Yesaya 15 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 15:1-9

Za Kulangidwa kwa Mowabu

1Uthenga wonena za Mowabu:

Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

Mzinda wa Kiri wawonongedwa,

wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.

2Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo,

akupita ku malo awo achipembedzo kukalira;

anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba.

Mutu uliwonse wametedwa mpala,

ndipo ndevu zonse zametedwa.

3Mʼmisewu akuvala ziguduli;

pa madenga ndi mʼmabwalo

aliyense akulira mofuwula,

misozi ili pupupu.

4Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula,

mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi.

Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula,

ndipo ataya mtima.

5Inenso ndikulirira Mowabu;

chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari

ndi Egilati-Selisiya

akupita akulira ku chikweza cha Luhiti,

Akulira mosweka mtima

pa njira yopita ku Horonaimu;

akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.

6Madzi a ku Nimurimu aphwa

ndipo udzu wauma;

zomera zawonongeka

ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.

7Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga,

achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.

8Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu;

kulira kwawo kosweka mtima kukumveka

mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.

9Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi,

komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni,

mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu

ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

New International Version

Isaiah 15:1-9

A Prophecy Against Moab

1A prophecy against Moab:

Ar in Moab is ruined,

destroyed in a night!

Kir in Moab is ruined,

destroyed in a night!

2Dibon goes up to its temple,

to its high places to weep;

Moab wails over Nebo and Medeba.

Every head is shaved

and every beard cut off.

3In the streets they wear sackcloth;

on the roofs and in the public squares

they all wail,

prostrate with weeping.

4Heshbon and Elealeh cry out,

their voices are heard all the way to Jahaz.

Therefore the armed men of Moab cry out,

and their hearts are faint.

5My heart cries out over Moab;

her fugitives flee as far as Zoar,

as far as Eglath Shelishiyah.

They go up the hill to Luhith,

weeping as they go;

on the road to Horonaim

they lament their destruction.

6The waters of Nimrim are dried up

and the grass is withered;

the vegetation is gone

and nothing green is left.

7So the wealth they have acquired and stored up

they carry away over the Ravine of the Poplars.

8Their outcry echoes along the border of Moab;

their wailing reaches as far as Eglaim,

their lamentation as far as Beer Elim.

9The waters of Dimon15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood. are full of blood,

but I will bring still more upon Dimon15:9 Dimon, a wordplay on Dibon (see verse 2), sounds like the Hebrew for blood.

a lion upon the fugitives of Moab

and upon those who remain in the land.