Yesaya 16 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 16:1-14

1Anthu a ku Mowabu

atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa,

kuchokera ku Sela kudutsa chipululu

mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.

2Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku

akazimwaza mʼchisa,

momwemonso akazi a ku Mowabu

akuyendayenda ku madooko a Arinoni.

3Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti,

“Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite.

Inu mutiteteze kwa adani anthu.

Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo.

Mutibise,

musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.

4Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu;

mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.”

Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso,

kuwononga kudzaleka;

waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.

5Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi;

mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika.

Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo

ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.

6Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri.

Kunyada kwawo

ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo,

zonse ndi zopanda phindu.

7Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri;

iwo akulirira dziko lawo.

Akubuma momvetsa chisoni

chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.

8Minda ya ku Hesiboni yauma,

minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga.

Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda

minda ya mpesa wabwino,

imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri,

mpaka kutambalalira ku chipululu.

Mizu yake inakafika

mpaka ku tsidya la nyanja.

9Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri,

chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima.

Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali,

ndikukunyowetsani ndi misozi!

Mwalephera kupeza zokolola,

chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.

10Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso;

palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa;

palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa,

pakuti ndathetsa kufuwula.

11Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu,

mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.

12Ngakhale anthu a ku Mowabu

apite ku malo awo achipembedzo

koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe

chifukwa sizidzatheka.

13Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu. 14Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 16:1-14

1摩押人从西拉穿过旷野,来到锡安城的山,

把羊羔献给那里的掌权者。

2亚嫩河渡口,

摩押16:2 摩押人”希伯来文是“摩押的女子”。如同被赶离巢穴的飞鸟。

3他们对犹大人说:“给我们出个主意,伸张正义吧!

请让你们的影子在正午如黑夜,

遮盖逃难的人,

不要出卖逃亡者。

4让我们这些逃难的摩押人留在你们那里,

好躲避毁灭者。”

欺压和毁灭之事终必停止,

入侵者终必从地上消失。

5那时,必有一个宝座在爱中坚立,

大卫家的人必坐在上面以信实治国,

秉公审判,速行公义。

6我们听说摩押人心骄气傲、狂妄自大,

然而他们所夸耀的都是虚假的。

7他们必为摩押哀哭,

人人都必哀哭,

为不再有吉珥·哈列设的美味葡萄饼而哀叹、悲伤。

8因为希实本的农田荒废,

西比玛的葡萄树枯萎。

各国的君王都来践踏这些上好的葡萄树。

它们的枝子曾经伸展到雅谢和旷野,

嫩枝一直蔓延到海。

9因此,我像雅谢人一样为西比玛的葡萄树哀哭。

希实本以利亚利啊,

我用眼泪来浇灌你们,

因为再无人为你们的果品和庄稼而欢呼了。

10肥美的田园里听不到快乐的声音,

葡萄园里也无人歌唱欢呼,

榨酒池里无人榨酒。

我已经使欢呼声止息。

11我的内心为摩押

吉珥·哈列设哀鸣,

好像凄凉的琴声。

12摩押人上丘坛祭拜,

却落得筋疲力尽;

在庙宇里祷告,

却毫无用处。

13以上是耶和华所说有关摩押的预言。 14现在,耶和华说:“正如一个雇工的工作年限是三年,摩押的荣耀也必在三年之内消失,那里的人民必遭藐视,残存的人必寥寥无几、软弱无力。”