เราได้ยินถึงความหยิ่งทะนงของโมอับ

ความอวดดี ความจองหอง

ความเย่อหยิ่ง และความโอหัง

แต่คำโอ้อวดของโมอับก็ว่างเปล่า

7ฉะนั้นชาวโมอับจึงพากันร่ำไห้ให้กับแผ่นดินโมอับ

และร้องไห้คร่ำครวญให้แก่ผู้คน16:7 หรือขนมลูกเกดเป็นการเล่นคำของคีร์หะเรเสท

8ท้องทุ่งแห่งเฮชโบนก็เหี่ยวเฉา

เช่นเดียวกับเถาองุ่นของสิบมาห์

บรรดาผู้ครอบครองชาติต่างๆ

ได้เหยียบย่ำเถาองุ่นที่ดีที่สุด

ซึ่งครั้งหนึ่งเคยงอกงามไปถึงยาเซอร์

แพร่ขยายไปถึงถิ่นกันดาร

แตกหน่อผลิผล

ไปไกลถึงทะเล

9ฉะนั้นเราจึงร่ำไห้เหมือนที่ยาเซอร์ร่ำไห้

ให้กับเถาองุ่นแห่งสิบมาห์

เฮชโบนเอ๋ย เอเลอาเลห์เอ๋ย

เราหลั่งน้ำตาให้เจ้าจนเปียกชุ่ม!

เสียงโห่ร้องยินดีเมื่อรวบรวมผลไม้สุกงอม

และเมื่อเก็บเกี่ยวพืชพันธุ์ธัญญาหารของเจ้านั้นก็เงียบไปแล้ว

10ความรื่นเริงยินดีสูญสิ้นไปจากสวนผลไม้

ไม่มีใครร้องเพลงหรือโห่ร้องในไร่องุ่น

ไม่มีใครย่ำองุ่นที่บ่อย่ำเหล้าองุ่นอีกต่อไป

เพราะเราได้ยุติเสียงโห่ร้องนั้นแล้ว

11ดวงใจของเราคร่ำครวญเพื่อโมอับดั่งเสียงพิณ

ส่วนลึกของจิตใจอาลัยคีร์หะเรเสท

12เมื่อโมอับขึ้นไปยังสถานบูชาบนที่สูง

ก็เหนื่อยเปล่า

เมื่อขึ้นไปสวดวิงวอนที่เทวสถาน

ก็เปล่าประโยชน์

13องค์พระผู้เป็นเจ้าได้ตรัสเกี่ยวกับโมอับไว้เช่นนี้แหละ 14บัดนี้องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสว่า “ภายในสามปี ตามปีของสัญญาว่าจ้างแรงงาน ความโอ่อ่าตระการและประชากรทั้งปวงของโมอับจะถูกเหยียดลง และผู้ที่รอดชีวิตอยู่ก็มีน้อยคนและอ่อนระโหยโรยแรง”