Yesaya 16 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 16:1-14

1Anthu a ku Mowabu

atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa,

kuchokera ku Sela kudutsa chipululu

mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.

2Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku

akazimwaza mʼchisa,

momwemonso akazi a ku Mowabu

akuyendayenda ku madooko a Arinoni.

3Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti,

“Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite.

Inu mutiteteze kwa adani anthu.

Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo.

Mutibise,

musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.

4Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu;

mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.”

Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso,

kuwononga kudzaleka;

waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.

5Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi;

mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika.

Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo

ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.

6Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri.

Kunyada kwawo

ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo,

zonse ndi zopanda phindu.

7Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri;

iwo akulirira dziko lawo.

Akubuma momvetsa chisoni

chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.

8Minda ya ku Hesiboni yauma,

minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga.

Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda

minda ya mpesa wabwino,

imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri,

mpaka kutambalalira ku chipululu.

Mizu yake inakafika

mpaka ku tsidya la nyanja.

9Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri,

chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima.

Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali,

ndikukunyowetsani ndi misozi!

Mwalephera kupeza zokolola,

chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.

10Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso;

palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa;

palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa,

pakuti ndathetsa kufuwula.

11Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu,

mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.

12Ngakhale anthu a ku Mowabu

apite ku malo awo achipembedzo

koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe

chifukwa sizidzatheka.

13Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu. 14Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

King James Version

Isaiah 16:1-14

1Send ye the lamb to the ruler of the land from Sela to the wilderness, unto the mount of the daughter of Zion.16.1 Sela: or, Petra: Heb. A rock 2For it shall be, that, as a wandering bird cast out of the nest, so the daughters of Moab shall be at the fords of Arnon.16.2 cast…: or, a nest forsaken 3Take counsel, execute judgment; make thy shadow as the night in the midst of the noonday; hide the outcasts; bewray not him that wandereth.16.3 Take: Heb. Bring 4Let mine outcasts dwell with thee, Moab; be thou a covert to them from the face of the spoiler: for the extortioner is at an end, the spoiler ceaseth, the oppressors are consumed out of the land.16.4 extortioner: Heb. wringer16.4 the oppressors: Heb. the treaders down 5And in mercy shall the throne be established: and he shall sit upon it in truth in the tabernacle of David, judging, and seeking judgment, and hasting righteousness.16.5 established: or, prepared

6¶ We have heard of the pride of Moab; he is very proud: even of his haughtiness, and his pride, and his wrath: but his lies shall not be so. 7Therefore shall Moab howl for Moab, every one shall howl: for the foundations of Kir-hareseth shall ye mourn; surely they are stricken.16.7 mourn: or, mutter 8For the fields of Heshbon languish, and the vine of Sibmah: the lords of the heathen have broken down the principal plants thereof, they are come even unto Jazer, they wandered through the wilderness: her branches are stretched out, they are gone over the sea.16.8 stretched…: or, plucked up

9¶ Therefore I will bewail with the weeping of Jazer the vine of Sibmah: I will water thee with my tears, O Heshbon, and Elealeh: for the shouting for thy summer fruits and for thy harvest is fallen.16.9 the shouting…: or, the alarm is fallen upon, etc 10And gladness is taken away, and joy out of the plentiful field; and in the vineyards there shall be no singing, neither shall there be shouting: the treaders shall tread out no wine in their presses; I have made their vintage shouting to cease. 11Wherefore my bowels shall sound like an harp for Moab, and mine inward parts for Kir-haresh.

12¶ And it shall come to pass, when it is seen that Moab is weary on the high place, that he shall come to his sanctuary to pray; but he shall not prevail. 13This is the word that the LORD hath spoken concerning Moab since that time. 14But now the LORD hath spoken, saying, Within three years, as the years of an hireling, and the glory of Moab shall be contemned, with all that great multitude; and the remnant shall be very small and feeble.16.14 feeble: or, not many